Псалми 52 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 52:1-9

Псалам 52

Хоровођи. Давидова поучна песма, када је Доик Едомац дошао и дојавио Саулу, рекавши му: „Давид је отишао у Ахимелекову кућу.“

1Што се хвалиш злобом, силниче?

Милост је Божија од јутра до сутра.

2Разарања ти смишља језик

попут бритве оштар,

о, превртљивче!

3Ти зло волиш више него добро,

и лаж више него право да говориш. Села

4Ти волиш све речи прождрљиве,

о, језиче обмањиви!

5Али тебе ће Бог довека оборити;

зграбиће те, од шатора отргнути;

из земље живих ишчупаће те. Села

6И видеће то праведници и бојаће се,

па ће му се смејати:

7„Гле човека што Бога није узео за тврђаву,

рушитеља силног,

што се поуздао у обиље свога блага!“

8А ја сам као зелена маслина

у Дому Божијем;

у милост се Божију уздам

од века до века.

9Хвалићу те у веке векова

за дела твоја;

надаћу се имену твоме

јер је добро пред твојим вернима.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 52:1-9

Salimo 52

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.”

1Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu?

Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse,

iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?

2Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena;

lilime lako lili ngati lumo lakuthwa,

ntchito yako nʼkunyenga.

3Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi.

Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona.

Sela

4Umakonda mawu onse opweteka,

iwe lilime lachinyengo!

5Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya:

iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako;

iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.

6Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha;

adzamuseka nʼkumanena kuti,

7“Pano tsopano pali munthu

amene sanayese Mulungu linga lake,

koma anakhulupirira chuma chake chambiri

nalimbika kuchita zoyipa!”

8Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi

wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu;

ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu

kwa nthawi za nthawi.

9Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita;

chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera

pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.