Masalimo 45:1-9 CCL

Masalimo 45:1-9

Salimo 45

Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe a “Maluwa a Kakombo.” Salimo la ana a Kora. Nyimbo ya pa ukwati.

Mtima wanga watakasika ndi nkhani yokoma

pamene ndikulakatula mawu anga kwa mfumu;

lilime langa ndi cholembera cha wolemba waluso.

Inu ndinu abwino kwambiri kuposa anthu onse

ndipo milomo yanu inadzozedwa ndi chikondi cha Mulungu chosasinthika,

popeza Mulungu wakudalitsani kwamuyaya.

Mangirirani lupanga lanu mʼchiwuno mwanu, inu munthu wamphamvu;

mudziveke nokha ndi ulemerero ndi ukulu wanu.

Mu ukulu wanu mupite mutakwera mwachigonjetso

mʼmalo mwa choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo;

dzanja lanu lamanja lionetsere ntchito zanu zoopsa.

Mivi yanu yakuthwa ilase mitima ya adani a mfumu,

mitundu ya anthu igwe pansi pa mapazi anu.

Mpando wanu waufumu, Inu Mulungu, udzakhala ku nthawi za nthawi;

ndodo yaufumu yachilungamo idzakhala ndodo yaufumu ya ufumu wanu.

Inu mumakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;

choncho Mulungu, Mulungu wanu, wakukhazikani pamwamba pa anzanu

pokudzozani ndi mafuta a chimwemwe.

Mikanjo yanu yonse ndi yonunkhira ndi mure ndi aloe ndi kasiya;

kuchokera ku nyumba zaufumu zokongoletsedwa ndi mnyanga wanjovu

nyimbo za zoyimbira zazingwe zimakusangalatsani.

Ana aakazi a mafumu ali pakati pa akazi anu olemekezeka;

ku dzanja lanu lamanja kuli mkwatibwi waufumu ali mu golide wa ku Ofiri.

Read More of Masalimo 45