Nnwom 45 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 45:1-17

Dwom 45

Kora mma dwom. Ayeforɔhyia dwom.

1Botaeɛ bi a ɛdi mu akanyane mʼakoma

ɛberɛ a merebɔ ɔhene mmrane no;

me tɛkrɛma yɛ ɔtwerɛfoɔ kunini bi twerɛdua.

2Wodi mu wɔ mmarima mu

na wɔde adom bi asra wʼano,

ɛsiane sɛ Onyankopɔn ahyira wo afebɔɔ no enti.

3Fa wʼakofena bɔ wo nkyɛn mu, Ao Otumfoɔ;

fa animuonyam ne kɛseyɛ fira.

4Fa wo kɛseyɛ mu kɔ wʼanim nkonimdie so

wɔ nokorɛ, ahobrɛaseɛ ne tenenee mu;

ma wo nsa nifa nna wo nnwuma a ɛyɛ nwanwa no adi.

5Ma wo bɛmma namnam no nhwere ɔhene atamfoɔ akoma mu;

na ma amanaman nhwe wo nan ase.

6Ao Onyankopɔn, wʼahennwa no bɛtena hɔ daa daa;

tenenee ahempoma bɛyɛ wʼahennie no ahempoma.

7Wodɔ tenenee na wokyiri bɔne.

Ɛno enti Onyankopɔn, wo Onyankopɔn de wo asi wo mfɛfoɔ so,

na ɔde anigyeɛ ngo asra wo.

8Kurobo, pɛperɛ ne bɛwewonua hwa agye wo batakari mu nyinaa;

sankuo so nnwom a ɛfiri ahemfie a wɔde asonse asiesie ho mu

ma wʼani gye.

9Ahemfo mmammaa ka wo mmaa atitire ho;

wo nsa nifa so na ayeforɔ dehyeɛ a ɔhyɛ Ofir sikakɔkɔɔ gyina.

10Ao ɔbabaa tie, dwene ho na yɛ ɔsetie;

ma wo werɛ mfiri wo nkurɔfoɔ ne wo agya fie.

11Wʼahoɔfɛ asɔ ɔhene no ani;

di no nni, ɛfiri sɛ ɔno ne wo wura.

12Tiro Babaa de ayɛyɛdeɛ bɛba;

mmarima adefoɔ bɛdɛfɛdɛfɛ wo.

13Ɔhene babaa a ɔwɔ ne piam no yɛ onimuonyamfoɔ

wɔde sikakɔkɔɔ abobɔ nʼatadeɛ yuu mu.

14Ɔhyɛ ntadeɛ a wɔadi mu adwinneɛ na wɔde no kɔma ɔhene;

ne mfɛfoɔ mmaabunu di nʼakyi

na wɔde wɔn nyinaa brɛ wo.

15Wɔde ahosɛpɛ ne anigyeɛ kɔ mu;

wɔhyɛne ɔhempɔn no ahemfie.

16Wo mmammarima bɛsi wʼagyanom ananmu

wobɛyɛ wɔn mmapɔmma wɔ asase no so nyinaa.

17Mɛma wɔakae wo wɔ awontoatoasoɔ nyinaa mu;

ɛno enti amanaman bɛkamfo wo daa nyinaa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 45:1-17

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

1Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

2Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

3Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

4Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

5Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

6Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

7Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

8Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

9Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

10Tamvera, iwe mwana wa mkazi ganizira ndipo tchera khutu;

iwala anthu ako ndi nyumba ya abambo ako.

11Mfumu yathedwa nzeru chifukwa cha kukongola kwako;

mulemekeze pakuti iyeyo ndiye mbuye wako.

12Mwana wa mkazi wa ku Turo adzabwera ndi mphatso,

amuna a chuma adzafunafuna kukoma mtima kwako.

13Wokongola kwambiri ndi mwana wa mfumu ali mʼchipinda mwake,

chovala chake ndi cholukidwa ndi thonje ndi golide.

14Atavala zovala zamaluwamaluwa akupita naye kwa mfumu;

anamwali okhala naye akumutsatira

ndipo abweretsedwa kwa inu.

15Iwo akuwaperekeza ndi chimwemwe ndi chisangalalo;

akulowa mʼnyumba yaufumu.

16Ana ako aamuna adzatenga malo a makolo ako;

udzachititsa kuti akhale ana a mfumu mʼdziko lonse.

17Ndidzabukitsa mbiri yako mʼmibado yonse;

choncho mitundu yonse idzakutamanda ku nthawi za nthawi.