Псалми 47 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 47:1-9

Псалам 47

Хоровођи. Псалам потомака Корејевих.

1Сви народи, запљескајте длановима;

кличите Богу веселим узвиком!

2Јер је страшан Свевишњи Господ,

цар велики над свом земљом.

3Он нам је покорио народе

и људе под ноге наше.

4Наследство је за нас одабрао,

понос за Јакова кога воли. Села

5Подиже се Бог уз поклик;

Господ, уз звук трубе.

6Певајте славопоје Богу,

певајте славопоје;

певајте славопоје цару нашем,

певајте славопоје.

7Јер, Бог је цар целе земље;

певајте песму поучну.

8Бог влада над народима,

Бог столује на престолу свом светом.

9Племићи народа се окупљају,

са народом Бога Аврахамовог;

Божији су штитови земље

и он је преузвишен.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 47:1-9

Salimo 47

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Ombani mʼmanja, inu anthu onse;

fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.

2Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba;

Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!

3Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu;

anayika anthu pansi pa mapazi athu.

4Iye anatisankhira cholowa chathu,

chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda.

Sela

5Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe,

Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.

6Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando;

imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.

7Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi;

imbirani Iye salimo la matamando.

8Mulungu akulamulira mitundu ya anthu;

Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.

9Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana

monga anthu a Mulungu wa Abrahamu,

pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu;

Iye wakwezedwa kwakukulu.