Zaburi 68 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 68:1-35

Zaburi 68

Wimbo Wa Taifa Wa Shangwe Kwa Ushindi

Kwa mwimbishaji. Zaburi ya Daudi. Wimbo.

168:1 Za 89:10; 132:8; 12:5; 18:14; 92:9; 144:6; Hes 10:35; Isa 17:13; 21:15; 33:3Mungu na ainuke, watesi wake watawanyike,

adui zake na wakimbie mbele zake.

268:2 Za 37:20; 80:16; 22:14; 9:3; Hes 10:35Kama vile moshi upeperushwavyo na upepo,

vivyo hivyo uwapeperushe mbali,

kama vile nta iyeyukavyo kwenye moto,

vivyo hivyo waovu na waangamie mbele za Mungu.

368:3 Za 64:10; 97:12Bali wenye haki na wafurahi,

washangilie mbele za Mungu,

wafurahi na kushangilia.

468:4 2Sam 22:50; Za 7:17; 30:4; 66:2; 68:33; 96:2; 100:4; 135:3; 83:18; Kut 6:3; 20:21; Kum 33:26Mwimbieni Mungu, liimbieni sifa jina lake,

mtukuzeni yeye aendeshwaye juu ya mawingu:

jina lake ni Bwana,

furahini mbele zake.

568:5 Za 10:14; Kut 22:22; Kum 10:18; 26:15; Yer 25:30Baba wa yatima, mtetezi wa wajane,

ni Mungu katika makao yake matakatifu.

668:6 Lk 4:18; Za 146:7; 113:9; 102:20; 79:11; 25:16; Isa 58:11; 35:7; 49:10; 61:1Mungu huwaweka wapweke katika jamaa,

huwaongoza wafungwa wakiimba,

bali waasi huishi katika nchi kame.

768:7 Kut 13:21; Za 78:40; 106:14Ee Mungu, ulipowatangulia watu wako,

ulipopita nyikani,

868:8 2Sam 22:8; Amu 5:4, 5; Mhu 11:3; 2Sam 21:10; Kum 33:2dunia ilitikisika,

mbingu zikanyesha mvua,

mbele za Mungu, Yule wa Sinai,

mbele za Mungu, Mungu wa Israeli.

968:9 Kum 32:2; Ay 36:28; Eze 34:26Ee Mungu, ulinyesha mvua nyingi

na kuiburudisha ardhi iliyokuwa imechoka.

1068:10 Kum 28:12; Za 65:9Ee Mungu, watu wako waliishi huko,

nawe kwa wingi wa utajiri wako

uliwapa maskini mahitaji yao.

1168:11 Lk 2:13Bwana alitangaza neno,

waliolitangaza neno hilo walikuwa kundi kubwa:

1268:12 Yos 10:16; Amu 5:30“Wafalme na majeshi walikimbia upesi,

watu waliobaki kambini waligawana nyara.

1368:13 Mwa 49:14Hata ulalapo katikati ya mioto ya kambini,

mabawa ya njiwa wangu yamefunikwa kwa fedha,

manyoya yake kwa dhahabu ingʼaayo.”

1468:14 2Sam 22:15; Amu 9:48Wakati Mwenyezi68:14 Mwenyezi hapa ina maana ya Shaddai kwa Kiebrania. alipowatawanya wafalme katika nchi,

ilikuwa kama theluji iliyoanguka juu ya Salmoni.

15Milima ya Bashani ni milima iliyotukuka,

milima ya Bashani ina vilele vilivyochongoka.

1668:16 Za 132:13, 14; 2:6; Kum 12:5Enyi milima yenye vilele vilivyochongoka,

kwa nini mnakazia macho kwa wivu,

katika mlima Mungu anaochagua kutawala,

ambako Bwana mwenyewe ataishi milele?

1768:17 2Fal 2:11; Isa 66:15; Hab 3:8; Dan 7:10Magari ya Mungu ni makumi ya maelfu,

na maelfu ya maelfu;

Bwana amekuja kutoka Sinai

hadi katika patakatifu pake.

1868:18 Za 47:5; 7:7; Amu 5:12; Efe 4:8; Hes 17:10Ulipopanda juu, uliteka mateka,

ukapokea vipawa kutoka kwa wanadamu,

hata kutoka kwa wale walioasi,

ili wewe, Ee Bwana Mungu, upate kuishi huko.

1968:19 Za 65:5; 81:6Sifa apewe Bwana, Mungu Mwokozi wetu,

ambaye siku kwa siku hutuchukulia mizigo yetu.

2068:20 1Sam 10:19; Za 56:13; Yer 45; 5; Eze 6:8Mungu wetu ni Mungu aokoaye,

Bwana Mwenyezi hutuokoa na kifo.

2168:21 Za 74:14; 110:5; Hab 3:13Hakika Mungu ataponda vichwa vya adui zake,

vichwa vya hao waendao katika njia za dhambi.

2268:22 Ay 36:30; Mt 18:6Bwana alisema, “Nitawarudisha kutoka Bashani;

nitawarudisha kutoka vilindi vya bahari,

2368:23 Za 58:10; 1Fal 21:19; 2Fal 9:36ili uweze kuchovya miguu yako katika damu ya adui zako,

huku ndimi za mbwa wako zikiwa na fungu lake.”

2468:24 Za 63:2Ee Mungu, maandamano yako yameonekana,

maandamano ya Mungu wangu, Mfalme wangu,

yakielekea patakatifu pake.

2568:25 1Nya 15:16; 6:31; 2Nya 5:12; Ufu 18:22; Mwa 31:27; Isa 5:12Mbele wako waimbaji, baada yao wapiga vinanda,

pamoja nao wako wanawali wakipiga matari.

2668:26 Za 22:22; Ebr 2:12; Law 19:2Msifuni Mungu katika kusanyiko kubwa,

msifuni Bwana katika kusanyiko la Israeli.

2768:27 1Sam 9:21; Hes 34:21; Amu 5:18Liko kabila dogo la Benyamini likiwaongoza,

wakifuatwa na kundi kubwa la watawala wa Yuda,

hatimaye watawala wa Zabuloni na Naftali.

2868:28 Kut 9:16; Za 29:11; Isa 26:12; 29:23; 45:11; 60:21; 64:8Ee Mungu, amuru uwezo wako,

Ee Mungu tuonyeshe nguvu zako,

kama ulivyofanya hapo awali.

2968:29 2Nya 9:24; 32:23Kwa sababu ya Hekalu lako Yerusalemu

wafalme watakuletea zawadi.

3068:30 Isa 27:1; 34:7; 51:9; Ay 40:21; Eze 29:3; Za 22:12; 18:14; 120:7; 89:10; 140:2; Yer 50:27Mkemee mnyama aliyeko kwenye manyasi,

kundi la mafahali katikati ya ndama za mataifa.

Na walete minara ya madini ya fedha wakinyenyekea.

Tawanya mataifa yapendayo vita.

3168:31 Isa 19:19; 43:3; 45:14; 11:11; 18:1; Sef 3:10Wajumbe watakuja kutoka Misri,

Kushi68:31 Kushi hapa ina maana maeneo ya Naili ya juu, yaani Ethiopia. atajisalimisha kwa Mungu.

3268:32 Za 46:6; 67:4; 7:17Mwimbieni Mungu, enyi falme za dunia,

mwimbieni Bwana sifa,

3368:33 Kum 33:26; Kut 9:23; Za 29:3, 4; Isa 30:30; 33:3; 66:6; 45:3mwimbieni sifa yeye apandaye mbingu za kale zilizo juu,

yeye angurumaye kwa sauti kuu.

3468:34 Za 68:28; 45:3Tangazeni uwezo wa Mungu,

ambaye fahari yake iko juu ya Israeli,

ambaye uwezo wake uko katika anga.

3568:35 Mwa 28:17; Isa 40:29; 41:10; 50:2; Za 66:20; 18:1; 29:11; 28:6; 2Kor 1:3; Kum 7:21Ee Mungu, wewe unatisha katika mahali patakatifu pako,

Mungu wa Israeli huwapa watu wake uwezo na nguvu.

Mungu Asifiwe!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 68:1-35

Salimo 68

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;

adani ake athawe pamaso pake.

2Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.

Monga phula limasungunukira pa moto,

oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.

3Koma olungama asangalale

ndi kukondwera pamaso pa Mulungu;

iwo akondwere ndi kusangalala.

4Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,

mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo;

dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.

5Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,

ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.

6Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,

amatsogolera amʼndende ndi kuyimba;

koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.

7Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,

pamene munayenda kudutsa chipululu,

8dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,

pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai.

Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.

9Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;

munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.

10Anthu anu anakhala mʼmenemo

ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.

11Ambuye analengeza mawu,

ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;

12“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro;

mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.

13Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto,

mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva,

nthenga zake ndi golide wonyezimira.”

14Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko,

zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.

15Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero;

mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.

16Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri,

pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira,

kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?

17Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka,

ndi miyandamiyanda;

Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.

18Pamene Inu munakwera mmwamba,

munatsogolera a mʼndende ambiri;

munalandira mphatso kuchokera kwa anthu,

ngakhale kuchokera kwa owukira,

kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.

19Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu

amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.

20Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;

Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.

21Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake,

zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.

22Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani;

ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.

23Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu,

pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”

24Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu;

mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.

25Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo;

pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.

26Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu;

tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.

27Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera,

pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda,

ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.

28Kungani mphamvu zanu Mulungu;

tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.

29Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu,

mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.

30Dzudzulani chirombo pakati pa mabango,

gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu.

Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva.

Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.

31Nthumwi zidzachokera ku Igupto;

Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.

32Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi

imbirani Ambuye matamando.

Sela

33Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba

amene amabangula ndi mawu amphamvu.

34Lengezani za mphamvu za Mulungu,

amene ulemerero wake uli pa Israeli

amene mphamvu zake zili mʼmitambo.

35Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika;

Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake.

Matamando akhale kwa Mulungu!