Esther 10 – NIV & CCL

New International Version

Esther 10:1-3

The Greatness of Mordecai

1King Xerxes imposed tribute throughout the empire, to its distant shores. 2And all his acts of power and might, together with a full account of the greatness of Mordecai, whom the king had promoted, are they not written in the book of the annals of the kings of Media and Persia? 3Mordecai the Jew was second in rank to King Xerxes, preeminent among the Jews, and held in high esteem by his many fellow Jews, because he worked for the good of his people and spoke up for the welfare of all the Jews.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Estere 10:1-3

Ukulu wa Mordekai

1Mfumu Ahasiwero anakhometsa msonkho mʼdziko lake lonse mpaka ku zilumba zonse. 2Ndipo ntchito zonse zochitika ndi mphamvu zake komanso ndi zonse zofotokoza za ukulu wa Mordekai, kukwezedwa kwake ndi mfumu, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Mediya ndi Peresiya? 3Pakuti Mordekai Myuda uja anali wachiwiri wa mfumu Ahasiwero. Kwa Ayuda onse Mordekai anali munthu wamkulu ndipo ankamukonda chifukwa ankachitira zabwino mtundu wake ndi kufunira mtendere abale ake.