Zaburi 60 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 60:1-12

Zaburi 60

Kuomba Kuokolewa

Kwa mwimbishaji. Mtindo wa “Shushani Eduthi.” Utenzi wa Daudi wa kufundisha. Wakati alipopigana na Waaramu kutoka Aramu-Naharaimu na Aramu-Soba, naye Yoabu akarudi nyuma na kuwaua Waedomu 12,000 katika Bonde la Chumvi.

160:1 2Sam 5:20; Za 18:7; 44:9; 79:5; 80:3; 60:2; 2Nya 7:14Ee Mungu, umetukataa na kutokea ghafula juu yetu,

umekasirika: sasa turejeshe upya!

2Umetetemesha nchi na kuipasua;

uiponye mavunjiko yake, kwa maana inatetemeka.

360:3 Za 71:20; 75:8; Isa 29:9; 51:17; 63:6; Yer 25:16; Zek 12:2; Ufu 14:10Umewaonyesha watu wako nyakati za kukata tamaa;

umetunywesha mvinyo unaotuyumbisha.

460:4 Isa 5:26; 11:10, 12; 18:3Kwa wale wanaokucha wewe,

umewainulia bendera,

ili iweze kutwekwa dhidi ya upinde.

560:5 Ay 40:14; Kum 33:12; Za 108:6Tuokoe na utusaidie kwa mkono wako wa kuume,

ili wale uwapendao wapate kuokolewa.

660:6 Mwa 12:6; 33:17; Za 89:35; Yos 13:27Mungu amenena kutoka patakatifu pake:

“Nitaigawa Shekemu kwa ushindi

na kulipima Bonde la Sukothi.

760:7 Yos 13:31; Hes 34:19; Mwa 41:52; 49:10; Kum 33:17Gileadi ni yangu na Manase ni yangu;

Efraimu ni kofia yangu ya chuma,

nayo Yuda ni fimbo yangu ya utawala.

860:8 2Sam 8:1Moabu ni sinia langu la kunawia,

juu ya Edomu natupa kiatu changu;

nashangilia kwa kushindwa kwa Ufilisti.”

9Ni nani atakayenipeleka hadi mji wenye ngome?

Ni nani atakayeniongoza hadi nifike Edomu?

1060:10 Yos 7:12; Za 44:9Ee Mungu, si ni wewe uliyetukataa sisi,

na hutoki tena na majeshi yetu?

1160:11 Za 146:3; Mit 3:5Tuletee msaada dhidi ya adui,

kwa maana msaada wa mwanadamu haufai kitu.

1260:12 1Nya 19:13; Ay 40:12; Za 44:5Kwa msaada wa Mungu tutapata ushindi,

naye atawaponda adui zetu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.