Psalm 54 – NIRV & CCL

New International Reader’s Version

Psalm 54:1-7

Psalm 54

For the director of music. To be played on stringed instruments. A maskil of David when the men from Ziph had gone to Saul. They had said, “Isn’t David hiding among us?”

1God, save me by your power.

Set me free by your might.

2God, hear my prayer.

Listen to what I’m saying.

3Enemies who are proud are attacking me.

Mean people are trying to kill me.

They don’t care about God.

4But I know that God helps me.

The Lord is the one who keeps me going.

5My enemies tell lies about me.

Do to them the evil things they planned against me.

God, be faithful and destroy them.

6I will sacrifice an offering to you

just because I choose to.

Lord, I will praise your name

because it is good.

7You have saved me from all my troubles.

With my own eyes I have seen you win the battle over my enemies.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 54:1-7

Salimo 54

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

1Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;

onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.

2Imvani pemphero langa, Inu Mulungu

mvetserani mawu a pakamwa panga.

3Alendo akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,

anthu amene salabadira za Mulungu.

4Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;

Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

5Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;

mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

6Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;

ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,

pakuti ndi labwino.

7Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,

ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.