Psalms 126 – NIV & CCL

New International Version

Psalms 126:1-6

Psalm 126

A song of ascents.

1When the Lord restored the fortunes of126:1 Or Lord brought back the captives to Zion,

we were like those who dreamed.126:1 Or those restored to health

2Our mouths were filled with laughter,

our tongues with songs of joy.

Then it was said among the nations,

“The Lord has done great things for them.”

3The Lord has done great things for us,

and we are filled with joy.

4Restore our fortunes,126:4 Or Bring back our captives Lord,

like streams in the Negev.

5Those who sow with tears

will reap with songs of joy.

6Those who go out weeping,

carrying seed to sow,

will return with songs of joy,

carrying sheaves with them.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 126:1-6

Salimo 126

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,

tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;

malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.

Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,

“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu,

ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,

monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira,

adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira,

atanyamula mbewu yokafesa,

adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,

atanyamula mitolo yake.