Mmɛbusɛm 24 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Mmɛbusɛm 24:1-34

1Mma wʼani mmerɛ amumuyɛfoɔ,

mfa wo ho mmɔ wɔn;

2Ɛfiri sɛ, wɔn akoma dwene atirimuɔdensɛm ho,

na wɔn ano ka deɛ ɛde basabasayɛ ba ho asɛm.

3Wɔde nyansa na ɛsi efie,

na nhunumu mu na wɔma ɛtim;

4ɛnam nimdeɛ so na wɔnya ademudeɛ a ɛho yɛ na

na ɛyɛ fɛ hyehyɛ nʼadan mu.

5Onyansafoɔ wɔ tumi a ɛso,

na onimdefoɔ nyini ahoɔden mu;

6deɛ ɔretu sa hia akwankyerɛ,

deɛ ɔrepɛ nkonimdie no hia afotufoɔ pii.

7Nyansa wɔ akyiri dodo ma ɔkwasea;

wɔ apono ano dwabɔ mu no ɔnni hwee ka.

8Onipa ɔbɔ pɔ bɔne no

wɔbɛfrɛ no ɔkɔtwebrɛfoɔ.

9Ogyimifoɔ nhyehyɛeɛ yɛ bɔne,

nnipa kyiri ɔfɛdifoɔ.

10Sɛ wʼabamu go wɔ ɔhaw mu a,

na wʼahoɔden sua!

11Gye wɔn a wɔde wɔn rekɔ akɔkum wɔn no nkwa;

na sianka wɔn a wɔtɔ ntintan kɔ akumiiɛ.

12Sɛ woka sɛ, “Na yɛnnim yei ho hwee a,”

deɛ ɔkari akoma hwɛ no nhunu anaa?

Deɛ ɔbɔ wo nkwa ho ban no nnim anaa?

Ɔrentua deɛ obiara ayɛ so ka anaa?

13Me ba, di ɛwoɔ, ɛfiri sɛ ɛyɛ;

ɛwokyɛm mu woɔ yɛ wʼanomu dɛ.

14Hunu nso sɛ nyansa yɛ wo kra dɛ;

sɛ wonya a, wowɔ anidasoɔ ma daakye,

na wʼanidasoɔ renyɛ kwa.

15Nkɔtɛ ɔteneneeni fie sɛ ɔkwanmukafoɔ,

na ɛnkɔto nhyɛ nʼatenaeɛ so,

16Ɛwom sɛ ɔteneneeni hwe ase mpɛn nson deɛ, nanso ɔsɔre bio,

na amumuyɛfoɔ deɛ, amanehunu baako ma wɔhwe ase.

17Sɛ wo ɔtamfoɔ hwe ase a mma ɛnyɛ wo dɛ;

na sɛ ɔsunti a mma wʼakoma nni ahurisie,

18ɛfiri sɛ Awurade bɛhunu wʼadwene na ɔrempɛ

na ɔbɛyi nʼabufuhyeɛ afiri ne so.

19Ɛnha wo ho wɔ abɔnefoɔ enti

na ɛmma wʼani mmere amumuyɛfoɔ nso,

20ɛfiri sɛ, ɔbɔnefoɔ nni anidasoɔ biara daakye,

na wɔbɛdum amumuyɛfoɔ kanea.

21Me ba, suro Awurade ne ɔhene,

na mfa wo ho mmɔ adɔnyɛfoɔ ho,

22ɛfiri sɛ saa baanu yi de ɔsɛeɛ bɛba wɔn so mpofirim,

na hwan na ɔnim amanehunu ko a wɔbɛtumi de aba?

Anyansafoɔ Nsɛnka A Ɛkeka Ho

23Yeinom nso yɛ anyansafoɔ Nsɛnka:

Atemmuo a animhwɛ wɔ mu no nyɛ:

24Obiara a ɔbɛka akyerɛ deɛ ɔdi fɔ sɛ, “Wo ho nni asɛm” no

nnipa bɛdome no na amanaman remmɔ no din pa.

25Na wɔn a wɔbu afɔdifoɔ fɔ no ɛbɛsi wɔn yie,

na nhyira bɛba wɔn so.

26Mmuaeɛ pa

te sɛ mfeano.

27Wie wo mfikyidwuma

na siesie wo mfuo;

ɛno akyi, si wo fie.

28Nni adanseɛ ntia ɔyɔnko a ɔnyɛɛ wo hwee,

na mfa wʼano nnaadaa.

29Nka sɛ, “Deɛ wayɛ me no me nso mɛyɛ no bi;

deɛ ɔyɛeɛ no metua ne so ka.”

30Menante faa onihafoɔ afuo ho

twaa mu wɔ deɛ ɔnni adwene bobefuo nso ho;

31nkasɛɛ afu wɔ baabiara,

wira afu akata asase no so,

na aboɔ afasuo no nso abubu.

32Mede mʼadwene kɔɔ deɛ mehunuiɛ no so

na mesuaa biribi firii mu:

33nna kakra, nkotɔ kakra,

nsa a woabobɔ de rehome kakra,

34bɛma ohia aba wo so sɛ ɔkwanmukafoɔ

na nneɛma ho nna bɛba wo so sɛ obi a ɔkura akodeɛ. Na ohia bɛto akyere wo sɛ ɔkwanmukafoɔ; ahokyere bɛtoa wo sɛ ɔkorɔmfoɔ.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 24:1-34

1Usachitire nsanje anthu oyipa,

usalakalake kuti uzikhala nawo,

2pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa,

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.

3Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru,

ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;

4Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake

ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.

5Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri,

ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.

6Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo.

Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.

7Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru;

chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.

8Amene amakonzekera kuchita zoyipa

adzatchedwa mvundulamadzi.

9Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo,

ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.

10Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti

mphamvu yako ndi yochepadi!

11Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe;

uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.

12Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,”

kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi?

Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi?

Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?

13Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino;

uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.

14Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako;

ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo,

ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.

15Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa.

Usachite nayo nkhondo nyumba yake;

16paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso.

Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.

17Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako.

Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.

18Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo,

angaleke kukwiyira mdaniyo.

19Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa

kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,

20paja munthu woyipa alibe tsogolo.

Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.

21Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu,

ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,

22awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi.

Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?

Malangizo Enanso a Anthu Anzeru

23Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa:

Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:

24Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,”

anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.

25Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino

ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.

26Woyankhula mawu owona

ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.

27Ugwiriretu ntchito zako zonse,

makamaka za ku munda

ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.

28Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa,

kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.

29Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine;

ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”

30Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi

ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.

31Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga,

mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa,

ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.

32Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga

ndipo ndinatolapo phunziro ili:

33Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,”

kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”

34umphawi udzafika pa iwe ngati mbala

ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.