Псалми 54 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 54:1-7

Псалам 54

Хоровођи, уз жичане инструменте. Давидова поучна песма, када су Зифејци дошли Саулу и рекли: „Не крије ли се Давид код нас?“

1Боже, именом ме својим спаси

и снагом ме својом ти одбрани.

2Боже, чуј молитву моју;

речи уста мојих послушај.

3Јер, против мене устају туђинци;

моју душу траже бездушници;

они Бога немају пред собом. Села

4Гле, Бог ми је помоћник;

Господ је међу онима што ми душу подупиру.

5Вратило се зло мрзитељу моме;

ти их сатри у верности својој.

6Радо ћу ти жртвовати;

хвалићу име твоје, Господе,

јер је добро.

7Јер оно ме је избавио из сваке невоље

и око ми победнички гледа противнике моје.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 54:1-7

Salimo 54

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

1Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;

onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.

2Imvani pemphero langa, Inu Mulungu

mvetserani mawu a pakamwa panga.

3Alendo akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,

anthu amene salabadira za Mulungu.

4Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;

Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

5Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;

mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

6Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;

ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,

pakuti ndi labwino.

7Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,

ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.