Nnwom 110 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 110:1-7

Dwom 110

Dawid dwom.

1Awurade ka kyerɛɛ me Wura sɛ,

“Tena me nifa so

kɔsi sɛ mede wʼatamfoɔ

bɛyɛ wo nan ntiasoɔ.”

2Awurade bɛtrɛ wʼahempoma denden mu afiri Sion;

na wobɛdi ɔhene wɔ wʼatamfoɔ so.

3Wʼakodɔm bɛyi wɔn akoma mu

ɛda a wobɛkɔ sa.

Tumi kronkron bɛyɛ wʼaduradeɛ

na wo mmabunu bɛba wo nkyɛn

sɛdeɛ bosuo gugu anɔpahema.

4Awurade aka ntam

na ɔrensesa nʼadwene:

“Woyɛ daapem ɔsɔfoɔ

te sɛ Melkisedek sɛso.”

5Awurade wɔ wo nifa so;

ɔbɛdwerɛ ahemfo wɔ nʼabufuhyeɛ da no.

6Ɔbɛbu amanaman atɛn aboaboa afunu ano;

na wadwerɛ sodifoɔ a wɔwɔ asase so nyinaa.

7Ɔbɛnom asuwa a ɛda ɛkwan nkyɛn mu nsuo

enti ɔbɛdi nkonim.

Ɔhene no bɛnom asuwa a ɛda kwankyɛn mu nsuo,

na wanya ahoɔden, na wagyina nkonimdie mu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 110:1-7

Salimo 110

Salimo la Davide.

1Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,

“Khala ku dzanja langa lamanja

mpaka nditasandutsa adani ako

kukhala chopondapo mapazi ako.”

2Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;

udzalamulira pakati pa adani ako.

3Ankhondo ako adzakhala odzipereka

pa tsiku lako la nkhondo.

Atavala chiyero chaulemerero,

kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,

udzalandira mame a unyamata wako.

4Yehova walumbira

ndipo sadzasintha maganizo ake:

“Ndiwe wansembe mpaka muyaya

monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

5Ambuye ali kudzanja lako lamanja;

Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.

6Adzaweruza anthu a mitundu ina,

adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.

7Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;

choncho adzaweramutsa mutu wake.