Botae Ne Nsɛmpɔw
1Dawid babarima Salomo, Israelhene, mmebusɛm ni:
2Ne botae ne sɛ ɛbɛkyerɛ nnipa nyansa ne ahohyɛso;
ne sɛ ɛbɛboa ama wɔate nsɛm a emu dɔ ase;
3sɛ wobenya akwankyerɛ wɔ abrabɔ pa mu,
a ɛbɛma wɔayɛ ade pa, nea ɛteɛ na ho nni asɛm;
4sɛ ɛbɛma nea nʼadwene mu nnɔ anya nyansa
na mmabun anya nimdeɛ ne adwene,
5anyansafo ntie na wɔmfa nka nea wonim ho,
na nea ɔwɔ nhumu nya akwankyerɛ a
6ɛbɛma wate mmɛ ne kasammebu,
anyansafo nsɛnka ne abisaa ase.
7Awurade suro yɛ nimdeɛ mfiase,
na nkwaseafo bu nyansa ne ahohyɛso animtiaa.
Nyansapɛ Ho Afotusɛm
Nnaadaa Ho Kɔkɔbɔ
8Me ba, tie wʼagya akwankyerɛ
na mpo wo na nkyerɛkyerɛ.
9Ɛbɛyɛ wo ti anuonyam abotiri
ne wo kɔn mu atweaban.
10Me ba, sɛ nnebɔneyɛfo twetwe wo a,
mma wɔn ho kwan.
11Sɛ wɔka se, “Bra ma yɛnkɔ;
ma yɛnkɔtetɛw na yenkum obi,
ma yɛnkɔtɛw ntwɛn mmɔborɔni bi;
12ma yɛmmemene wɔn anikann sɛ ɔda,
koraa, te sɛ wɔn a wɔkɔ ɔda mu;
13yebenya nneɛma a ɛsom bo ahorow
na yɛde asade ahyɛ yɛn afi ma;
14fa wo ho bɛhyɛ mu,
na wubenya wo kyɛfa wɔ ahonyade no mu.”
15Me ba, wo ne wɔn nnantew,
mfa wo nan nsi wɔn akwan so;
16Wɔn anan de ntɛmpɛ kɔ bɔne mu,
na wɔde ahoɔhare ka mogya gu.
17So nni mfaso sɛ obi besum nnomaafiri
wɔ beae a anomaa biara hu!
18Saa nnipa yi tetɛw pɛ wɔn ankasa mogya;
wɔtetɛw wɔn ankasa wɔn ho!
19Saa na wɔn a wodi akorɔnne akyi no awiei te;
ɛma wɔhwere wɔn nkwa!
Nyansa A Wɔpo Ho Kɔkɔbɔ
20Nyansa teɛ mu wɔ mmɔnten so,
ɔma ne nne so wɔ aguabɔbea,
21ɔteɛ mu wɔ afasu no atifi,
ɔkasa wɔ kuropɔn no apon ano se,
22“Mo adwenharefo, mobɛyɛ adwenhare akosi da bɛn?
Fɛwdifo bedi fɛw akosi da bɛn?
Nkwaseafo bekyi nimdeɛ akosi da bɛn?
23Sɛ mutiee mʼanimka a,
anka mekaa me koma mu nsɛm nyinaa kyerɛɛ mo
ma muhuu me nsusuwii.
24Nanso sɛ muyii mo aso, bere a mefrɛɛ mo
na amfa obiara ho, bere a meteɛɛ me nsa mu,
25sɛ mopoo mʼafotu,
na moampɛ mʼanimka nti,
26me nso mɛserew mo wɔ mo amanehunu mu;
sɛ abɛbrɛsɛ bi bu fa mo so a, midi mo ho fɛw,
27sɛ abɛbrɛsɛ bi bu fa mo so te sɛ ahum,
na amanehunu bi bɔ fa mo so sɛ mfɛtɛ,
na awerɛhow ne ɔhaw mene mo a,
28“Afei wɔbɛfrɛ me, nanso meremmua;
wɔbɛhwehwɛ me, nanso wɔrenhu me.
29Esiane sɛ wokyii nimdeɛ
na wɔampɛ sɛ wobesuro Awurade,
30sɛ wɔpoo mʼafotu,
na wobuu me nteɛso animtiaa nti,
31wobedi wɔn akwan so aba;
na wɔn nhyehyɛe mu aduan bɛmee wɔn.
32Na ntetekwaafo asoɔden bekum wɔn,
na nkwaseafo tirimudɛ bɛsɛe wɔn;
33Nanso obiara a obetie me no, ɔbɛtena ase asomdwoe mu
na ne ho bɛtɔ no a ɔrensuro ɔhaw biara.”
Mawu Oyamba: Cholinga ndi Mutu
1Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo;
kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru,
akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera,
achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake,
ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo,
mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru.
Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
Malangizo kuti Asunge Nzeru
Malangizo kwa Achinyamata
8Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako
ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako
ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa
usamawamvere.
11Akadzati, “Tiye kuno;
tikabisale kuti tiphe anthu,
tikabisalire anthu osalakwa;
12tiwameze amoyo ngati manda,
ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje.
13Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali
ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14Bwera, chita nafe maere,
ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15Mwana wanga, usayende nawo pamodzi,
usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha,
amathamangira kukhetsa magazi.
17Nʼkopanda phindu kutchera msampha
mbalame zikuona!
18Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe;
amangodzitchera okha msampha!
19Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza;
chumacho chimapha mwiniwake.
Chenjezo Pomwe Tikana Nzeru
20Nzeru ikufuwula mu msewu,
ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21ikufuwula pa mphambano ya misewu,
ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti?
Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti?
Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23Tamverani mawu anga a chidzudzulo.
Ine ndikukuwuzani maganizo anga
ndi kukudziwitsani mawu anga.
24Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera.
Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25Uphungu wanga munawunyoza.
Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto;
ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe,
tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu,
mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha;
mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29Popeza iwo anadana ndi chidziwitso
ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30popeza iwo sanasamale malangizo anga
ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo
ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo,
ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata;
adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”