Yesaia 38 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Yesaia 38:1-22

Hesekia Yadeɛ

1Saa ɛberɛ no mu, ɔhene Hesekia yaree yarewuo, ɛnna Amos babarima odiyifoɔ Yesaia kɔsraa no. Ɔkaa saa asɛm yi kyerɛɛ ɔhene no, “Sɛdeɛ Awurade seɛ nie: Hyɛ wo nsamanseɛ, ɛfiri sɛ, wobɛwu. Wo yadeɛ no rennyae.”

2Ɛberɛ a Hesekia tee asɛm yi, ɔtwaa nʼani hwɛɛ fasuo, bɔɔ Awurade mpaeɛ sɛ, 3“Kae, Ao, Awurade, sɛdeɛ manante wʼanim nokorɛm na mede mʼakoma ayɛ deɛ ɛfata wɔ wʼanim.” Na Hesekia suu bebree.

4Na saa asɛm yi firi Awurade nkyɛn kɔɔ Yesaia hɔ sɛ, 5“Sane kɔ Hesekia nkyɛn, na kɔka kyerɛ no sɛ, ‘Sei na Awurade, wʼagya Dawid Onyankopɔn ka: Mate wo mpaeɛbɔ no, na mahunu wo nisuo. Mede mfeɛ dunum bɛka wo nkwa nna ho. 6Na mɛgye wo ne kuropɔn yi afiri Asiriahene nsam. Mɛbɔ kuropɔn yi ho ban.

7“ ‘Na yei ne nsɛnkyerɛnneɛ a Awurade bɛyɛ de adi ho adanseɛ sɛ, ɔbɛdi ne bɔhyɛ so: 8Mɛma owia ano sunsum atwe akɔ nʼakyi anammɔn edu wɔ Ahas atwedeɛ so.’ ” Ɛno enti, owia hyerɛn no kɔɔ nʼakyi anammɔn edu.

9Deɛ Yudahene Hesekia twerɛeɛ ne yadeɛ ne nʼayaresa akyi nie:

10Mekaa sɛ, “Mʼasetena mu nnapa yi mu

ɛsɛ sɛ mefa owuo apono mu

na wɔgye me mfeɛ a aka yi anaa?”

11Mekaa sɛ, “Merenhunu Awurade Onyankopɔn bio

Awurade a ɔwɔ ateasefoɔ asase so.

Merenhunu adasamma bio,

anaa merenka wɔn a wɔte ewiase yi ho bio.

12Wɔadwiri me fie agu agye afiri me nsam,

te sɛ odwanhwɛfoɔ ntomadan.

Matwa me nkwa so sɛdeɛ ɔnwomfoɔ,

twa me firi asadua so;

awia ne anadwo wotwaa me nkwa so.

13Mede ntoboaseɛ twɛneeɛ kɔsii ahemadakye,

nanso wɔbobɔɔ me nnompe mu te sɛ gyata;

awia ne anadwo wotwaa me nkwa so.

14Mesuiɛ sɛ asomfena anaa asukɔnkɔn;

metwaa adwo sɛ aborɔnoma a ɔredi awerɛhoɔ.

Mʼani yɛɛ siamoo ɛberɛ a mehwɛɛ soro.

Mewɔ ɔhaw mu, Awurade, bra bɛboa me!”

15Na ɛdeɛn na mɛtumi aka?

Wakasa akyerɛ me, na ɔno ankasa na wayɛ yei.

Mede ahobrɛaseɛ bɛnante mʼasetena nyinaa mu

me kra ahoyera yi enti.

16Awurade, ɛnam saa nneɛma yi so na nnipa nya nkwa

na me honhom nso anya nkwa wɔ mu.

Wode mʼapɔmuden asane ama me.

Wonam so ama manya nkwa.

17Aane, ɛyɛ me yieyɛ enti

na mekɔɔ saa ahoyera yi mu.

Wo dɔ enti, wode me sieeɛ

na mankɔ ɔsɛe amena mu;

na wode me bɔne nyinaa akyɛ me.

18Damena rentumi nkamfo wo;

owuo rentumi nto wo ayɛyi nnwom;

wɔn a wɔsiane kɔ amena mu no

rentumi nya anidasoɔ wɔ wo nokorɛ mu bio.

19Ateasefoɔ nko na wɔbɛtumi akamfo wo,

sɛdeɛ mereyɛ ɛnnɛ yi;

agyanom ka wo nokorɛdie ho asɛm

kyerɛ wɔn mma.

20Awurade bɛgye me nkwa,

na yɛde ahoma nnwontodeɛ bɛto nnwom

yɛn nkwa nna nyinaa

Awurade efie.

21Na Yesaia kaa sɛ, “Momfa borɔdɔma nyɛ nku mfa nsra pɔmpɔ no so, na ne ho bɛyɛ no den.”

22Na Hesekia bisaa sɛ, “Ɛdeɛn nsɛnkyerɛnneɛ na ɛbɛda no adi sɛ mɛkɔ Awurade asɔredan mu?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 38:1-22

Kudwala kwa Hezekiya

1Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

2Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, 3“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

4Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: 5“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. 6Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

7“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: 8Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

9Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10Ine ndinaganiza kuti

ndidzapita ku dziko la akufa

pamene moyo ukukoma.

11Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,

mʼdziko la anthu amoyo,

sindidzaonanso mtundu wa anthu

kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.

12Nyumba yanga yasasuka

ndipo yachotsedwa.

Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,

ngati munthu wowomba nsalu;

kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.

13Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;

koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,

ndipo mwakhala mukundisiya.

14Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,

ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.

Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.

Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15Koma ine ndinganene chiyani?

Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.

Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,

ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.

16Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.

Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.

Munandichiritsa ndi

kundikhalitsa ndi moyo.

17Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere

kuti ndikhale ndi moyo;

Inu munandisunga

kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko

chifukwa mwakhululukira

machimo anga onse.

18Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,

akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.

Iwo amene akutsikira ku dzenje

sangakukhulupirireni.

19Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,

monga mmene ndikuchitira ine lero lino;

abambo amawuza ana awo za

kukhulupirika kwanu.

20Yehova watipulumutsa.

Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe

masiku onse a moyo wathu

mʼNyumba ya Yehova.

21Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”