Biribiara Yɛ Adehuhuw
1Eyinom ne nsɛm a Ɔsɛnkafo, ɔhene Dawid babarima a ɔyɛ ɔhene wɔ Yerusalem se:
2“Ahuhude! Ahuhude!”
Ɔsɛnkafo no na ose.
“Ahuhude mu ahuhude
Biribiara yɛ ahuhude.”
3Dɛn na onipa nya fi nʼadwumayɛ nyinaa mu,
nea okum ne ho yɛ no owia so no?
4Awo ntoatoaso ba na ɛkɔ,
nanso asase tim hɔ daa.
5Owia pue na owia kɔtɔ,
na ɛyɛ ntɛm kɔ nea epue fii hɔ no.
6Mframa bɔ kɔ anafo fam
na ɛdan hwɛ atifi fam;
ekyinkyin kɔ baabiara,
na ɛsan bɔ fa ne kwan so.
7Nsubɔnten nyinaa sen kogu po mu,
nanso po nyɛ ma da.
Faako a nsubɔnten no fi no
hɔ na wɔsan kɔ bio.
8Biribiara yɛ ɔbrɛ
a ɛboro nea obi bɛka so.
Ani nhwɛ ade nwie da
na aso nso ntie nsɛm mma ɛnyɛ mma da.
9Nea aba no bɛba bio,
nea wɔayɛ no, wɔbɛyɛ bio;
ade foforo biara nni owia yi ase.
10Biribi wɔ hɔ a wobetumi aka wɔ ho se:
“Hwɛ! eyi yɛ ade foforo” ana?
Ɛwɔ hɔ dedaw fi tete nteredee;
ɛwɔ hɔ ansa na wɔwoo yɛn.
11Wɔnkae tetefo no,
na wɔn a wonnya nnwoo wɔn no nso,
wɔn a wobedi wɔn akyi no
renkae wɔn.
Nimdeɛ Yɛ Ahuhude
12Me, Ɔsɛnkafo, na meyɛ Israelhene wɔ Yerusalem. 13Mituu me ho sii hɔ sɛ mede nimdeɛ besua ayɛ nhwehwɛmu wɔ biribiara a wɔyɛ no owia yi ase ho. Adesoa duruduru a Onyankopɔn de ato adesamma so! 14Mahu biribiara a wɔyɛ no owia yi ase; ne nyinaa nka hwee, ɛte sɛnea obi tu mmirika taa mframa.
15Nea akyea no wontumi nteɛ;
na nea enni hɔ no wontumi nkan.
16Mekaa wɔ me tirim se, “Hwɛ, manyin na manya nimdeɛ bebree asen obiara a watena Yerusalem ahengua so ansa na merebedi ade. Manya nhumu ne nimdeɛ mu osuahu.” 17Afei meyɛɛ mʼadwene sɛ mɛhwehwɛ na mate nimdeɛ, ne adammɔsɛm ne nkwaseasɛm ase. Nanso mihuu sɛ eyi nso te sɛnea obi tu mmirika taa mframa.
18Nimdeɛ bebree de awerɛhow na ɛba;
nyansa dɔɔso a, awerɛhowdi dɔɔso.
Zapansipano Nʼzopandapake
1Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:
2“Zopandapake! Zopandapake!”
atero Mlaliki.
“Zopandapake kotheratu!
Zopandapake.”
3Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zake zonse
zimene amasautsidwa nazo pansi pano?
4Mibado imabwera ndipo mibado imapita,
koma dziko lapansi limakhalapobe nthawi zonse.
5Dzuwa limatuluka ndipo dzuwa limalowa
ndipo limapita mwamsanga kumene limatulukira.
6Mphepo imawombera cha kummwera
ndi kukhotera cha kumpoto;
imawomba mozungulirazungulira,
kumangobwererabwerera komwe yachokera.
7Mitsinje yonse imakathira ku nyanja,
koma nyanjayo sidzaza;
kumene madziwo amachokera,
amabwereranso komweko.
8Zinthu zonse ndi zotopetsa,
kutopetsa kwake ndi kosaneneka.
Maso satopa ndi kuona
kapena khutu kukwaniritsidwa ndi kumva.
9Zomwe zinalipo kale zidzakhalaponso,
zomwe zinachitika kale zidzachitikanso.
Ndiye kuti chatsopano palibiretu pansi pano.
10Kodi chilipo chinthu chimene wina anganene kuti,
“Taona! Ichi ndiye chatsopano?”
Chinalipo kale, kalekale;
chinalipo ife kulibe.
11Anthu akale sakumbukiridwa,
ngakhale amene adzabwera mʼtsogolomu
sadzakumbukiridwa ndi iwo
amene adzabwere pambuyo pawo.
Nzeru Nʼzopandapake
12Ine, Mlalikine, ndinali mfumu ya Israeli mu Yerusalemu. 13Ndinayika mtima wanga pophunzira ndi kufunafuna mwa nzeru zinthu zonse zimene zimachitika pansi pa thambo. Ndi ntchito yolemetsa ndithu imene Mulungu anayipereka kwa anthu! 14Ine ndaona zinthu zonse zochitika pansi pano; zinthu zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.
15Chinthu chokhota sichingathe kuwongoledwa;
chimene palibe sichingathe kuwerengedwa.
16Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Taona, ine ndakula ndi kukhala wa nzeru zochuluka kupambana aliyense amene analamulirapo Yerusalemu ndisanabadwe; ndaphunzira nzeru zochuluka ndi luntha.” 17Ndipo ndinadzipereka kuti ndithe kumvetsa kuti nzeru nʼchiyani, misala nʼchiyani, uchitsiru nʼchiyani, koma ndinazindikira ichi, kuti kuteronso nʼkungodzivuta chabe.
18Pakuti nzeru zochuluka zimabweretsa chisoni chochulukanso:
chidziwitso chochuluka, zowawa zochulukanso.