Zaburi 33 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 33:1-22

Zaburi 33

Ukuu Na Wema Wa Mungu

133:1 Za 64:10; 101:1; 147:1; 11:7Mwimbieni Bwana kwa furaha, enyi wenye haki;

kusifu kunawapasa wanyofu wa moyo.

233:2 Mwa 4:21; 1Kor 14:7; Ufu 5:8; Za 92:3; 144:9Msifuni Bwana kwa kinubi,

mwimbieni sifa kwa zeze la nyuzi kumi.

333:3 Za 40:3; 35:27; 47:1; Isa 42:10; Ufu 5:9; Ay 3:7Mwimbieni wimbo mpya;

pigeni kwa ustadi, na mpaze sauti za shangwe.

433:4 Ufu 19:9; 22:6; Za 19:8; 18:25; 119:142; 25:10Maana neno la Bwana ni haki na kweli,

ni mwaminifu kwa yote atendayo.

533:5 Za 11:7; 6:4Bwana hupenda uadilifu na haki;

dunia imejaa upendo wake usiokoma.

633:6 Ebr 11:3; Kut 8:19; Mwa 1:3, 16; 2Nya 2:12; Yn 1:1-3; Ay 26:13Kwa neno la Bwana mbingu ziliumbwa,

jeshi lao la angani kwa pumzi ya kinywa chake.

733:7 Mwa 1:10; Yos 3:16Ameyakusanya maji ya bahari

kama kwenye chungu;

vilindi vya bahari

ameviweka katika ghala.

833:8 Kum 6:13; 14:23; Za 2:11; 49:1; Isa 18:3; Mik 1:2Dunia yote na imwogope Bwana,

watu wote wa dunia wamche.

933:9 Za 148:5; Mwa 1:3Kwa maana Mungu alisema, na ikawa,

aliamuru na ikasimama imara.

1033:10 Isa 44:25; Za 2:1; Ay 5:12Bwana huzuia mipango ya mataifa,

hupinga makusudi ya mataifa.

1133:11 Hes 23:19; Yer 51:12, 29; Ay 23:13; Mit 19:21; Eze 38:10; Mdo 4:27, 28Lakini mipango ya Bwana inasimama imara milele,

makusudi ya moyo wake kwa vizazi vyote.

1233:12 Za 144:15; 65:4; 4:3; 84:4; Kum 7:6; Kut 8:22; 34:9Heri taifa ambalo Bwana ni Mungu wao,

watu ambao aliwachagua kuwa urithi wake.

1333:13 Za 53:2; 102:19; 11:4; 14:2; Ebr 4:13; 2Nya 16:9; Ay 28:24Kutoka mbinguni Bwana hutazama chini

na kuwaona wanadamu wote;

1433:14 Law 15:31; 1Fal 8:39kutoka maskani mwake huwaangalia

wote wakaao duniani:

1533:15 Ay 10:8; 11:11; 10:4; Yer 32:19; Isa 64:8; Hes 7:2; Za 44:21; 119:73; Mit 24:12yeye ambaye huumba mioyo yao wote,

ambaye huangalia kila kitu wanachokitenda.

1633:16 1Sam 14:6Hakuna mfalme aokokaye kwa ukubwa wa jeshi lake;

hakuna shujaa aokokaye kwa wingi wa nguvu zake.

1733:17 Za 20:7Farasi ni tumaini la bure kwa wokovu,

licha ya nguvu zake nyingi, hawezi kuokoa.

1833:18 Kut 3:16; Ay 36:7; Za 11:4; 6:4; 34:15; 1Pet 3:12Lakini macho ya Bwana yako kwa wale wamchao,

kwa wale tumaini lao liko katika upendo wake usio na kikomo,

1933:19 Za 56:13; Ay 5:20; Mdo 12:11ili awaokoe na mauti,

na kuwahifadhi wakati wa njaa.

2033:20 Za 27:14Sisi tunamngojea Bwana kwa matumaini,

yeye ni msaada wetu na ngao yetu.

2133:21 1Sam 2:1; Yoe 2:23; Za 30:4; 99:3Mioyo yetu humshangilia,

kwa maana tunalitumainia jina lake takatifu.

2233:22 Za 6:4Upendo wako usio na mwisho ukae juu yetu, Ee Bwana,

tunapoliweka tumaini letu kwako.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 33:1-22

Salimo 33

1Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama,

nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.

2Mutamandeni Yehova ndi pangwe;

muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.

3Muyimbireni nyimbo yatsopano;

imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.

4Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona;

Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.

5Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama;

dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.

6Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa,

zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.

7Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko;

amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.

8Dziko lonse lapansi liope Yehova;

anthu onse amulemekeze Iye.

9Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo;

Iye analamulira ndipo zinakhazikika.

10Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina;

Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.

11Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya,

zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.

12Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova,

anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.

13Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi

ndi kuona anthu onse;

14kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira

onse amene amakhala pa dziko lapansi.

15Iye amene amapanga mitima ya onse,

amaona zonse zimene akuchita.

16Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo;

palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.

17Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso,

ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.

18Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye;

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,

19kuwawombola iwo ku imfa

ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.

20Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo;

Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.

21Mwa Iye mitima yathu imakondwera,

pakuti ife timadalira dzina lake loyera.

22Chikondi chanu chosatha

chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.