耶稣降生伯利恒
1那时,凯撒奥古斯都颁下谕旨,命罗马帝国的人民都办理户口登记。 2这是第一次户口登记,正值居里纽任叙利亚总督。 3大家都回到本乡办理户口登记。 4约瑟因为是大卫家族的人,就从加利利的拿撒勒镇赶到犹太地区大卫的故乡伯利恒, 5要和已许配给他、怀着身孕的玛丽亚一起登记。 6他们抵达目的地时,玛丽亚产期到了, 7便生下第一胎,是个儿子。她用布把孩子裹好,安放在马槽里,因为旅店没有房间了。
牧羊人和天使
8当晚,伯利恒郊外有一群牧羊人正在看守羊群。 9忽然,主的天使向他们显现,主的荣光四面照着他们,他们非常害怕。 10天使对他们说:“不要怕!我告诉你们一个有关万民的大喜讯, 11今天在大卫的城里有一位救主为你们降生了,祂就是主基督! 12你们将看见一个婴孩包着布躺在马槽里,这就是给你们的记号。”
13忽然,有一大队天军出现,与那天使一同赞美上帝说:
14“在至高之处,
愿荣耀归于上帝!
在地上,
愿平安临到祂所喜悦的人!”
15众天使离开他们升回天上之后,牧羊人便商议说:“我们现在去伯利恒,察看一下主刚才告诉我们的那件事吧!” 16他们就连忙进城,找到了玛丽亚和约瑟以及躺在马槽里的婴孩。 17他们看过之后,就把天使告诉他们有关这婴孩的事传开了。 18听见的人都对牧羊人的话感到惊讶。
19但玛丽亚把这些事牢记在心里,反复思想。 20牧羊人在归途中不断地将荣耀归于上帝,赞美祂,因为他们的所见所闻跟天使告诉他们的一样。
奉献圣婴
21在第八天,婴孩接受了割礼,祂的名字叫耶稣,是玛丽亚怀孕前天使取的。
22摩西律法规定的洁净期满后,约瑟和玛丽亚把婴孩带到耶路撒冷去献给主, 23因为主的律法规定:必须把长子分别出来献给主。 24他们又按照主的律法献上祭物,即一对斑鸠或两只雏鸽。 25耶路撒冷有一位公义敬虔、有圣灵同在的人名叫希缅,他一直期待着以色列的安慰者到来。 26圣灵曾启示他:他去世前必能亲眼看见主所立的基督。
27一天,他受圣灵感动进入圣殿,看见约瑟和玛丽亚抱着婴孩耶稣进来,要依照律法的规定为祂行奉献礼, 28就把祂抱过来,称颂上帝说:
29“主啊,现在你的话已经成就,
可以让你的奴仆安然离世了,
30因为我已亲眼看到你的救恩,
31就是你为万民所预备的救恩。
32这救恩是启示外族人的光,
也是你以色列子民的荣耀。”
33约瑟和玛丽亚听见这番话,感到惊奇。 34希缅给他们祝福后,就对孩子的母亲玛丽亚说:“看啊,这孩子必使以色列许多人跌倒、许多人兴起。祂将成为众人攻击的对象, 35好叫许多人的心思意念暴露出来,你自己则会心如刀割。”
36-37亚设支派中有一位八十四岁高龄的女先知名叫亚拿,是法内利的女儿,婚后七年便开始守寡,之后一直住在圣殿里,禁食祷告,日夜事奉上帝。 38正在那时,她也前来感谢上帝,并把耶稣的事报告给所有盼望耶路撒冷蒙救赎的人。
39约瑟和玛丽亚办完了主的律法规定的一切事之后,就回到他们的家乡——加利利的拿撒勒。 40耶稣渐渐长大,身心强健,充满智慧,上帝的恩典与祂同在。
少年耶稣圣殿论道
41约瑟和玛丽亚每年都上耶路撒冷去过逾越节。 42耶稣十二岁那年,跟父母照例上去过节。 43节期完了,约瑟和玛丽亚便启程回家,他们并不知道少年耶稣仍然留在耶路撒冷, 44还以为祂跟在同行的人中间。他们走了一天的路后,才开始在亲戚朋友中找祂, 45结果没有找到,只好回到耶路撒冷。 46三天后,他们才在圣殿里找到耶稣,祂正和教师们坐在一起,一边听一边问问题。 47祂的知识和对答令听见的人感到惊奇。 48约瑟和玛丽亚看见耶稣在那里,大为惊奇。
玛丽亚对祂说:“儿子,你为什么这样对我们呢?你父亲和我急得到处找你!”
49耶稣对他们说:“你们为什么找我呢?难道你们不知道我应该在我父的家吗?” 50但他们不明白祂在讲什么。
51于是,耶稣随父母回到拿撒勒,并顺从他们。玛丽亚把这一切事牢记在心。 52耶稣渐渐长大,智慧与日俱增,越来越受上帝和人们的喜爱。
Kubadwa kwa Yesu
1Mʼmasiku amenewo Kaisara Augusto anapereka lamulo kuti kalembera achitike mʼdziko lonse la Aroma. 2(Uyu ndi kalembera woyamba amene anachitika pamene Kureniyo anali bwanamkubwa wa Siriya). 3Ndipo aliyense anapita ku mzinda wa kwawo kukalembetsa.
4Choncho Yosefe anachoka ku Nazareti ku Galileya kupita ku Yudeya, ku Betelehemu ku mudzi wa Davide, chifukwa anali wa banja ndi fuko la Davide. 5Iye anapita kumeneko kukalembetsa pamodzi ndi Mariya, amene anapalana naye ubwenzi kuti akwatirane ndipo anali woyembekezera. 6Ali kumeneko, nthawi inakwana yakuti mwana abadwe, 7ndipo anabereka mwana wake woyamba, wamwamuna. Iye anamukulunga mʼnsalu ndi kumuyika modyera ngʼombe, chifukwa kunalibe malo mʼnyumba ya alendo.
Abusa ndi Angelo
8Ndipo kunali abusa amene amakhala ku dera lomwelo, kuyangʼanira ziweto zawo usiku. 9Mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iwo ndipo ulemerero wa Ambuye unawala mowazungulira. Iwo anachita mantha. 10Koma mngeloyo anawawuza kuti, “Musachite mantha. Ine ndakubweretserani Uthenga Wabwino wachimwemwe chachikulu umene udzakhala wa anthu onse. 11Lero mʼmudzi wa Davide wakubwadwirani Mpulumutsi; Iye ndi Khristu Ambuye. 12Ichi chidzakhala chizindikiro kwa inu: mukapeza mwana wakhanda wokutidwa ndi nsalu atagona modyera ngʼombe.”
13Mwadzidzidzi gulu lalikulu la angelo linaonekera pamodzi ndi mngeloyo, kuyamika Mulungu ndi kumati,
14“Ulemerero kwa Mulungu mmwambamwamba,
ndi mtendere kwa anthu pa dziko lapansi amene Iye akondwera nawo.”
15Angelowo atabwerera kumwamba, abusawo anati kwa wina ndi mnzake, “Tiyeni ku Betelehemu tikaone zinthu zomwe zachitika, zimene Ambuye atiwuza ife.”
16Ndipo iwo anafulumira nyamuka nakapeza Mariya ndi Yosefe ndi mwana wakhanda, amene anagona modyera ngʼombe. 17Pamene anamuona Iye, iwo anafotokoza zomwe anawuzidwa za mwanayo, 18ndipo onse amene anamva zimene abusawa ananena anadabwa. 19Koma Mariya anasunga zonsezi mu mtima mwake ndi kumazilingalira. 20Abusa anabwerera, akulemekeza ndi kuyamika Mulungu chifukwa cha zonse anazimva ndi kuziona, zomwe zinali monga anawuzidwira ndi angelo aja.
Yesu Aperekedwa mʼNyumba ya Mulungu
21Pa tsiku lachisanu ndi chitatu, tsiku loti amuchite mdulidwe anamutcha Yesu, dzina limene mngelo anamupatsa asanabadwe.
22Nthawi yoyeretsedwa kwawo itatha, monga mwa lamulo la Mose, Yosefe ndi Mariya anapita naye ku Yerusalemu kukamupereka kwa Ambuye. 23(Monga mmene zinalembedwera mu lamulo la Ambuye kuti, “Muzikapereka kwa Ambuye mwana aliyense wamwamuna woyamba kubadwa”), 24ndi kupereka nsembe posunga zimene zinanenedwa mulamulo la Ambuye: “Njiwa ziwiri kapena mawunda ankhunda awiri.”
25Ndipo taonani, mu Yerusalemu munali munthu wotchedwa Simeoni, amene anali wolungama ndi wodzipereka. Iye ankadikira chitonthozo cha Israeli, ndipo Mzimu Woyera anali pa iye. 26Mzimu Woyera anamuwululira kuti sadzafa asanaone Khristu wa Ambuye. 27Motsogozedwa ndi Mzimu Woyera, iye anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Makolo ake a Yesu atabwera naye kuti achite naye mwambo malingana ndi malamulo, 28Simeoni anamunyamula mʼmanja mwake nayamika Mulungu, nati:
29“Ambuye waulamuliro, monga munalonjeza,
tsopano lolani kuti mtumiki wanu apite mu mtendere.
30Pakuti maso anga aona chipulumutso chanu,
31chimene Inu munakonza pamaso pa anthu onse,
32kuwala kowunikira anthu a mitundu ina
ndi kwa ulemerero kwa anthu anu Aisraeli.”
33Abambo ndi amayi a Mwanayo anadabwa chifukwa cha zimene zinanenedwa za Iye. 34Kenaka Simeoni anawadalitsa ndipo anati kwa Mariya amayi ake: “Mwana uyu wakonzedwa kukhala kugwa ndi kudzuka kwa ambiri mu Israeli, ndi kukhala chizindikiro chimene adzayankhula motsutsana nacho, 35kotero kuti malingaliro a mitima ya ambiri adzawululidwa. Ndipo lupanga lidzabaya moyo wakonso.”
36Panalinso mneneri wamkazi, dzina lake Ana, mwana wa Fanuelo, wa fuko la Aseri. Anali wokalamba kwambiri; anakhala ndi mwamuna wake zaka zisanu ndi ziwiri atakwatiwa, 37ndipo kenaka anakhala wamasiye mpaka pamene anali ndi zaka 84. Iye sanachoke mʼNyumba ya Mulungu koma ankapembedza usiku ndi usana, kusala kudya ndi kupemphera. 38Pa nthawiyo pamene ankapita kwa iwo, iye anayamika Mulungu ndi kuyankhula za Mwanayo kwa onse amene ankayembekezera chipulumutso cha Yerusalemu.
39Yosefe ndi Mariya atachita zonse zimene zinkafunikira ndi lamulo la Ambuye, anabwerera ku Galileya ku mudzi wa Nazareti. 40Ndipo Mwanayo anakula nakhala wamphamvu; Iye anadzazidwa ndi nzeru, ndipo chisomo cha Mulungu chinali pa Iye.
Yesu mʼNyumba ya Mulungu
41Chaka chilichonse makolo ake ankapita ku Yerusalemu ku phwando la Paska. 42Iye ali ndi zaka khumi ndi ziwiri, anapita ku phwando, monga mwa mwambo. 43Phwando litatha, pamene makolo ake ankabwerera kwawo, mnyamata Yesu anatsalira ku Yerusalemu, koma iwo sanadziwe zimenezi. 44Poganiza kuti anali nawo mʼgulu lawo, anayenda tsiku limodzi. Kenaka anayamba kumufunafuna pakati pa abale awo ndi anzawo. 45Atalephera kumupeza, anabwerera ku Yerusalemu kukamufuna. 46Patatha masiku atatu anamupeza ali mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, atakhala pakati pa aphunzitsi, akumvetsera ndi kuwafunsa mafunso. 47Aliyense amene anamumva Iye anadabwa ndi chidziwitso chake ndi mayankho ake. 48Makolo ake atamuona, anadabwa. Amayi ake anati kwa Iye, “Mwanawe, watichitira zimenezi chifukwa chiyani? Abambo ako ndi ine takhala tili ndi nkhawa kukufunafuna Iwe.”
49Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumandifunafuna? Kodi simukudziwa kuti ndikuyenera kukhala mʼnyumba ya Atate anga?” 50Koma iwo sanazindikire chomwe Iye amatanthauza.
51Kenaka anapita nawo ku Nazareti ndipo anawamvera iwo. Koma amayi ake anasunga zinthu zonsezi mu mtima mwawo.
52Ndipo Yesu anakula mu nzeru, msinkhu ndi chisomo cha Mulungu ndi anthu.