Psalms 1 – NIVUK & CCL

New International Version – UK

Psalms 1:1-6

Book I

Psalms 1–41

Psalm 1

1Blessed is the one

who does not walk in step with the wicked

or stand in the way that sinners take

or sit in the company of mockers,

2but whose delight is in the law of the Lord,

and who meditates on his law day and night.

3That person is like a tree planted by streams of water,

which yields its fruit in season

and whose leaf does not wither –

whatever they do prospers.

4Not so the wicked!

They are like chaff

that the wind blows away.

5Therefore the wicked will not stand in the judgment,

nor sinners in the assembly of the righteous.

6For the Lord watches over the way of the righteous,

but the way of the wicked leads to destruction.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 1:1-6

BUKU LOYAMBA

Masalimo 1–41

Salimo 1

1Wodala munthu

amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,

kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,

kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.

2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova

ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.

3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake

ndipo masamba ake safota.

Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.

4Sizitero ndi anthu oyipa!

Iwo ali ngati mungu

umene umawuluzidwa ndi mphepo.

5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,

kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.

6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,

koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.