Псалми 98 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 98:1-9

Псалам 98

Псалам.

1Певајте Господу нову песму,

јер је чудеса учинио!

Десница му донесе победу

и мишица његова света.

2Спасење је своје Господ обзнанио,

наочиглед народа је објавио праведност своју.

3Сетио се своје милости

и своје верности према дому Израиљевом,

и сви су крајеви земље

видели спасење Бога нашег.

4Ускликни Господу, земљо сва!

Подвикујте, запевајте и засвирајте!

5Засвирајте Господу уз харфу;

и уз харфу, и уз звуке песме.

6Уз трубе, уз јеку рогова

ускликните пред царем Господом!

7Нека хучи море и све што је у њему,

свет и његови становници.

8Нек рукама запљескају реке,

с њима горе нек радосно кличу

9пред Господом;

јер долази да суди земљи,

да поштено суди свету

и људима по правди.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 98:1-9

Salimo 98

Salimo.

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa;

dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera

zamuchitira chipulumutso.

2Yehova waonetsa chipulumutso chake

ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.

3Iye wakumbukira chikondi chake

ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli;

malekezero onse a dziko lapansi aona

chipulumutso cha Mulungu wathu.

4Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi,

muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.

5Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze,

ndi zeze ndi mawu a kuyimba,

6ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna

fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.

7Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,

dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.

8Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo,

mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;

9izo ziyimbe pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi.

Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo,

ndi mitundu ya anthu mosakondera.