Псалми 121 – NSP & CCL

New Serbian Translation

Псалми 121:1-8

Псалам 121

Песма поклоничка.

1Своје очи ка горама дижем.

Одакле ће мени помоћ доћи?

2Доћи ће ми помоћ од Господа,

Саздатеља небеса и земље!

3Нози твојој да посрне не да,

твој заштитник задремати неће.

4Гле, не дрема и не спава

заштитник Израиља!

5Господ је заштитник твој!

Господ ти је сенка с твоје десне стране.

6Неће ти шкодити ни сунце по дану

ни месец по ноћи.

7Од свакога зла Господ ће те заштитити,

заштитиће душу твоју.

8Господ ће те заштитити када будеш одлазио

и кад будеш долазио,

од сада па довека!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 121:1-8

Salimo 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga ku mapiri;

kodi thandizo langa limachokera kuti?

2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

4Taonani, Iye amene amasunga Israeli

sadzawodzera kapena kugona.

5Yehova ndiye amene amakusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.

6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,

kapena mwezi nthawi ya usiku.

7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;

adzasunga moyo wako.

8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;

kuyambira tsopano mpaka muyaya.