Psalm 127
A song of ascents. Of Solomon.
1Unless the Lord builds the house,
the builders labor in vain.
Unless the Lord watches over the city,
the guards stand watch in vain.
2In vain you rise early
and stay up late,
toiling for food to eat—
for he grants sleep to127:2 Or eat— / for while they sleep he provides for those he loves.
3Children are a heritage from the Lord,
offspring a reward from him.
4Like arrows in the hands of a warrior
are children born in one’s youth.
5Blessed is the man
whose quiver is full of them.
They will not be put to shame
when they contend with their opponents in court.
Salimo 127
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni.
1Yehova akapanda kumanga nyumba,
omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe.
Yehova akapanda kulondera mzinda,
mlonda akanangolondera pachabe.
2Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa
ndi kusagona msanga madzulo,
kuvutikira chakudya choti mudye,
pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova,
ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja
mwa munthu wankhondo.
5Wodala munthu
amene motengera mivi mwake mwadzaza.
Iwo sadzachititsidwa manyazi
pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.