Psalms 133 – NIV & CCL

New International Version

Psalms 133:1-3

Psalm 133

A song of ascents. Of David.

1How good and pleasant it is

when God’s people live together in unity!

2It is like precious oil poured on the head,

running down on the beard,

running down on Aaron’s beard,

down on the collar of his robe.

3It is as if the dew of Hermon

were falling on Mount Zion.

For there the Lord bestows his blessing,

even life forevermore.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 133:1-3

Salimo 133

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Onani, nʼkokoma ndi kokondweretsa ndithu

pamene abale akhala pamodzi mwachiyanjano!

2Zili ngati mafuta amtengowapatali othiridwa pa mutu,

otsikira ku ndevu,

ku ndevu za Aaroni,

oyenderera mpaka mʼkhosi mwa mkanjo wake.

3Zili ngati mame a ku Heremoni

otsikira pa Phiri la Ziyoni.

Pakuti pamenepo Yehova amaperekapo dalitso,

ndiwo moyo wamuyaya.