PRIMEIRO LIVRO
Salmo 1
1Como é feliz aquele
que não segue o conselho dos ímpios,
não imita a conduta dos pecadores,
nem se assenta na roda dos zombadores!
2Ao contrário, sua satisfação
está na lei do Senhor,
e nessa lei medita dia e noite.
3É como árvore plantada à beira de águas correntes:
Dá fruto no tempo certo
e suas folhas não murcham.
Tudo o que ele faz prospera!
4Não é o caso dos ímpios!
São como palha que o vento leva.
5Por isso os ímpios não resistirão no julgamento
nem os pecadores na comunidade dos justos.
6Pois o Senhor aprova o1.6 Ou cuida do; ou ainda conhece o caminho dos justos,
mas o caminho dos ímpios leva à destruição!
BUKU LOYAMBA
Masalimo 1–41
Salimo 1
1Wodala munthu
amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4Sizitero ndi anthu oyipa!
Iwo ali ngati mungu
umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.