Salmos 1 – NVI-PT & CCL

Nova Versão Internacional

Salmos 1:1-6

PRIMEIRO LIVRO

Salmo 1

1Como é feliz aquele

que não segue o conselho dos ímpios,

não imita a conduta dos pecadores,

nem se assenta na roda dos zombadores!

2Ao contrário, sua satisfação

está na lei do Senhor,

e nessa lei medita dia e noite.

3É como árvore plantada à beira de águas correntes:

Dá fruto no tempo certo

e suas folhas não murcham.

Tudo o que ele faz prospera!

4Não é o caso dos ímpios!

São como palha que o vento leva.

5Por isso os ímpios não resistirão no julgamento

nem os pecadores na comunidade dos justos.

6Pois o Senhor aprova o1.6 Ou cuida do; ou ainda conhece o caminho dos justos,

mas o caminho dos ímpios leva à destruição!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 1:1-6

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Salimo 1

1Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake

ndipo masamba ake safota.

Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.

4Sizitero ndi anthu oyipa!

Iwo ali ngati mungu

umene umawuluzidwa ndi mphepo.

5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,

kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,

koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.