Zaburi 44 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 44:1-26

Zaburi 44

Kuomba Ulinzi Wa Mungu

Kwa mwimbishaji. Utenzi wa wana wa Kora.

144:1 2Sam 7:22; 1Nya 17:20; Yer 26:11; Amu 6:13; Kum 32:7; Ay 37:23Ee Mungu, tumesikia kwa masikio yetu,

baba zetu wametueleza

yale uliyotenda katika siku zao,

siku za kale.

244:2 Kut 15:17; Kum 7:1; Yos 10:42; 3:10; Mdo 7:45; Isa 60:21; Amu 4:23; 2Nya 14:13; Za 80:9; Yer 32:23Kwa mkono wako uliwafukuza mataifa

na ukawapanda baba zetu,

uliangamiza mataifa

na kuwastawisha baba zetu.

344:3 Yos 24:12; Kut 15:16; Za 78:54; 77:15; 79:11; 89:10, 15; Isa 40:10; 52:10; 63:5; Kum 4:37Sio kwa upanga wao waliipata nchi,

wala si mkono wao uliwapatia ushindi;

ilikuwa ni kitanga cha mkono wako wa kuume,

na nuru ya uso wako,

kwa kuwa uliwapenda.

444:4 Za 24:7; 5:2; 21:5; 74:12Wewe ni mfalme wangu na Mungu wangu,

unayeamuru ushindi kwa Yakobo.

544:5 Yos 23:5; Za 60:12; 108:13; Dan 8:10Kwa uwezo wako tunawasukuma nyuma watesi wetu;

kwa jina lako tunawakanyaga adui zetu.

644:6 Za 33:16; Hos 1:7; Mwa 48:22Siutumaini upinde wangu,

upanga wangu hauniletei ushindi;

744:7 Kum 20:4; Ay 8:2bali wewe unatupa ushindi juu ya adui zetu,

unawaaibisha watesi wetu.

844:8 1Kor 1:3; Rum 2:17; Za 34:2; 52:1; 30:12; 2Kor 10:17Katika Mungu wetu tunajivuna mchana kutwa,

nasi tutalisifu jina lako milele.

944:9 Kum 8:3; 31:17; Za 43:2; 107:39; 108:11; Isa 5:15; Yos 7:12Lakini sasa umetukataa na kutudhili,

wala huendi tena na jeshi letu.

1044:10 Law 26:17; Amu 2:14; Kum 28:25Umetufanya turudi nyuma mbele ya adui,

nao watesi wetu wametuteka nyara.

1144:11 Yer 12:3; 32:37; Law 26:33; Zek 2:6; Kum 4:27; Eze 6:8; Lk 21:24; Za 9:11; 60:1; 2Fal 17:6Umetuacha tutafunwe kama kondoo

na umetutawanya katika mataifa.

1244:12 Kum 32:30; Isa 50:1; 52:3; Yer 15:13Umewauza watu wako kwa fedha kidogo,

wala hukupata faida yoyote kwa mauzo yao.

1344:13 2Nya 29:8; Isa 30:3; Yer 25:9; 42:18; 44:8; Kum 28:37; Mik 2:6; Za 79:4; 80:6; 89:41; Eze 23:32Umetufanya lawama kwa jirani zetu,

dharau na dhihaka kwa wale wanaotuzunguka.

1444:14 1Fal 9:7; 2Fal 19:21Umetufanya kuwa mithali miongoni mwa mataifa,

mataifa hutikisa vichwa vyao.

1544:15 Mwa 30:23; 2Nya 32:21; Za 35:26; 34:5Fedheha yangu iko mbele yangu mchana kutwa,

na uso wangu umejaa aibu tele,

1644:16 Za 42:10; 10:13; 55:3; 74:10; 1Sam 18:25; Yer 11:19; Rum 12:19kwa ajili ya dhihaka ya wale wanaonilaumu na kunitukana,

kwa sababu ya adui, ambaye anatamani kulipiza kisasi.

1744:17 Kum 6:12; 32:18; Mit 3:1; Dan 9:13; Za 119:16, 61, 153, 176Hayo yote yametutokea,

ingawa tulikuwa hatujakusahau

wala hatujaenda kinyume na agano lako.

1844:18 Za 119:51, 157Mioyo yetu ilikuwa haijarudi nyuma;

nyayo zetu zilikuwa hazijaiacha njia yako.

1944:19 2Nya 14:13; Za 51:8; Isa 43:12; Ay 30:29; 3:5Lakini ulituponda na kutufanya makao ya mbweha,

na ukatufunika kwa giza nene.

2044:20 Kum 32:18; Amu 4:7; Isa 43:12; Kut 20:3; Yer 5:12Kama tungalikuwa tumelisahau jina la Mungu wetu

au kunyooshea mikono yetu kwa mungu mgeni,

2144:21 1Sam 16:7; 1Fal 8:39; Yn 2:25; Mit 15:11; Yer 12:3; 17:10; Ay 31:14; Za 139:1; Mhu 12:14; Mdo 1:24; Ufu 2:23; Rum 2:16; Ebr 4:12je, Mungu hangaligundua hili,

kwa kuwa anazijua siri za moyo?

2244:22 Yer 11:19; 12:3; Isa 53:7; Rum 8:36Hata hivyo kwa ajili yako tunauawa mchana kutwa;

tumehesabiwa kama kondoo wa kuchinjwa.

2344:23 Za 7:6; 78:65; 59:5; 74:1; 77:7Amka, Ee Bwana! Kwa nini unalala?

Zinduka! Usitukatae milele.

2444:24 Mao 5:20Kwa nini unauficha uso wako

na kusahau taabu na mateso yetu?

2544:25 Za 119:25Tumeshushwa hadi mavumbini,

miili yetu imegandamana na ardhi.

2644:26 Za 102:13; 26:11; 12:5; 6:4; Hes 10:25Inuka na utusaidie,

utukomboe kwa sababu ya upendo wako usio na mwisho.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 44:1-26

Salimo 44

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora.

1Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu;

makolo athu atiwuza

zimene munachita mʼmasiku awo,

masiku akalekalewo.

2Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena

ndi kudzala makolo athu;

Inu munakantha mitundu ya anthu,

koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.

3Sanalande dziko ndi lupanga lawo,

si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso,

koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu,

pakuti munawakonda.

4Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga

amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.

5Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu;

kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.

6Sindidalira uta wanga,

lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;

7koma Inu mumatigonjetsera adani athu,

mumachititsa manyazi amene amadana nafe.

8Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse,

ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.

9Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa;

Inu simupitanso ndi ankhondo athu.

10Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani

ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.

11Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa

ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.

12Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika,

osapindulapo kanthu pa malondawo.

13Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina,

chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.

14Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina;

anthu amapukusa mitu yawo akationa.

15Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse

ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi

16chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe,

chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.

17Zonsezi zinatichitikira

ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu

kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.

18Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo;

mapazi athu sanatayike pa njira yanu.

19Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe

ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.

20Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu

kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,

21kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi,

pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?

22Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse,

tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.

23Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona!

Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.

24Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu,

ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?

25Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi;

matupi athu amatirira pa dothi.

26Imirirani ndi kutithandiza,

tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.