Psalm 3
A psalm of David when he ran away from his son Absalom.
1Lord, I have so many enemies!
So many people are rising up against me!
2Many are saying about me,
“God will not save him.”
3Lord, you are like a shield that keeps me safe.
You bring me honor. You help me win the battle.
4I call out to the Lord.
He answers me from his holy mountain.
5I lie down and sleep.
I wake up again, because the Lord takes care of me.
6I won’t be afraid even though tens of thousands
attack me on every side.
7Lord, rise up!
My God, save me!
Strike all my enemies in the face.
Break the teeth of sinful people.
8Lord, you are the one who saves.
May your blessing be on your people.
Salimo 3
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu.
1Inu Yehova, achulukadi adani anga!
Achulukadi amene andiwukira!
2Ambiri akunena za ine kuti,
“Mulungu sadzamupulumutsa.”
Sela
3Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza,
Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula
ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera.
Sela
5Ine ndimagona ndi kupeza tulo;
ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene
abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7Dzukani, Inu Yehova!
Pulumutseni, Inu Mulungu wanga.
Akantheni adani anga onse pa msagwada;
gululani mano a anthu oyipa.
8Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.
Madalitso akhale pa anthu anu.
Sela