Zaburi 31 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 31:1-24

Zaburi 31

Maombi Na Sifa Kwa Kuokolewa Kutoka Kwa Adui

Kwa mwimbishaji. Zaburi ya Daudi.

131:1 Za 7:1; 5:8Ee Bwana, nimekukimbilia wewe,

usiache nikaaibika kamwe,

kwa haki yako uniokoe.

231:2 Za 6:4Nitegee sikio lako,

uje uniokoe haraka;

uwe kwangu mwamba wa kimbilio,

ngome imara ya kuniokoa.

331:3 Za 18:2; 23:3; Yer 14:7Kwa kuwa wewe ni mwamba wangu na ngome yangu,

uniongoze na kunilinda kwa ajili ya jina lako.

431:4 1Sam 28:9; Ay 18:10; Za 9:9Uniepushe na mtego niliotegewa,

maana wewe ndiwe kimbilio langu.

531:5 Lk 23:46; Ebr 6:18; Mdo 7:59; Isa 45:19; 65:16; 2Tim 1:12Ninaikabidhi roho yangu mikononi mwako,

unikomboe Ee Bwana, uliye Mungu wa kweli.

631:6 Kum 32:21; Za 4:5Ninawachukia wale wanaongʼangʼania sanamu batili;

mimi ninamtumaini Bwana.

731:7 Yn 10:27; Lk 22:44; Za 25:17Nitafurahia na kushangilia upendo wako,

kwa kuwa uliona mateso yangu

na ulijua maumivu ya nafsi yangu.

831:8 Za 18:19; Kum 32:30; 2Sam 22:20Hukunikabidhi kwa adui yangu

bali umeiweka miguu yangu mahali penye nafasi.

931:9 Za 4:1; 6:7; 63:1Ee Bwana unihurumie, kwa kuwa niko kwenye shida;

macho yangu yanafifia kwa huzuni,

nafsi yangu na mwili wangu kwa sikitiko.

1031:10 Za 6:6; 22:5; 32:4; 38:10; 73:26; 25:18; 6:2Maisha yangu yamedhoofika kwa majonzi,

naam, miaka yangu kwa kulia kwa maumivu makali;

nguvu zangu zinaisha kwa ajili ya mateso,

na mifupa yangu inachakaa.

1131:11 Kum 30:7; Za 3:7; 25:19; 102; 22:6; 38:11; 88:8Kwa sababu ya adui zangu wote,

nimedharauliwa kabisa na jirani zangu,

hata kwa rafiki zangu nimekuwa tisho,

wale wanionao barabarani hunikimbia.

1231:12 Za 28:1; 88:4Nimesahaulika miongoni mwao kama mtu aliyekufa,

nimekuwa kama chombo cha mfinyanzi kilichovunjika.

1331:13 Law 19:16; Isa 13:8; Za 50:20; 41:7; 56:6; 71:10; 83:3; Ay 18:11; Yer 6:25; 20:3, 10; 46:5; 49:5; Mao 2:22; Mwa 37:18; Mt 12:14; 27:1Kwa maana nimesikia maneno niliyosingiziwa na wengi;

vitisho viko pande zote;

kwa kuwa wamefanya mashauri dhidi yangu,

na kula njama kuniua.

1431:14 Za 4:5Lakini mimi ninakutumaini wewe peke yako, Ee Bwana;

nimesema, “Wewe ndiwe Mungu wangu.”

1531:15 Ay 14:5Siku za maisha yangu ziko mikononi mwako,

uniokoe mikononi mwa adui zangu

na wale wanifuatiao.

1631:16 Hes 6:25; Dan 9:17; Za 4:6; 6:4Mwangazie mtumishi wako uso wako,

uniokoe kwa ajili ya upendo wako usiokoma.

1731:17 Za 22:5; 94:17; 115:17; 25:2; 1Sam 2:9Usiniache niaibike, Ee Bwana,

kwa maana nimekulilia wewe,

bali waovu waaibishwe

na kunyamazishwa Kuzimu.

1831:18 Za 120:2; 12:3; Mit 10:18; 26:24; 1Sam 2:3; Yud 15Midomo yao isemayo uongo na inyamazishwe,

kwa maana kwa kiburi na dharau

wao husema kwa majivuno

dhidi ya wenye haki.

1931:19 Za 27:13; 23:5; Isa 64:4; 1Kor 2:9; Rum 11:22Tazama jinsi ulivyo mkuu wema wako,

uliowawekea akiba wakuchao,

ambao huwapa wale wakukimbiliao

machoni pa watu.

2031:20 Za 55:8; 27:5; 17:8; Mwa 37:18; Ay 5:21Unawahifadhi katika uvuli wa uwepo wako

kutokana na hila za wanadamu;

katika makao yako huwaweka salama

kutokana na ndimi za mashtaka.

2131:21 Za 28:6; 17:7; 1Sam 23:7Atukuzwe Bwana,

kwa kuwa amenionyesha upendo wake wa ajabu

nilipokuwa katika mji uliozingirwa.

2231:22 Za 116:11; 37:9; 88:5; 6:9; 66:19; 116:1; 145:19; Ay 6:9; 17:1; Isa 38:12Katika hofu yangu nilisema,

“Nimekatiliwa mbali na macho yako!”

Hata hivyo ulisikia kilio changu

ukanihurumia nilipokuita unisaidie.

2331:23 Za 4:3; 94:2; 18:25; Ufu 2:10; Kum 32:41; 1Pet 1:5Mpendeni Bwana ninyi watakatifu wake wote!

Bwana huwahifadhi waaminifu,

lakini wenye kiburi huwalipiza kikamilifu.

2431:24 Za 27:14Kuweni hodari na mjipe moyo,

ninyi nyote mnaomtumaini Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.