Hiob 39 – ASCB & CCL

Asante Twi Contemporary Bible

Hiob 39:1-30

1“Wonim ɛberɛ a bepɔ so mmirekyie wowoɔ?

Woahwɛ, ahunu ɛberɛ a ɔforoteɛ nyinsɛn ne ba?

2Woakane abosome dodoɔ a wɔde nyinsɛn?

Wonim ɛberɛ a wɔwoɔ anaa?

3Wɔkoto wowo wɔn mma;

na wɔn awokoɔ yea to twa.

4Wɔn mma nyini ahoɔden so wɔ wiram;

na wɔgya wɔn awofoɔ hɔ a wɔnnsane nkɔ wɔn nkyɛn bio.

5“Hwan na ɔma wiram afunumu fa ne ho die?

Hwan na ɔsanee ne nhoma?

6Mede asase bonini maa no sɛ ne fie,

ne nkyene asase tamaa sɛ nʼatenaeɛ.

7Ɔsere kurom gyegyeegyeyɛ no;

na ɔnte ɔkafoɔ nteateam.

8Ɔkyinkyini mmepɔ no so sɛ nʼadidibea;

ɛhɔ na ɔkyin hwehwɛ wira mono biara.

9“Ɛkoɔ bɛpene sɛ ɔbɛsom wo anaa?

Ɔbɛtena wo mmoa adididaka nkyɛn anadwo anaa?

10Wobɛtumi asa no wɔ fentemfidie so?

Ɔbɛfentem mmɔnhwa a ɛda wʼakyi anaa?

11Wobɛtumi de wo ho ato no so ɛsiane nʼahoɔden dodoɔ nti?

Wobɛgya wʼadwuma a ɛyɛ den ama no anaa?

12Wogye di sɛ ɔde wʼaburo bɛba

na waboa ano de akɔ ayuporobea anaa?

13“Sohori bɔ nʼataban mu anigyeɛ so,

nanso wɔntumi mfa ntoto asukɔnkɔn deɛ ho.

14Ɔto ne nkosua gu asase so

ma mfuturo ka no hye,

15ɛmfa ne ho sɛ ɛnan bi bɛpɛkyɛ no,

sɛ wiram aboa bi bɛtiatia so.

16Ɔbɔ ne mma atirimuɔden sɛdeɛ wɔnnyɛ ne dea;

ɛmfa ne ho sɛ nʼadwuma bɛyɛ kwa,

17ɛfiri sɛ Onyankopɔn amma no nyansa,

wamma no nhunumu biara.

18Nanso sɛ ɔtrɛ ne ntaban mu tu mmirika a,

ɔsere ɔpɔnkɔ ne ne sotefoɔ.

19“Wo na woma ɔpɔnkɔ no nʼahoɔden

anaa wode ne kɔn mu nwi kuhaa no ma no?

20Wo na woma no huri te sɛ ntutummɛ,

na ɔde ne nkorɔmo hunahuna anaa?

21Ɔde ne nan tintim fam denden, na nʼani gye nʼahoɔden mu,

na afei ɔbɔ wura ɔko mu.

22Ɔmmɔ hu, na ɔnsuro biribiara;

ɔhunu akofena a ɔnnwane.

23Bɛmma woso wɔ ne nkyɛn mu bɔha mu,

na pea ne pɛmɛ nso di ahim wɔ ne ho.

24Ɔfiri ahopereɛ mu de nʼano sisi fam;

na sɛ wɔhyɛn totorobɛnto a, ɔntumi nnyina faako.

25Sɛ totorobɛnto hyɛne a ɔka sɛ, ‘Wiɛɛ!’

ɔte ɔko ho hwa firi akyirikyiri,

ɔsahene no nteamu ne ɔko mu osebɔ.

26“Wo nyansa na ɛma akorɔma tuo

na ɔtrɛ ne ntaban mu fa anafoɔ?

27Wo na wohyɛ ɔkɔdeɛ ma no tu kɔ sorosoro

kɔyɛ ne pirebuo wɔ hɔ?

28Ɔbotan mu na ɔteɛ na ɛhɔ na ɔda;

ɔbotan sorɔnsorɔn yɛ nʼabandenden.

29Ɛhɔ na ɔfiri kɔpɛ nʼaduane;

nʼani hunu adeɛ a ɛwɔ akyirikyiri.

30Mogya yɛ ne mma aduane,

na baabi a atɔfoɔ wɔ no, ɛhɔ na ɔwɔ.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 39:1-30

1“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera?

Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?

2Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere?

Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?

3Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo;

pamenepo ululu wobereka nʼkutha.

4Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo;

kenaka amachoka ndipo sabwereranso.

5“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera?

Ndani amamasula zingwe zake?

6Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake,

nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo

7Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda;

ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.

8Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu

ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.

9“Kodi njati ingavomere kukutumikira?

Kodi ingagone mu gome lako usiku?

10Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima?

Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?

11Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake?

Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?

12Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako

ndi kumuyika ku malo opunthira?

13“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira,

koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.

14Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi

ndipo amafundidwa ndi nthaka,

15nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa,

ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.

16Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake;

Imayiwala zoti inavutika powabala.

17Chifukwa Mulungu anayimana nzeru,

simvetsa kanthu kalikonse.

18Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga,

imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.

19“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo

kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?

20Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira,

ukali wake nʼkumachititsa mantha?

21Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake,

ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.

22Iye sachita mantha, saopa chilichonse;

sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.

23Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake

pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.

24Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha;

satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.

25Lipenga likalira amati, ‘Twee!’

Amamva fungo la nkhondo ali patali,

kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.

26“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako,

ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?

27Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka

ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?

28Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku;

chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.

29Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye;

maso ake amachionera patali chinthucho.

30Ana ake amayamwa magazi,

ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”