Zaburi 27 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 27:1-14

Zaburi 27

Sala Ya Kusifu

Zaburi ya Daudi.

127:1 2Sam 22:29; Ay 13:5; Za 3:8; 9:9; 56:4, 11; 118:6; Kut 15:2Bwana ni nuru yangu na wokovu wangu,

nimwogope nani?

Bwana ni ngome ya uzima wangu,

nimhofu nani?

227:2 Za 9:3; 20:8; 37:24; Dan 11:19; Rum 11:11Waovu watakaposogea dhidi yangu

ili wanile nyama yangu,

adui zangu na watesi wangu watakaponishambulia,

watajikwaa na kuanguka.

327:3 Mwa 4:7; Za 3:6; Ay 4:6Hata jeshi linizunguke pande zote,

moyo wangu hautaogopa;

hata vita vitokee dhidi yangu,

hata hapo nitakuwa na ujasiri.

427:4 Lk 10:42; Za 23:6; 61:4Jambo moja ninamwomba Bwana,

hili ndilo ninalolitafuta:

niweze kukaa nyumbani mwa Bwana

siku zote za maisha yangu,

niutazame uzuri wa Bwana

na kumtafuta hekaluni mwake.

527:5 Ay 38:23; Za 12:7, 8; 40:2Kwa kuwa siku ya shida,

atanihifadhi salama katika maskani yake,

atanificha uvulini mwa hema yake

na kuniweka juu kwenye mwamba.

627:6 2Sam 22:49; Za 3:3; 33:2; 54:6; 18:48; 22:12; 92:1; 50:14; 107:22; 116:17; 147:7; Ezr 3:13; Ay 22:26; Kut 15:1; Efe 5:19Kisha kichwa changu kitainuliwa

juu ya adui zangu wanaonizunguka.

Katika maskani yake nitatoa dhabihu kwa kelele za shangwe;

nitamwimbia Bwana na kumsifu.

727:7 Za 4:1; 5:3; 18:6; 55:17; 119:149; 130:2; Isa 28:23Isikie sauti yangu nikuitapo, Ee Bwana,

unihurumie na unijibu.

827:8 1Nya 16:11Moyo wangu unasema kuhusu wewe,

“Utafute uso wake!”

Uso wako, Bwana “Nitautafuta.”

927:9 Za 2:5; 119:8; 18:46; 22:24; 37:28; Mwa 49:25; Kum 31:17; 33:29; 4:31; Isa 41:17; 62:12; Yer 14:9Usinifiche uso wako,

usimkatae mtumishi wako kwa hasira;

wewe umekuwa msaada wangu.

Usinikatae wala usiniache,

Ee Mungu Mwokozi wangu.

10Hata kama baba yangu na mama wakiniacha,

Bwana atanipokea.

1127:11 Ezr 8:21; Za 5:8; 72:4; 78:42; 106:10; Yer 21:12; Kut 33:13Nifundishe njia yako, Ee Bwana,

niongoze katika njia iliyonyooka

kwa sababu ya watesi wangu.

1227:12 Kum 19:16; Mt 26:60; Mdo 6:13; 1Kor 15:15Usiniachilie kwa nia za adui zangu,

kwa maana mashahidi wa uongo

wameinuka dhidi yangu,

wakipumua ujeuri.

1327:13 Kut 33:19; 2Nya 6:41; Za 33:6; 31:19; 145:7; Ay 18:13Nami bado nina tumaini hili:

nitauona wema wa Bwana

katika nchi ya walio hai.

1427:14 Efe 6:10; Amu 5:21; Kum 1:21; Sef 3:8; Hab 2:3; Za 33:20; 130:5, 6; Mdo 1:4; Isa 8:17; 30:18Mngojee Bwana,

uwe hodari na mwenye moyo mkuu,

nawe, umngojee Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 27:1-14

Salimo 27

Salimo la Davide.

1Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa;

ndidzaopa yani?

Yehova ndi linga la moyo wanga;

ndidzachita mantha ndi yani?

2Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane

kudzadya mnofu wanga,

pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo,

iwo adzapunthwa ndi kugwa.

3Ngakhale gulu lankhondo lindizinge,

mtima wanga sudzaopa.

Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane,

ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.

4Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova,

ichi ndi chimene ndidzachifunafuna:

kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova

masiku onse a moyo wanga,

ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova,

ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.

5Pakuti pa tsiku la msautso

Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo;

adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake

ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.

6Kotero mutu wanga udzakwezedwa

kuposa adani anga amene andizungulira;

pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe;

ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.

7Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova

mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.

8Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!”

Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.

9Musandibisire nkhope yanu,

musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo;

mwakhala muli thandizo langa.

Musandikane kapena kunditaya,

Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.

10Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya

Yehova adzandisamala.

11Phunzitseni njira yanu Inu Yehova,

munditsogolere mʼnjira yowongoka

chifukwa cha ondizunza.

12Musandipereke ku zokhumba za adani anga,

pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane

ndipo zikundiopseza.

13Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi;

ndidzaona ubwino wa Yehova

mʼdziko la anthu amoyo.

14Dikirani pa Yehova;

khalani anyonga ndipo limbani mtima

nimudikire Yehova.