Nkɔmhyɛ A Ɛtia Moab
1Adehunu a ɛfa Moab ho:
Wɔasɛe Ar a ɛwɔ Moab
anadwo koro pɛ!
Wɔasɛe Kir a ɛwɔ Moab
anadwo koro pɛ!15.1 Ar ne Kir yɛ Moabfoɔ nkuro atitire mmienu.
2Dibon foro kɔ nʼasɔredan mu,
ɔkɔ ne sorɔnsorɔmmea kɔ su;
Moab twa adwo wɔ Nebo ne Medeba ho.
Wɔayi eti biara so nwi
na abɔgyesɛ biara nso wɔatwitwa.
3Wɔfirafira ayitoma wɔ mmɔntene so;
wɔ adan atifi ne ɔman ahyiaeɛ
wɔn nyinaa retwa adwo,
wɔdeda fam na wɔsu.
4Hesbon ne Eleale teaam su,
wɔte wɔn nne kɔduru Yahas nohoa.
Enti Moab mmarimma akofoɔ teaam su,
na wɔabotoboto.
5Medi Moab ho awerɛhoɔ wɔ mʼakoma mu;
nʼadwanefoɔ dwane kɔduru Soar,
ne Eglat Selisiya.
Wɔforo kɔ Luhit,
wɔrekɔ nyinaa na wɔresu;
Horonaim ɛkwan so nso
wɔdi wɔn sɛeɛ ho awerɛhoɔ.
6Nimrim nsuwansuwa awewe
na ɛserɛ no ahye
afifideɛ nyinaa ayera
na ɛnkaa wira biara a ɛyɛ mono.
7Enti ahonyadeɛ a wɔapɛ agu hɔ no
wɔsoa de kɔtwa mpampuro bɔnhwa.
8Wɔn nkekamu gyegye wɔ Moab ahyeɛ so;
wɔn agyaadwotwa kɔduru Eglaim
na wɔn abubuobɔ kɔduru Beer Elim.
9Dimon nsuo ayɛ mogya nkoaa
nanso mɛkɔ so ne no adi.
Gyata bɛba Moab adwanefoɔ no so
ne wɔn a wɔbɛka asase no so.
Za Kulangidwa kwa Mowabu
1Uthenga wonena za Mowabu:
Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
Mzinda wa Kiri wawonongedwa,
wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,
akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;
anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.
Mutu uliwonse wametedwa mpala,
ndipo ndevu zonse zametedwa.
3Mʼmisewu akuvala ziguduli;
pa madenga ndi mʼmabwalo
aliyense akulira mofuwula,
misozi ili pupupu.
4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,
mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.
Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,
ndipo ataya mtima.
5Inenso ndikulirira Mowabu;
chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari
ndi Egilati-Selisiya
akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,
Akulira mosweka mtima
pa njira yopita ku Horonaimu;
akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6Madzi a ku Nimurimu aphwa
ndipo udzu wauma;
zomera zawonongeka
ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,
achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;
kulira kwawo kosweka mtima kukumveka
mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,
komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,
mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu
ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.