Salmo 137
1Junto aos rios da Babilônia nós nos sentamos e choramos
com saudade de Sião.
2Ali, nos salgueiros,
penduramos as nossas harpas;
3ali os nossos captores pediam-nos canções,
os nossos opressores exigiam canções alegres, dizendo:
“Cantem para nós uma das canções de Sião!”
4Como poderíamos cantar as canções do Senhor
numa terra estrangeira?
5Que a minha mão direita definhe,
ó Jerusalém, se eu me esquecer de ti!
6Que me grude a língua ao céu da boca,
se eu não me lembrar de ti
e não considerar Jerusalém
a minha maior alegria!
7Lembra-te, Senhor, dos edomitas
e do que fizeram quando Jerusalém foi destruída,
pois gritavam: “Arrasem-na!
Arrasem-na até aos alicerces!”
8Ó cidade137.8 Hebraico: filha. de Babilônia, destinada à destruição,
feliz aquele que lhe retribuir o mal que você nos fez!
9Feliz aquele que pegar os seus filhos
e os despedaçar contra a rocha!
Salimo 137
1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira
pamene tinakumbukira Ziyoni.
2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi
tinapachika apangwe athu,
3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.
Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;
iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova
mʼdziko lachilendo?
5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,
dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga
ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,
ngati sindiyesa iwe
chimwemwe changa chachikulu.
7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita
pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.
Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi
mpaka pa maziko ake!”
8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,
wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera
pa zimene watichitira.
9Amene adzagwira makanda ako
ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.