Zaburi 39 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 39:1-13

Zaburi 39

Maombi Ya Mtu Anayeteseka

Kwa mwimbishaji. Mtindo wa Yeduthuni. Zaburi ya Daudi.

139:1 1Fal 2:4; Kol 4:5; Ebr 2:1; Ay 1:22; 6:24; Yak 1:26; 3:2; Za 34:13; 119:9, 59; Mit 4:26, 27; 20:11Nilisema, “Nitaziangalia njia zangu

na kuuzuia ulimi wangu usije ukatenda dhambi;

nitaweka lijamu kinywani mwangu

wakati wote waovu wanapokuwa karibu nami.”

239:2 Za 6:3; 25:17; 39:9; 77:4; 31:10; Ay 31:34Lakini niliponyamaza kimya na kutulia,

hata pasipo kusema lolote jema,

uchungu wangu uliongezeka.

339:3 Yer 20:9; Lk 24:32; Za 1:2; 119:15; Yer 5:14; 20:9; 23:29Moyo wangu ulipata moto ndani yangu,

nilipotafakari, moto uliwaka,

ndipo nikasema kwa ulimi wangu:

439:4 Ay 14:5; 14:2; 7:7; Mwa 47:9“Ee Bwana, nijulishe mwisho wa maisha yangu

na hesabu ya siku zangu;

nijalie kujua jinsi maisha yangu

yanavyopita upesi.

539:5 Ay 10:20; 7:7; Za 62:9; 90:4; 89:45; 102:23Umefanya maisha yangu mafupi kama pumzi;

muda wangu wa kuishi ni kama

hauna thamani kwako.

Maisha ya kila mwanadamu

ni kama pumzi.

639:6 Ay 8:9; 27:17; Mhu 6:12; Lk 12:20; Yak 4:14; 1:11; Za 102:11; 127:2Hakika kila binadamu ni kama njozi

aendapo huku na huko:

hujishughulisha na mengi lakini ni ubatili;

anakusanya mali nyingi,

wala hajui ni nani atakayeifaidi.

739:7 Za 9:18“Lakini sasa Bwana, nitafute nini?

Tumaini langu ni kwako.

839:8 Isa 53:5, 8, 10; 43:28; Kum 28:37; Za 69:7; 51:1, 14; 32:1; 6:4; 79:4; Dan 9:16Niokoe kutoka kwenye makosa yangu yote,

usinifanye kuwa dhihaka ya wapumbavu.

939:9 Za 38:13; Isa 38:15Nilinyamaza kimya,

sikufumbua kinywa changu,

kwa sababu wewe ndiwe uliyetenda hili.

1039:10 2Nya 21:14; Eze 7:9; 24:16; Kut 9:3Niondolee mjeledi wako,

nimeshindwa kwa mapigo ya mkono wako.

1139:11 Kum 28:20; Isa 26:16; 51:8; 66:15; Eze 5:15; 2Pet 2:16; Za 94:10; 90:7; Ay 7:7; 13:28; Lk 12:33; Yak 5:2Unakemea na kuadhibu wanadamu

kwa ajili ya dhambi zao;

unaharibu utajiri wao kama nondo aharibuvyo:

kila mwanadamu ni kama pumzi tu.

1239:12 Za 17:1; 1Nya 29:15; Ebr 11:13; Law 25:23; Kum 1:45; 2Fal 20:5; Mwa 23:4; 47:9“Ee Bwana, usikie maombi yangu,

usikie kilio changu unisaidie,

usiwe kiziwi kwa kulia kwangu.

Kwani mimi ninaishi na wewe kama mgeni,

kama walivyokuwa baba zangu wote,

1339:13 Ay 10:20, 21Tazama mbali nami, ili niweze kufurahi tena

kabla sijaondoka na nisiwepo tena.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”