Masalimo 69:1-12 CCL

Masalimo 69:1-12

Salimo 69

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.”

Pulumutseni Inu Mulungu,

pakuti madzi afika mʼkhosi

Ine ndikumira mʼthope lozama

mʼmene mulibe popondapo.

Ndalowa mʼmadzi ozama;

mafunde andimiza.

Ndafowoka ndikupempha chithandizo;

kummero kwanga kwawuma gwaa,

mʼmaso mwanga mwada

kuyembekezera Mulungu wanga.

Iwo amene amadana nane popanda chifukwa

ndi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga;

ambiri ndi adani anga popanda chifukwa,

iwo amene akufunafuna kundiwononga.

Ndikukakamizidwa kubwezera

zomwe sindinabe.

Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu,

kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu.

Iwo amene amadalira Inu

asanyozedwe chifukwa cha ine,

Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Iwo amene amafunafuna Inu

asachititsidwe manyazi chifukwa cha ine,

Inu Mulungu wa Israeli.

Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu,

ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.

Ndine mlendo kwa abale anga,

munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga;

pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa

ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.

Pamene ndikulira ndi kusala kudya,

ndiyenera kupirira kunyozedwa;

pomwe ndavala chiguduli,

anthu amandiseweretsa.

Iwo amene amakhala pa chipata amandinena,

ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa.

Read More of Masalimo 69