Zaburi 69 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 69:1-36

Zaburi 69

Kilio Cha Kuomba Msaada Wakati Wa Dhiki

Kwa mwimbishaji. Mtindo wa “Yungiyungi.” Zaburi ya Daudi.

169:1 Za 42:7; 32:6; Yon 2:5Ee Mungu, niokoe,

kwa maana maji yamenifika shingoni.

269:2 Ay 30:19Ninazama kwenye vilindi vya matope,

pasipo mahali pa kukanyaga,

Nimefika kwenye maji makuu,

mafuriko yamenigharikisha.

369:3 Za 6:6; 119:82Nimechoka kwa kuomba msaada,

koo langu limekauka.

Macho yangu yanafifia,

nikimtafuta Mungu wangu.

469:4 Yn 15:25; Za 25:19; 35:19; 38:19; 40:14; 119:95; Isa 32:7Wale wanaonichukia bila sababu

ni wengi kuliko nywele za kichwa changu;

wengi ni adui kwangu bila sababu,

wale wanaotafuta kuniangamiza.

Ninalazimishwa kurudisha

kitu ambacho sikuiba.

569:5 Za 38:5; 44:21Ee Mungu, wewe unajua upumbavu wangu,

wala hatia yangu haikufichika kwako.

6Ee Bwana, ewe Bwana Mwenye Nguvu Zote,

wakutumainio wasiaibishwe

kwa ajili yangu;

wakutafutao wasifedheheshwe kwa ajili yangu,

Ee Mungu wa Israeli.

769:7 Yer 15:15; Za 39:8; 44:15Kwa maana nimestahimili dharau kwa ajili yako,

aibu imefunika uso wangu.

869:8 Ay 19:13-15; Za 31:11; 38:11; Isa 53:3; Yn 7:5Nimekuwa mgeni kwa ndugu zangu,

mgeni kwa wana wa mama yangu mwenyewe.

969:9 Yn 2:17; Rum 15:3; Za 89:50-51Kwa kuwa wivu wa nyumba yako unanila,

matukano ya wale wanaokutukana yameniangukia.

1069:10 Za 35:13Ninapolia na kufunga,

lazima nivumilie matusi.

1169:11 2Sam 3:31; Za 35:13Ninapovaa nguo ya gunia,

watu hunidharau.

1269:12 Mwa 18:1; 23:10; Ay 30:9Wale wanaoketi mlangoni wananisimanga,

nimekuwa wimbo wa walevi.

1369:13 Isa 49:8; 2Kor 6:2; Za 17:7; 51:1Lakini Ee Bwana, ninakuomba,

kwa wakati ukupendezao;

katika upendo wako mkuu, Ee Mungu,

unijibu kwa wokovu wako wa hakika.

1469:14 Za 69:2; 144:7Uniokoe katika matope,

usiniache nizame;

niokoe na hao wanichukiao,

kutoka kwenye vilindi vya maji.

1569:15 Za 36:6; 68:22; Hes 21:33; Yer 22:2069:15 Za 28:1; 124:4, 5; Hes 16:33Usiache mafuriko yanigharikishe

au vilindi vinimeze,

au shimo lifumbe kinywa chake juu yangu.

1669:16 Za 63:3Ee Bwana, unijibu, kwa wema wa upendo wako;

kwa huruma zako nyingi unigeukie.

1769:17 Za 22:24; 143:7; 50:15; 66:14Usimfiche mtumishi wako uso wako,

uharakishe kunijibu, kwa sababu niko katika shida.

1869:18 Za 49:15Njoo karibu uniokoe,

nikomboe kwa sababu ya adui zangu.

1969:19 Za 22:6Unajua jinsi ninavyodharauliwa,

kufedheheshwa na kuaibishwa,

adui zangu wote unawajua.

2069:20 Ay 16:2; Isa 63:5; Za 142:4Dharau zimenivunja moyo

na nimekata tamaa,

nimetafuta wa kunihurumia, lakini sikumpata,

wa kunituliza, lakini sikumpata.

2169:21 Hes 6:3; Lk 23:36; Mt 27:34, 48; Mk 15:23, 36; Yn 19:28-30Waliweka nyongo katika chakula changu

na walinipa siki nilipokuwa na kiu.

2269:22 1Sam 28:9; Ay 18:10Meza iliyoandaliwa mbele yao na iwe mtego,

nayo iwe upatilizo na tanzi.

2369:23 Rum 11:9-10Macho yao yatiwe giza ili wasiweze kuona,

nayo migongo yao iinamishwe daima.

2469:24 Za 79:6; Yer 10:25Uwamwagie ghadhabu yako,

hasira yako kali na iwapate.

2569:25 Law 26:43; Mt 23:38; Mdo 1:20Mahali pao na pawe ukiwa,

wala asiwepo yeyote atakayeishi katika mahema yao.

2669:26 Ay 19:22; Zek 1:15Kwa kuwa wanawatesa wale uliowajeruhi,

na kuzungumza juu ya maumivu ya wale uliowaumiza.

2769:27 Neh 4:5; Za 109:14Walipize uovu juu ya uovu,

usiwaache washiriki katika wokovu wako.

2869:28 Kut 32:32-33; Lk 10:20; Eze 13:9Wafutwe kutoka kitabu cha uzima

na wasiorodheshwe pamoja na wenye haki.

2969:29 Za 20:1Mimi niko katika maumivu na dhiki;

Ee Mungu, wokovu wako na unihifadhi.

3069:30 Za 28:7; 34:3Nitalisifu jina la Mungu kwa wimbo,

nami nitamtukuza kwa kumtolea shukrani.

3169:31 Za 50:9-13; 51:16Hili litampendeza Bwana kuliko ngʼombe dume,

zaidi ya fahali akiwa na pembe na kwato zake.

3269:32 Za 34:2; 22:26Maskini wataona na kufurahi:

ninyi mnaomtafuta Mungu, mioyo yenu na iishi!

3369:33 Za 12:5Bwana huwasikia wahitaji

wala hadharau watu wake waliotekwa.

3469:34 Za 96:11; 98:7; Isa 44:23Mbingu na dunia zimsifu,

bahari na vyote viendavyo ndani yake,

3569:35 Oba 1:17; Ezr 9:9; Za 51:18kwa maana Mungu ataiokoa Sayuni

na kuijenga tena miji ya Yuda.

Kisha watu watafanya makao yao humo na kuimiliki,

3669:36 Za 25:13; 37:29watoto wa watumishi wake watairithi

na wale wote walipendao jina lake

wataishi humo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 69:1-36

Salimo 69

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.”

1Pulumutseni Inu Mulungu,

pakuti madzi afika mʼkhosi

2Ine ndikumira mʼthope lozama

mʼmene mulibe popondapo.

Ndalowa mʼmadzi ozama;

mafunde andimiza.

3Ndafowoka ndikupempha chithandizo;

kummero kwanga kwawuma gwaa,

mʼmaso mwanga mwada

kuyembekezera Mulungu wanga.

4Iwo amene amadana nane popanda chifukwa

ndi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga;

ambiri ndi adani anga popanda chifukwa,

iwo amene akufunafuna kundiwononga.

Ndikukakamizidwa kubwezera

zomwe sindinabe.

5Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu,

kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu.

6Iwo amene amadalira Inu

asanyozedwe chifukwa cha ine,

Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Iwo amene amafunafuna Inu

asachititsidwe manyazi chifukwa cha ine,

Inu Mulungu wa Israeli.

7Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu,

ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.

8Ndine mlendo kwa abale anga,

munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga;

9pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa

ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.

10Pamene ndikulira ndi kusala kudya,

ndiyenera kupirira kunyozedwa;

11pomwe ndavala chiguduli,

anthu amandiseweretsa.

12Iwo amene amakhala pa chipata amandinena,

ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa.

13Koma ndikupempha kwa Inu Ambuye,

pa nthawi yanu yondikomera mtima;

mwa chikondi chanu chachikulu

Inu Mulungu, mundiyankhe pondipulumutsa.

14Mundilanditse kuchoka mʼmatope,

musalole kuti ndimire,

pulumutseni ine kwa iwo

amene amadana nane, kuchoka mʼmadzi ozama.

15Musalole kuti chigumula chindimeze,

kuya kusandimeze

ndipo dzenje lisatseke pakamwa pake kundimiza.

16Ndiyankheni Inu Yehova mwa ubwino wanu wa chikondi chanu;

mwa chifundo chanu chachikulu tembenukirani kwa ine.

17Musabisire nkhope yanu mtumiki wanu,

ndiyankheni msanga, pakuti ndili pa mavuto.

18Bwerani pafupi ndi kundilanditsa;

ndiwomboleni chifukwa cha adani anga.

19Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera,

kunyozedwa ndi kuchititsidwa manyazi; adani anga onse ali pamaso panu.

20Mnyozo waswa mtima wanga

ndipo wandisiya wopanda thandizo lililonse;

ndinafunafuna ena woti andichitire chisoni,

koma panalibe ndi mmodzi yemwe woti anditonthoze, sindinapeze ndi mmodzi yemwe.

21Iwo anayika ndulu mʼchakudya changa

ndi kundipatsa vinyo wosasa chifukwa cha ludzu.

22Chakudya chomwe chayikidwa patsogolo pawo chikhale msampha;

chikhale chobwezera chilango ndiponso khwekhwe.

23Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonenso

ndipo misana yawo ipindike mpaka kalekale.

24Khuthulirani ukali wanu pa iwo;

mkwiyo wanu woyaka moto uwathe mphamvu.

25Malo awo akhale wopanda anthu

pasapezeke ndi mmodzi yemwe wokhala mʼmatenti awo.

26Pakuti iwo amazunza amene inu munamuvulaza

ndi kuyankhula zowawa kwa amene munawapweteka.

27Awonjezereni kulakwa pa kulakwa kwawo,

musalole kuti akhale ndi gawo pa chipulumutso chanu.

28Iwo afufutidwe mʼbuku la amoyo

ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama.

29Ndikumva zowawa ndi kuzunzika;

lolani chipulumutso chanu, Inu Mulungu, chinditeteze.

30Ine ndidzatamanda dzina la Mulungu mʼnyimbo,

ndidzalemekeza Iye ndi chiyamiko.

31Izi zidzakondweretsa Yehova kupambana ngʼombe,

kupambananso ngʼombe yayimuna, pamodzi ndi nyanga ndi ziboda zake.

32Wosauka adzaona ndipo adzasangalala,

Inu amene mumafunafuna Mulungu, mitima yanu ikhale ndi moyo!

33Yehova amamvera anthu osowa

ndipo sanyoza anthu ake omangidwa.

34Kumwamba ndi dziko lapansi zitamanda Iye,

nyanja ndi zonse zomwe zimayenda mʼmenemo,

35pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni

ndi kumanganso mizinda ya Yuda,

anthu adzakhala kumeneko ndipo dzikolo lidzakhala lawo;

36ana atumiki ake adzalitenga kukhala cholowa chawo,

ndipo iwo amene amakonda dzina lake adzakhala kumeneko.