Masalimo 10:1-11 CCL

Masalimo 10:1-11

Salimo 10

Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?

Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,

amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.

Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;

amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.

Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;

mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.

Zinthu zake zimamuyendera bwino;

iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;

amanyogodola adani ake onse.

Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.

Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”

Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;

zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.

Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,

kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,

amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.

Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.

Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;

amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.

Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;

amakhala pansi pa mphamvu zake.

Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,

wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

Read More of Masalimo 10