Masalimo 69:1-12
Salimo 69
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.”
Pulumutseni Inu Mulungu,
pakuti madzi afika mʼkhosi
Ine ndikumira mʼthope lozama
mʼmene mulibe popondapo.
Ndalowa mʼmadzi ozama;
mafunde andimiza.
Ndafowoka ndikupempha chithandizo;
kummero kwanga kwawuma gwaa,
mʼmaso mwanga mwada
kuyembekezera Mulungu wanga.
Iwo amene amadana nane popanda chifukwa
ndi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga;
ambiri ndi adani anga popanda chifukwa,
iwo amene akufunafuna kundiwononga.
Ndikukakamizidwa kubwezera
zomwe sindinabe.
Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu,
kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu.
Iwo amene amadalira Inu
asanyozedwe chifukwa cha ine,
Inu Ambuye Wamphamvuzonse.
Iwo amene amafunafuna Inu
asachititsidwe manyazi chifukwa cha ine,
Inu Mulungu wa Israeli.
Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu,
ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.
Ndine mlendo kwa abale anga,
munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga;
pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa
ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.
Pamene ndikulira ndi kusala kudya,
ndiyenera kupirira kunyozedwa;
pomwe ndavala chiguduli,
anthu amandiseweretsa.
Iwo amene amakhala pa chipata amandinena,
ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa.