历代志上 19 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

历代志上 19:1-19

大卫击败亚扪人和亚兰人

1后来,亚扪拿辖死了,他儿子继位。 2大卫说:“我要恩待拿辖的儿子哈嫩,因为他父亲曾经恩待我。”他便派臣仆去安慰丧父的哈嫩大卫的臣仆来到亚扪境内要安慰哈嫩3亚扪的官长却对哈嫩说:“大卫派人来安慰你,你以为他是来吊唁你父亲吗?他的臣仆来见你不过是来探听虚实,想征服这地方。” 4哈嫩便把大卫的臣仆抓起来,剃去他们一半胡子,割去他们下身的衣服,然后放走他们。 5消息传到大卫那里,他就派人去迎接他们,告诉他们住在耶利哥,等胡须长好了再回来,因为他们倍觉羞辱。

6哈嫩及其他亚扪人知道得罪了大卫,就派人用三十四吨银子从美索不达米亚亚兰玛迦琐巴招兵买马, 7雇了三万二千辆战车和玛迦王及其军队。他们在米底巴附近扎营,亚扪人也从各城出来准备作战。 8大卫听见消息后,就派约押率领全体勇士出战。 9亚扪人在城门前列阵,来助战的诸王在郊野列阵。

10约押见自己前后受敌,就从以色列军中挑选一些精兵迎战亚兰人, 11把余下的军兵交给他的兄弟亚比筛领导,迎战亚扪人。 12他对亚比筛说:“倘若我胜不过亚兰人,你便过来支援我;倘若你胜不过亚扪人,我便过去支援你。 13我们要刚强,为我们的人民和我们上帝的城邑而奋勇作战。愿耶和华成全祂自己的旨意!” 14于是,约押率领军兵进攻亚兰人,亚兰人败逃。 15亚兰人败逃,亚扪人也逃离亚比筛,退回城中。约押便回师耶路撒冷

16亚兰人见自己败在以色列人手下,就派使者调来幼发拉底河那边的亚兰人,由哈大底谢的将军朔法率领。 17大卫听到消息后,就召集以色列全军,渡过约旦河,列阵与亚兰人交战。 18他们击溃了亚兰人,杀了七千名战车兵、四万步兵,还杀了他们的将军朔法19哈大底谢的属下见自己败于以色列人,便向大卫求和,臣服于他。从此,亚兰人不敢再支援亚扪人了。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 19:1-19

Davide Achita Nkhondo ndi Aamoni

1Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake. 2Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake.

Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa, 3atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?” 4Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.

5Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”

6Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba. 7Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.

8Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu. 9Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.

10Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu. 11Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni. 12Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa. 13Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”

14Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake. 15Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.

16Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.

17Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye. 18Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.

19Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake.

Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.