BOOK I
Psalms 1–41
Psalm 1
1Blessed is the one
who does not walk in step with the wicked
or stand in the way that sinners take
or sit in the company of mockers,
2but whose delight is in the law of the Lord,
and who meditates on his law day and night.
3That person is like a tree planted by streams of water,
which yields its fruit in season
and whose leaf does not wither—
whatever they do prospers.
4Not so the wicked!
They are like chaff
that the wind blows away.
5Therefore the wicked will not stand in the judgment,
nor sinners in the assembly of the righteous.
6For the Lord watches over the way of the righteous,
but the way of the wicked leads to destruction.
BUKU LOYAMBA
Masalimo 1–41
Salimo 1
1Wodala munthu
amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,
kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,
kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova
ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,
umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake
ndipo masamba ake safota.
Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4Sizitero ndi anthu oyipa!
Iwo ali ngati mungu
umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,
kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,
koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.