Psalm 113
1Praise the Lord.113:1 Hebrew Hallelu Yah; also in verse 9
Praise the Lord, you his servants;
praise the name of the Lord.
2Let the name of the Lord be praised,
both now and forevermore.
3From the rising of the sun to the place where it sets,
the name of the Lord is to be praised.
4The Lord is exalted over all the nations,
his glory above the heavens.
5Who is like the Lord our God,
the One who sits enthroned on high,
6who stoops down to look
on the heavens and the earth?
7He raises the poor from the dust
and lifts the needy from the ash heap;
8he seats them with princes,
with the princes of his people.
9He settles the childless woman in her home
as a happy mother of children.
Praise the Lord.
Salimo 113
1Tamandani Yehova.
Mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
tamandani dzina la Yehova.
2Yehova atamandidwe,
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake,
dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse,
ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu,
Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6amene amawerama pansi kuyangʼana
miyamba ndi dziko lapansi?
7Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi
ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8amawakhazika pamodzi ndi mafumu,
pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake
monga mayi wa ana wosangalala.
Tamandani Yehova.