马太福音 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible 2022 (Simplified)

马太福音 1:1-25

耶稣基督的家谱

1耶稣基督是亚伯拉罕的子孙、大卫的后裔,以下是祂的家谱:

2亚伯拉罕以撒

以撒雅各

雅各犹大和他的兄弟,

3犹大她玛法勒斯谢拉

法勒斯希斯仑

希斯仑1:3 “兰”希腊文是“亚兰”。

4亚米拿达

亚米拿达拿顺

拿顺撒门

5撒门喇合波阿斯

波阿斯路得俄备得

俄备得耶西

6耶西大卫王。

大卫乌利亚的妻子生所罗门

7所罗门罗波安

罗波安亚比雅

亚比雅亚撒

8亚撒约沙法

约沙法约兰

约兰乌西雅

9乌西雅约坦

约坦亚哈斯

亚哈斯希西迦

10希西迦玛拿西

玛拿西亚们

亚们约西亚

11约西亚耶哥尼雅和他的兄弟,

那时以色列人被掳往巴比伦

12被掳到巴比伦以后,

耶哥尼雅撒拉铁

撒拉铁所罗巴伯

13所罗巴伯亚比玉

亚比玉以利亚敬

以利亚敬亚所

14亚所撒督

撒督亚金

亚金以律

15以律以利亚撒

以利亚撒马但

马但雅各

16雅各约瑟

约瑟就是玛丽亚的丈夫,

那被称为基督1:16 “基督”意思是“受膏者”。的耶稣就是玛丽亚生的。

17这样,从亚伯拉罕大卫共有十四代,从大卫到被掳至巴比伦也是十四代,从被掳至巴比伦到基督降生也是十四代。

耶稣的降生

18耶稣基督降生的经过记载如下。

耶稣的母亲玛丽亚约瑟订了婚,还没有成亲就从圣灵怀了孕。 19她未婚夫约瑟是个义人,不愿公开地羞辱她,就想暗中和她解除婚约。 20他正在考虑这事的时候,主的一位天使在梦中向他显现,说:“大卫的后裔约瑟,不要怕,把玛丽亚娶过来,因为她所怀的孕是从圣灵来的。 21她将生一个儿子,你要给祂取名叫耶稣1:21 “耶稣”意思是“救主”。,因为祂要把自己的子民从罪恶中救出来。”

22这一切应验了主借着先知所说的话: 23“必有童贞女怀孕生子,祂的名字要叫以马内利。”1:23 以赛亚书7:14以马内利的意思是“上帝与我们同在”。 24约瑟醒来,就遵从主的天使所吩咐的娶玛丽亚为妻, 25只是在她生下孩子之前没有与她同房。约瑟给孩子取名叫耶稣。

The Word of God in Contemporary Chichewa

Mateyu 1:1-25

Makolo a Yesu Khristu Monga mwa Thupi

1Buku lofotokoza za mʼbado wa Yesu Khristu mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu:

2Abrahamu anabereka Isake,

Isake anabereka Yakobo,

Yakobo anabereka Yuda ndi abale ake.

3Yuda anabereka Perezi ndi Zara, amene amayi awo anali Tamara.

Perezi anabereka Hezironi,

Hezironi anabereka Aramu.

4Aramu anabereka Aminadabu,

Aminadabu anabereka Naasoni,

Naasoni anabereka Salimoni.

5Salimoni anabereka Bowazi amene amayi ake anali Rahabe,

Bowazi anabereka Obedi amene amayi ake anali Rute,

Obedi anabereka Yese.

6Yese anabereka Mfumu Davide.

Ndipo Davide anabereka Solomoni, amene amayi ake anali mkazi wa Uriya.

7Solomoni anabereka Rehabiamu,

Rehabiamu anabereka Abiya,

Abiya anabereka Asa,

8Asa anabereka Yehosafati,

Yehosafati anabereka Yoramu,

Yoramu anabereka Uziya.

9Uziya anabereka Yotamu,

Yotamu anabereka Ahazi,

Ahazi anabereka Hezekiya.

10Hezekiya anabereka Manase,

Manase anabereka Amoni,

Amoni anabereka Yosiya.

11Yosiya anali atabala Yekoniya ndi abale ake pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babuloni.

12Ali ku ukapolo ku Babuloni,

Yekoniya anabereka Salatieli,

Salatieli anabereka Zerubabeli.

13Zerubabeli anabereka Abiudi,

Abiudi anabereka Eliakimu,

Eliakimu anabereka Azoro.

14Azoro anabereka Zadoki,

Zadoki anabereka Akimu,

Akimu anabereka Eliudi.

15Eliudi anabereka Eliezara,

Eliezara anabereka Matani,

Matani anabereka Yakobo.

16Yakobo anabereka Yosefe, mwamuna wa Mariya. Mariyayu ndiye anabereka Yesu wotchedwa Khristu.

17Kuyambira pa Abrahamu mpaka pa Davide, pali mibado khumi ndi inayi. Ndipo kuyambira pa Davide mpaka pamene Ayuda anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babuloni, pali mibado khumi ndi inayi. Ndiponso kuyambira nthawi ya ukapolo ku Babuloni mpaka pamene Khristu anabadwa, palinso mibado khumi ndi inayi.

Kubadwa kwa Yesu Khristu

18Kubadwa kwa Yesu Khristu kunali motere: Amayi ake, Mariya, anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanagone malo amodzi, anapezeka ali woyembekezera mwana mwa mphamvu ya Mzimu Woyera. 19Popeza Yosefe mwamuna wake anali munthu wolungama, sanafune kumuchititsa manyazi pomuleka poyera. Choncho anaganiza zomuleka mosaonetsera.

20Koma akuganiza zimenezi, taonani, mngelo wa Ambuye anamuonekera mʼmaloto nati, “Yosefe mwana wa Davide, usaope kumutenga Mariya kukhala mkazi wako, chifukwa mwana akuyembekezerayo ndi wochokera kwa Mzimu Woyera. 21Ndipo adzabala mwana wamwamuna, udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake ku machimo awo.”

22Zonsezi zinachitika kukwaniritsa zimene Ambuye ananena mwa mneneri kuti, 23“Onani namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli,” kutanthauza kuti, “Mulungu ali nafe.”

24Yosefe atadzuka, anachita zomwe mngelo wa Ambuye uja anamulamulira. Iye anamutenga Mariya kukhala mkazi wake. 25Koma sanagone malo amodzi mpaka mwanayo atabadwa ndipo anamutcha dzina lake Yesu.