1 Mose 49 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

1 Mose 49:1-33

Yakob Hyira Ne Mmabarima

1Yakob frɛɛ ne mmabarima nyinaa ka kyerɛɛ wɔn se, “Mummetwa me ho nhyia, na menka mo nea ɛbɛba mo so daakye.

2“Yakob mmabarima, mommoaboa mo ho ano, na muntie;

muntie mo agya Israel.

3“Ruben, wo na woyɛ mʼabakan.

Wo na woyɛ me tumi ne mʼahoɔden nsɛnkyerɛnne a edi kan a

ɛboro anuonyam ne tumi so.

4Woyɛ kitikiti sɛ asorɔkye, nanso worenkɔ so bio,

efisɛ woforoo wʼagya mpa ne ne yere kɔdae,

de guu mʼanim ase.

5“Simeon ne Lewi yɛ anuanom.

Wogyina hɔ ma basabasayɛ ne asisi.

6Mma me nkɔka wɔn agyinatu ho,

efisɛ wɔnam wɔn abufuw so akunkum nnipa,

na wokunkum anantwi de gyee wɔn ani.

7Nnome nka wɔn abufuw, efisɛ ano yɛ den,

na ɛyɛ atirimɔdensɛm!

Ɛno nti, mɛbɔ wɔn asefo ahwete

Israelman mu nyinaa.

8“Yuda, wo nuabarimanom beyi wo ayɛ.

Wobɛsɛe wʼatamfo nyinaa.

Wʼagya mmabarima bɛkotow wo.

9Yuda, woyɛ gyata ba a

woawe wʼatamfo nam awie.

Wote sɛ gyata a wabutuw.

Hena na obetumi akɔka no?

10Ahempema remfi Yuda nsam,

na saa ara nso na ahempema remfi nʼanan ntam,

kosi sɛ, nea ɛyɛ ne dea a aman nyinaa betie no no bɛba.

11Ɔbɛsa nʼafurum wɔ bobe dua mu.

Ɔde nʼafurum ba bɛsa bobe pa mman mu.

Ɔbɛhoro ne ntama wɔ nsa mu,

na wahoro nʼatade nso wɔ bobesa kɔɔ mu.

12Nʼaniwa aba bebiri asen bobesa.

Ne se bɛyɛ fitaa asen nufusu.

13“Sebulon bɛtena mpoano.

Obesisi ahyɛngyinabea ama ahyɛn.

Nʼahye so bɛtrɛw akosi Sidon.

14“Isakar yɛ afurum hoɔdenfo a

obutuw hɔ rehome wɔ nguankuw mu.

15Sɛ ohu sɛnea nʼahomegyebea ye fa,

ne sɛnea nʼasase no so dwo a,

obekuntun agye adesoa,

na wapene so sɛ akoa ama ɔhyɛ adwuma.

16“Dan bebu ne manfo atɛn

sɛ Israel mmusuakuw no baako.

17Dan bɛyɛ sɛ ɔwɔ a ɔda kwankyɛn;

ɔbɛyɛ sɛ ahurutoa a ɔnam ɔtempɔn mu a

ɔka ɔpɔnkɔ nantin,

sɛnea ɛbɛma ne sotefo atew ahwe nʼakyi.

18Awurade, wo nkwagye na meretwɛn.

19“Nnipa bɔnefo bɛtow ahyɛ Gad so,

na ɔno nso betiw wɔn atow ahyɛ wɔn so.

20“Aser aduan a odi no bɛyɛ aduan pa.

Na ɔbɛma ahennuan a ɛyɛ akɔnnɔ.

21“Naftali te sɛ ɔforote a wɔagyaa no a

ɔwo mma ahoɔfɛfo.

22“Yosef yɛ ngodua a ɛsow aba,

a esi asuten ho,

na ne mman tra afasu.

23Agyantowfo kaa no hyɛe,

de abufuw tow hyɛɛ ne so.

24Nanso ne bɛma no gyinaa pintinn,

na ne basa mu yɛɛ den;

esiane Otumfo Nyankopɔn a Yakob som no no

a ɔyɛ oguanhwɛfo ne Israel botantim no;

25esiane Onyankopɔn a wʼagya som no a ɔboa wo no;

Otumfo a ɔde ɔsoro nhyira behyira wo;

nhyira a efi asase ase pɛɛ;

nhyira a efi nufu ne ɔyafunu mu no.

26Wʼagya nhyira a wɔahyira no no

bɛdɔɔso asen tete nteredee mmepɔw

ne nkoko a etintim hɔ daa no so nnɔbae.

Eyinom nyinaa mmra Yosef ti so,

engugu anuanom no mu nea wɔapaw no no anintɔn so.

27“Benyamin yɛ pataku a ɔyɛ nam;

ɔbɔ aporɔw anɔpa, kyere ne hanam we,

na edu anwummere a, ɔkyekyɛ nam nkae no.”

28Eyi ne nhyira a Israel mmusuakuw dumien no agya de hyiraa wɔn; obiara ne sɛnea ɛfata no.

Yakob Wu Ne Ne Sie

29Yakob rebewu no, ɔka kyerɛɛ wɔn hyɛɛ wɔn se, “Aka kakraa bi, na wɔrebɛfa me akɔka me mpanyimfo ho. Sɛ miwu a, munsie me wɔ ɔboda a ɛwɔ Hetini Efron afuw a wosiee me mpanyimfo wɔ mu no mu. 30Ɛno ne ɔboda ne afuw a ɛwɔ Makpela, a ɛbɛn Mamrɛ a ɛwɔ Kanaan asase so no. Abraham tɔɔ saa ɔboda no fii Hetini Efron nkyɛn, de yɛɛ amusiei. 31Saa ɔboda no mu na wosiee Abraham ne ne yere Sara. Ɛhɔ ara nso na wosiee Isak ne ne yere Rebeka, na misiee Lea nso. 32Me nena Abraham tɔɔ afuw no ne ɔboda a ɛka ho no nyinaa fii Hetifo no nkyɛn.”

33Bere a Yakob kasa kyerɛɛ ne mma no wiee no, ɔmaa ne nan so guu ne mpa so wui. Wokosiee no wɔ ne mpanyimfo nkyɛn.

The Word of God in Contemporary Chichewa

Genesis 49:1-33

Yakobo Adalitsa Ana ake Aamuna

1Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

2“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;

mverani abambo anu Israeli.

3“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;

mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga,

wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.

4Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,

iwe unagona pa bedi la abambo ako,

ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.

5“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,

anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.

6Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,

kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo,

pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo

ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.

7Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi

ndi ukali wawo wankhanza choterewu!

Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo

ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.

8“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;

dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako;

abale ako adzakugwadira iwe.

9Yuda ali ngati mwana wa mkango;

umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga.

Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi,

ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?

10Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,

udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse,

mpaka mwini wake weniweni atabwera

ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.

11Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,

ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino.

Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo;

ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.

12Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,

mano ake woyera chifukwa cha mkaka.

13“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;

adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi;

malire ake adzafika ku Sidoni.

14“Isakara ali ngati bulu wamphamvu

wogona pansi pakati pa makola.

15Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira

ndi kukongola kwa dziko lake,

iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake

ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.

16“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake

monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.

17Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,

songo yokhala mʼnjira

imene imaluma chidendene cha kavalo

kuti wokwerapoyo agwe chagada.

18“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,

koma iye adzawathamangitsa.

20“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,

ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.

21“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi

yokhala ndi ana okongola kwambiri.

22“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,

mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe,

nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.

23Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;

anamuthamangitsa ndi mauta awo.

24Koma uta wake sunagwedezeke,

ndi manja ake amphamvu aja analimbika,

chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo,

chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.

25Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;

chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa

ndi mvula yochokera kumwamba,

ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka,

ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.

26Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa

madalitso a mapiri akale

oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona.

Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe,

pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.

27“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;

umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha,

ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”

28Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

Kumwalira kwa Yakobo

29Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti. 30Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 31Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya. 32Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.