Yesaia 15 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Yesaia 15:1-9

Nkɔmhyɛ A Ɛtia Moab

1Adehunu a ɛfa Moab ho:

Wɔasɛe Ar a ɛwɔ Moab

anadwo koro pɛ!

Wɔasɛe Kir a ɛwɔ Moab

anadwo koro pɛ!15.1 Ar ne Kir yɛ Moabfoɔ nkuro atitire mmienu.

2Dibon foro kɔ nʼasɔredan mu,

ɔkɔ ne sorɔnsorɔmmea kɔ su;

Moab twa adwo wɔ Nebo ne Medeba ho.

Wɔayi eti biara so nwi

na abɔgyesɛ biara nso wɔatwitwa.

3Wɔfirafira ayitoma wɔ mmɔntene so;

wɔ adan atifi ne ɔman ahyiaeɛ

wɔn nyinaa retwa adwo,

wɔdeda fam na wɔsu.

4Hesbon ne Eleale teaam su,

wɔte wɔn nne kɔduru Yahas nohoa.

Enti Moab mmarimma akofoɔ teaam su,

na wɔabotoboto.

5Medi Moab ho awerɛhoɔ wɔ mʼakoma mu;

nʼadwanefoɔ dwane kɔduru Soar,

ne Eglat Selisiya.

Wɔforo kɔ Luhit,

wɔrekɔ nyinaa na wɔresu;

Horonaim ɛkwan so nso

wɔdi wɔn sɛeɛ ho awerɛhoɔ.

6Nimrim nsuwansuwa awewe

na ɛserɛ no ahye

afifideɛ nyinaa ayera

na ɛnkaa wira biara a ɛyɛ mono.

7Enti ahonyadeɛ a wɔapɛ agu hɔ no

wɔsoa de kɔtwa mpampuro bɔnhwa.

8Wɔn nkekamu gyegye wɔ Moab ahyeɛ so;

wɔn agyaadwotwa kɔduru Eglaim

na wɔn abubuobɔ kɔduru Beer Elim.

9Dimon nsuo ayɛ mogya nkoaa

nanso mɛkɔ so ne no adi.

Gyata bɛba Moab adwanefoɔ no so

ne wɔn a wɔbɛka asase no so.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 15:1-9

Za Kulangidwa kwa Mowabu

1Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

Mzinda wa Kiri wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,

akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;

anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.

Mutu uliwonse wametedwa mpala,

ndipo ndevu zonse zametedwa.

3Mʼmisewu akuvala ziguduli;

pa madenga ndi mʼmabwalo

aliyense akulira mofuwula,

misozi ili pupupu.

4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,

mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.

Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,

ndipo ataya mtima.

5Inenso ndikulirira Mowabu;

chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari

ndi Egilati-Selisiya

akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,

Akulira mosweka mtima

pa njira yopita ku Horonaimu;

akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.

6Madzi a ku Nimurimu aphwa

ndipo udzu wauma;

zomera zawonongeka

ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.

7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,

achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.

8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;

kulira kwawo kosweka mtima kukumveka

mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.

9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,

komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,

mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu

ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.