Psalm 120 – NIRV & CCL

New International Reader’s Version

Psalm 120:1-7

Psalm 120

A song for those who go up to Jerusalem to worship the Lord.

1I call out to the Lord when I’m in trouble,

and he answers me.

2Lord, save me from people whose lips tell lies.

Save me from people whose tongues don’t tell the truth.

3What will the Lord do to you, you lying tongue?

And what more will he do?

4He will punish you with the sharp arrows of a soldier.

He will punish you with burning coals from a desert bush.

5How terrible it is for me to live in the tents of the people of Meshek!

How terrible to live in the tents of the people of Kedar!

6I have lived too long

among those who hate peace.

7I want peace.

But when I speak, they want war.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 120:1-7

Salimo 120

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,

ndipo Iye amandiyankha.

2Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,

ndi kwa anthu achinyengo.

3Kodi adzakuchitani chiyani,

ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?

4Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,

ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

5Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,

kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!

6Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati

pa iwo amene amadana ndi mtendere.

7Ine ndine munthu wamtendere;

koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.