Mmebusɛm 2 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Mmebusɛm 2:1-22

Nyansa So Mfaso Wɔ Abrabɔ Mu

1Me ba, sɛ wutie me nsɛm,

na woma me mmaransɛm tena wo mu a,

2sɛ wowɛn wʼaso ma nyansa

na wode wo koma ma ntease,

3na woma wo nne so frɛ nhumu

na wusu frɛ ntease,

4na sɛ wohwehwɛ no te sɛnea wohwehwɛ dwetɛ

na wohwehwɛ no sɛnea worepɛ ademude a ahintaw a,

5ɛno na wobɛte Awurade suro ase

na woahu Onyankopɔn ho nimdeɛ.

6Awurade ma nimdeɛ,

na nʼanom na nyansa ne ntease fi ba.

7Ɔkora nkonimdi ma wɔn a wɔteɛ,

ɔyɛ kyɛm ma wɔn a wɔn akwan yɛ pɛ,

8ɔwɛn nea ɔyɛ pɛ kwan,

na ɔbɔ wɔn a wodi no nokware no akwan ho ban.

9Ɛno na wobɛte nea eye ne nea ɛyɛ pɛ,

ne nea ɛfata, ɔkwan biara a eye ase.

10Afei nyansa bewura wo koma mu,

na nimdeɛ ayɛ ahomeka ama wo kra.

11Adwene bɛbɔ wo ho ban

na ntease ahwɛ wo so.

12Nyansa beyi wo afi amumɔyɛfo akwan mu,

ebeyi wo afi nnipa a wɔn nsɛm yɛ basabasa nsam,

13wɔn a wɔaman afi akwan pa so

akɔnantew sum akwan so no,

14wɔn a wɔn ani gye bɔneyɛ ho,

na wodi ahurusi wɔ bɔne mu basabasayɛ ho,

15wɔn a wɔn akwan yɛ kɔntɔnkye

na wɔyɛ abonsam wɔ wɔn akwan mu.

16Nimdeɛ begye wo afi ɔbea waresɛefo no nsam,

afi ɔbea warefo huhuni a ɔka nnaadaasɛm ho,

17nea wagyaa ne mmabaabere mu kunu

na wapo apam a ɔyɛɛ wɔ Onyankopɔn anim no.

18Ne fi yɛ ɔkwan a ɛkɔ owu mu

na nʼakwan kɔ awufo honhom nkyɛn.

19Obiara a ɔkɔ ne nkyɛn no nsan mma

anaasɛ ɔrensi nkwa akwan so.

20Enti wubedi nnipa pa anammɔn akyi

na woanantew atreneefo akwan so.

21Efisɛ wɔn a wɔteɛ bɛtena asase no so,

na wɔn a asɛm nni wɔn ho no na wɔbɛka hɔ;

22na wobetwa amumɔyɛfo afi asase no so,

na wɔatɔre atorofo ase.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 2:1-22

Ubwino Wanzeru

1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga

ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,

2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru

ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;

3ngati upempha kuti uzindikire zinthu

inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,

4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva

ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,

5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;

ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.

6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,

ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.

7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.

Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,

8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.

Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,

kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.

10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,

kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.

11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;

kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,

kwa anthu amabodza,

13amene amasiya njira zolungama

namayenda mʼnjira zamdima,

14amene amakondwera pochita zoyipa

namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.

15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,

ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;

kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,

17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake

ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.

18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;

njira zake zimamufikitsa ku manda.

19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera

kapena kupezanso njira zamoyo.

20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,

uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.

21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko

ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;

22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,

ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.