Psalms 137 – NIV & CCL

New International Version

Psalms 137:1-9

Psalm 137

1By the rivers of Babylon we sat and wept

when we remembered Zion.

2There on the poplars

we hung our harps,

3for there our captors asked us for songs,

our tormentors demanded songs of joy;

they said, “Sing us one of the songs of Zion!”

4How can we sing the songs of the Lord

while in a foreign land?

5If I forget you, Jerusalem,

may my right hand forget its skill.

6May my tongue cling to the roof of my mouth

if I do not remember you,

if I do not consider Jerusalem

my highest joy.

7Remember, Lord, what the Edomites did

on the day Jerusalem fell.

“Tear it down,” they cried,

“tear it down to its foundations!”

8Daughter Babylon, doomed to destruction,

happy is the one who repays you

according to what you have done to us.

9Happy is the one who seizes your infants

and dashes them against the rocks.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.