历代志下 14 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

历代志下 14:1-15

亚撒王击败古实人

1亚比雅与祖先同眠后,葬在大卫城中,他儿子亚撒继位。亚撒执政期间,国中太平十年。 2亚撒做他的上帝耶和华看为好、视为正的事, 3拆除外族神明的丘坛和神庙,打碎神柱,砍倒亚舍拉神像, 4命令犹大人寻求他们祖先的上帝耶和华,遵行祂的律法和诫命。 5他除掉犹大各城邑的丘坛和香坛,那时国中太平。 6他还在犹大修筑坚城,那些年国中太平,没有战事,因为耶和华赐他平安。 7他对犹大人说:“我们要修筑城邑,在四周建造城墙和望楼,装置大门和门闩。我们仍拥有这片土地,是因为我们寻求我们的上帝耶和华;我们寻求祂,祂就赐我们四境平安。”于是,他们修筑城邑,凡事顺利。 8亚撒的军队中有三十万持大盾牌和矛枪的犹大人,二十八万持小盾牌和弓箭的便雅悯人。他们都是英勇的战士。

9古实谢拉率领一百万大军和三百辆战车攻打犹大,到了玛利沙10亚撒出兵迎敌,双方在玛利沙洗法谷摆开阵势。 11亚撒呼求他的上帝耶和华说:“耶和华啊,唯有你才能帮助弱小的胜过强大的。我们的上帝耶和华啊,求你帮助我们,因为我们依靠你,奉你的名迎战这大军。耶和华啊,你是我们的上帝,不要让人胜过你。”

12于是,耶和华使古实人败在亚撒犹大人面前,古实人溃逃。 13亚撒率领军队乘胜追击,直追到基拉耳古实人在耶和华和祂的军兵面前大败,伤亡惨重,一蹶不振。犹大人掳走了许多财物, 14攻陷了基拉耳四周的城邑,因为这些城里的人都惧怕耶和华。他们洗劫各城,因为城中有大量财物。 15他们毁坏牲畜的围栏,抢走许多羊和骆驼,然后返回耶路撒冷

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Mbiri 14:1-15

1Tsono Abiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide. Asa mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake ndipo pa masiku ake, dziko linakhala pa mtendere kwa zaka khumi.

Asa Mfumu ya Yuda

2Asa anachita zabwino ndi zolungama pamaso pa Yehova Mulungu wake. 3Iye anachotsa maguwa achilendo ndi malo opembedzerapo mafano, anaphwanya zipilala za miyala yachipembedzo ndi kugwetsa mafano a Asera. 4Asa analamula Yuda kuti afunefune Yehova Mulungu wa makolo awo ndi kumvera malamulo ndi zolamulira zake. 5Iye anachotsa malo opembedzera mafano ndi maguwa ofukizira lubani mu mzinda uliwonse wa mu Yuda, ndipo mu ufumu wake munali mtendere pa nthawi ya ulamuliro wake. 6Asa anamanga mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda pakuti dziko linali pa mtendere. Panalibe amene anachita naye nkhondo mʼzaka zimenezo, pakuti Yehova anamupatsa mpumulo.

7Iye anati kwa Yuda “Tiyeni timange mizinda iyi ndipo timange makoma ndi nsanja, zitseko ndi zotchinga. Dzikoli likanali lathu chifukwa tafuna Yehova Mulungu wathu; tinamufuna Iye ndipo watipatsa mpumulo mbali zonse.” Kotero iwo anamanga ndi kukhala pa ulemerero.

8Asa anali ndi ankhondo 300,000 ochokera ku Yuda, okhala ndi zishango zikuluzikulu ndi mikondo, ndiponso ankhondo 280,000 ochokera ku Benjamini, okhala ndi zishango ndi mauta. Onsewa anali ankhondo amphamvu ndi olimba mtima.

9Zera wa ku Kusi anapita kukamenyana nawo ali ndi gulu lalikulu kwambiri la asilikali ndi magaleta 300 ndipo anafika mpaka ku Maresa. 10Asa anapita kukakumana naye ndipo anakhala pa mizere yawo ya nkhondo mʼchigwa cha Zefata pafupi ndi Maresa.

11Kenaka Asa anafuwulira Yehova Mulungu wake ndipo anati “Yehova palibe wina wofanana nanu kuti angathandize anthu opanda mphamvu pakati pa amphamvu. Tithandizeni Inu Yehova Mulungu wathu pakuti ife timadalira Inu ndipo mʼdzina lanu ife tabwera kudzalimbana ndi gulu la ankhondo lalikulu kwambiri ngati ili. Inu Yehova ndinu Mulungu wathu, musalole kuti munthu akupambaneni.”

12Yehova anakantha Akusi pamaso pa Asa ndi Ayuda. Akusi anathawa, 13ndipo Asa ndi ankhondo ake anawathamangitsa mpaka ku Gerari. Gulu lonse lalikulu lija la Akusi linaphedwa. Sanapezeke mmodzi wamoyo pakati pawo. Iwo anakanthidwa pamaso pa Yehova ndi asilikali ake. Anthu a ku Yuda anatenga katundu wambiri olanda ku nkhondo. 14Iwo anawononga midzi yonse yozungulira Gerari pakuti mantha aakulu wochokera kwa Yehova anagwera anthuwo. Analanda katundu wa midzi yonse, popeza kunali katundu wambiri kumeneko. 15Anakathiranso nkhondo misasa ya anthu oweta ziweto ndipo anatenga nkhosa zambiri, mbuzi ndi ngamira. Atatero anabwerera ku Yerusalemu.