路加福音 1 – CCB & CCL

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

路加福音 1:1-80

1-2提阿非罗大人,已经有很多人根据最初的目击者和传道者给我们的口述,把我们中间发生的事记载下来。 3我把一切事情从头至尾仔细查考之后,决定按次序写出来, 4使你知道自己所学的道都是有真凭实据的。

天使预告施洗者约翰出生

5犹太希律执政期间,亚比雅的班里有位祭司名叫撒迦利亚,他妻子伊丽莎白亚伦的后裔。 6夫妻二人遵行主的一切诫命和条例,无可指责,在上帝眼中是义人。 7但他们没有孩子,因为伊丽莎白不能生育,二人又年纪老迈。

8有一天,轮到撒迦利亚他们那一班祭司当值, 9他们按照祭司的规矩抽签,抽中撒迦利亚到主的殿里去烧香。 10众百姓都在外面祷告。 11那时,主的天使在香坛的右边向撒迦利亚显现, 12撒迦利亚见了,惊慌害怕起来。

13天使对他说:“撒迦利亚,不要害怕,你的祷告已蒙垂听。你的妻子伊丽莎白要为你生一个儿子,你要给他取名叫约翰14你必欢喜快乐,许多人也会因为他的诞生而欣喜雀跃, 15因为他将成为主伟大的仆人。他必滴酒不沾,并且在母腹里就被圣灵充满。 16他将劝导许多以色列人回心转意,归顺主——他们的上帝。 17他将以先知以利亚的心志和能力做主的先锋,使父亲的心转向儿女,使叛逆的人回转、顺从义人的智慧,为主预备合用的子民。”

18撒迦利亚对天使说:“我已经老了,我的妻子也上了年纪,我如何知道这是真的呢?” 19天使回答说:“我是侍立在上帝面前的加百列,奉命来向你报这喜讯。 20我说的这些话到时候必定应验。但因为你不肯相信我的话,所以这事成就以前,你将变成哑巴,不能说话。”

21人们在等候撒迦利亚,见他在圣殿里迟迟不出来,都感到奇怪。 22后来他出来了,却成了哑巴,不能说话,只能打手势,大家意识到他在圣殿里看见了异象。 23撒迦利亚供职期满,就回家去了。 24不久,伊丽莎白果然怀了孕,她有五个月闭门不出。 25她说:“主真是眷顾我,除掉了我不生育的羞耻。”

天使预告耶稣降生

26伊丽莎白怀孕六个月的时候,天使加百列又奉上帝的命令到加利利拿撒勒27去见一位童贞女,她叫玛丽亚玛丽亚已经和大卫的后裔约瑟订了婚。

28天使到了玛丽亚那里,说:“恭喜你,蒙大恩的女子,主与你同在!”

29玛丽亚听了觉得十分困惑,反复思想这话的意思。

30天使对她说:“玛丽亚,不要害怕,你在上帝面前已经蒙恩了。 31你要怀孕生子,并给祂取名叫耶稣。 32祂伟大无比,将被称为至高者的儿子,主上帝要把祂祖先大卫的王位赐给祂。 33祂要永远统治以色列1:33 以色列”希腊文是“雅各的家”。,祂的国度永无穷尽。”

34玛丽亚对天使说:“这怎么可能呢?我还是童贞女。”

35天使回答说:“圣灵要临到你身上,至高者的能力要荫庇你,所以你要生的那圣婴必称为上帝的儿子。 36看啊,你的亲戚伊丽莎白年纪老迈,一向不能生育,现在已经怀男胎六个月了。 37因为上帝无所不能。”

38玛丽亚说:“我是主的婢女,愿你所说的话在我身上成就。”于是天使离开了她。

玛丽亚看望伊丽莎白

39不久,玛丽亚便动身赶到犹太山区的一座城, 40进了撒迦利亚的家,向伊丽莎白请安。 41伊丽莎白一听见玛丽亚的问安,腹中的胎儿便跳动起来,伊丽莎白被圣灵充满, 42高声喊着说:“在妇女中你是最蒙福的!你腹中的孩子也是蒙福的! 43我主的母亲来探望我,我怎么敢当呢? 44我一听到你问安的声音,腹中的孩子就欢喜跳动。 45相信主所说的话必实现的女子有福了!”

46玛丽亚说:

“我的心尊主为大,

47我的灵因我的救主上帝而欢喜,

48因祂眷顾我这卑微的婢女,

从今以后,

世世代代都要称我是有福的。

49全能者在我身上行了奇事,

祂的名是神圣的。

50祂怜悯敬畏祂的人,

直到世世代代。

51祂伸出臂膀,施展大能,

驱散心骄气傲的人。

52祂使当权者失势,

叫谦卑的人升高。

53祂使饥饿的得饱足,

叫富足的空手而去。

54祂扶助了自己的仆人以色列

55祂要施怜悯给亚伯拉罕和他的子孙,

直到永远,

正如祂对我们祖先的应许。”

56玛丽亚伊丽莎白同住了约三个月,便回家去了。

施洗者约翰出生

57伊丽莎白的产期到了,生下一个儿子。 58亲戚和邻居听见主向她大施怜悯,都和她一同欢乐。 59到了第八天,他们来给孩子行割礼,想照他父亲的名字给他取名叫撒迦利亚

60伊丽莎白说:“不!要叫他约翰。”

61他们说:“你们家族中没有人用这个名字啊!” 62他们便向他父亲打手势,问他要给孩子起什么名字。 63撒迦利亚就要了一块写字板,写上:“他的名字叫约翰。”大家看了都很惊奇。 64就在那时,撒迦利亚恢复了说话的能力,便开口赞美上帝。 65住在周围的人都很惧怕,这消息很快就传遍了整个犹太山区。 66听见的人都在想:“这孩子将来会怎样呢?因为主与他同在。”

撒迦利亚的预言

67孩子的父亲撒迦利亚被圣灵充满,便预言说:

68“主——以色列的上帝当受称颂,

因祂眷顾、救赎了自己的子民,

69在祂仆人大卫的家族中为我们兴起了一位大能的拯救者1:69 拯救者”希腊文是“拯救的角”。

70正如祂从亘古借着祂圣先知们的口所说的。

71祂要从仇敌和一切恨我们之人手中拯救我们。

72祂怜悯我们的祖先,

持守自己的圣约,

73就是祂对我们的先祖亚伯拉罕所起的誓,

74要把我们从仇敌手中拯救出来,

75使我们一生一世在圣洁和公义中坦然无惧地事奉祂。

76至于你,我的儿子啊!

你将要被称为至高者的先知,

因为你要走在主的前面,

为祂预备道路,

77使百姓因罪得赦免而明白救恩的真谛。

78由于上帝的怜悯,

清晨的曙光必从高天普照我们,

79照亮那些生活在黑暗中和死亡阴影下的人,

带领我们走平安的道路。”

80那孩子渐渐长大,心灵强健,在向以色列人公开露面之前,一直住在旷野。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 1:1-80

Mawu Oyamba

1Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu, 2monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu. 3Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo, 4kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.

Aneneratu za Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

5Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni. 6Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse. 7Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.

8Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu, 9Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani. 10Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.

11Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira. 12Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha. 13Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane. 14Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake, 15chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa. 16Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo. 17Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”

18Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”

19Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu. 20Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”

21Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu. 22Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.

23Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo. 24Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu. 25Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”

Aneneratu za Kubadwa kwa Yesu

26Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya, 27kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya. 28Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”

29Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere. 30Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu. 31Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu. 32Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide, 33ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.”

34Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”

35Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu. 36Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi. 37Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”

38Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”

Mariya Acheza kwa Elizabeti

39Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya, 40kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti. 41Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera. 42Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke! 43Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine? 44Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe. 45Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”

Nyimbo ya Mariya

46Ndipo Mariya anati:

“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.

47Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

48pakuti wakumbukira

kudzichepetsa kwa mtumiki wake.

Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,

49pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,

dzina lake ndi loyera.

50Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye

kufikira mibadomibado.

51Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;

Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.

52Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,

koma wakweza odzichepetsa.

53Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino

koma anachotsa olemera wopanda kanthu.

54Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,

pokumbukira chifundo chake.

55Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse

monga ananena kwa makolo athu.”

56Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.

Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

57Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna. 58Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.

59Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya, 60koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”

61Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”

62Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo. 63Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.” 64Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu. 65Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi. 66Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.

Nyimbo ya Zakariya

67Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,

68“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli

chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.

69Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife

mu nyumba ya mtumiki wake Davide.

70(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera),

71chipulumutso kuchoka kwa adani athu

ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,

72kuonetsa chifundo kwa makolo athu

ndi kukumbukira pangano lake loyera,

73lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:

74kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu,

ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,

75mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.

76“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba;

pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,

77kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso

kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,

78chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu,

ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,

79kuwalira iwo okhala mu mdima

ndi mu mthunzi wa imfa,

kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”

80Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.