อิสยาห์ 20 – TNCV & CCL

Thai New Contemporary Bible

อิสยาห์ 20:1-6

คำพยากรณ์กล่าวโทษอียิปต์และคูช

1ในปีที่กษัตริย์ซาร์กอนแห่งอัสซีเรียส่งแม่ทัพสูงสุดมาโจมตีอัชโดดและยึดเมืองได้ 2ครั้งนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสผ่านอิสยาห์บุตรอาโมศว่า “เจ้าจงถอดเสื้อผ้ากระสอบออกจากกาย และถอดรองเท้าออก” อิสยาห์ก็ปฏิบัติตาม เดินเปลือยกายและเท้าเปล่า

3แล้วองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสว่า “เช่นเดียวกับที่อิสยาห์ผู้รับใช้ของเราเดินเปลือยกายและเท้าเปล่าตลอดสามปี ซึ่งเป็นหมายสำคัญและลางร้ายแก่อียิปต์และคูช20:3 คือ ตอนบนของลุ่มแม่น้ำไนล์ เช่นเดียวกับข้อ 4 และ 5 4กษัตริย์อัสซีเรียจะจับตัวชาวอียิปต์และคูชไปเป็นนักโทษและเป็นเชลย ให้เดินเปลือยกายและเท้าเปล่าไม่ว่าหนุ่มหรือแก่ กับเปลือยก้นยังความอัปยศมาสู่อียิปต์ 5บรรดาคนที่พึ่งคูชและโอ้อวดเรื่องอียิปต์จะหวาดกลัวและอับอาย 6ในวันนั้นประชาชนที่อาศัยตามชายฝั่งทะเลจะกล่าวว่า ‘ดูสิ ขนาดผู้ที่เราพึ่งพาและหนีมาขอความช่วยเหลือให้พ้นมือจากกษัตริย์อัสซีเรียยังเป็นไปถึงเพียงนี้ แล้วเราจะหนีรอดไปได้อย่างไร?’”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 20:1-6

Za Chilango cha Igupto ndi Kusi

1Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda, 2nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.

3Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi, 4momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto. 5Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi. 6Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’ ”