Hiob 4 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Hiob 4:1-21

Elifas Mmuaeɛ A Ɛdi Ɛkan

1Na Temanni Elifas buaa Hiob sɛ,

2“Sɛ obi pɛ sɛ ɔne wo kasa a, worennya ntoboaseɛ mma no anaa?

Hwan na wɔbɛtumi aka nʼano ato mu?

3Dwene sɛdeɛ wakyerɛkyerɛ nnipa bebree,

sɛdeɛ woahyɛ nsa a emu ayɛ mmerɛ den.

4Wo nsɛm ahyɛ wɔn a wɔasunti no den;

woahyɛ nkotodwe a ayɛ mmerɛ mu den.

5Na afei a ɔhaw aba no, wʼaba mu abu;

aba wo so, na wo ho adwiri wo.

6Wo nyamesuro mma wo ahotosoɔ anaa,

na wʼakwan a ɛho nni asɛm mma wo anidasoɔ anaa?

7“Dwene ho: Wɔasɛe obi a ne ho nni asɛm pɛn anaa?

Ɛhefa na wɔsɛee obi a ɔyɛ pɛ?

8Sɛdeɛ mahunu no, wɔn a wɔfɛntɛm bɔne

ne wɔn a wɔdua ɔhaw no, wɔtwa so aba.

9Sɛ Onyankopɔn home a, wɔsɛe;

nʼabufuo ma wɔyera.

10Agyata bɛtumi abobom na wɔapɔ so,

nanso wɔbɛbubu gyata akɛseɛ no se.

11Gyata annya haboa a ɔwu,

na gyatabereɛ mma no bɔ hwete.

12“Wɔbɛkaa kokoamsɛm bi kyerɛɛ me

na mʼaso tee no sɛ asomusɛm.

13Wɔ anadwo daeɛso basabasa mu,

ɛberɛ a nnipa adeda nnahɔɔ no,

14ehu ne nketenkete kyeree me.

Ɛmaa me nnompe nyinaa wosoeɛ.

15Honhom bi twaa mʼani so,

na me ho nwi sɔre gyinaeɛ.

16Ɛgyinaeɛ,

nanso, manhunu nʼabɔsuo.

Biribi bɛgyinaa mʼanim,

na metee nne bɔkɔɔ bi a ɛrebisa sɛ,

17‘Onipa dasani bɛtumi atene asene Onyankopɔn?

Onipa bɛtumi ayɛ kronn asene ne Yɛfoɔ anaa?

18Sɛ Onyankopɔn ntumi mfa ne ho nto nʼankasa asomfoɔ so,

na sɛ ɔka nʼabɔfoɔ mpo anim a,

19hwan ne onipa a wɔde dɔteɛ anwene no,

a ne fapem sisi mfuturo mu

na wɔdwerɛ no ntɛm so sene abubummabaa?

20Ɛfiri anɔpahema kɔsi anwummerɛ wɔbubu wɔn mu nketenkete;

na wɔyera korakora a obiara nhunu wɔn bio.

21Wɔtete wɔn ntomadan nhoma mu,

ɛno enti wɔwuwu a wɔnnim.’

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 4:1-21

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?

Koma ndani angakhale chete wosayankhula?

3Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,

momwe walimbitsira anthu ofowoka.

4Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;

unachirikiza anthu wotha mphamvu.

5Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,

zakukhudza ndipo uli ndi mantha.

6Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?

Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

7“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?

Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?

8Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,

ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.

9Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;

amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.

10Mikango imabangula ndi kulira,

komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.

11Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,

ndipo ana amkango amamwazikana.

12“Mawu anabwera kwa ine mwamseri,

makutu anga anamva kunongʼona kwake.

13Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,

nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,

14ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera

ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.

15Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,

ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.

16Chinthucho chinayimirira

koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.

Chinthu chinayima patsogolo panga,

kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,

17‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?

Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?

18Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,

ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,

19nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,

amene maziko awo ndi fumbi,

amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!

20Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;

mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.

21Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,

kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’