Zaburi 132 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Zaburi 132:1-18

Zaburi 132

Maskani Ya Mungu Ya Milele Katika Sayuni

Wimbo wa kwenda juu.

1Ee Bwana, mkumbuke Daudi

na taabu zote alizozistahimili.

2132:2 Mwa 49:24; Isa 49:26; 60:16Aliapa kiapo kwa Bwana

na akaweka nadhiri kwa Yule Mwenye Nguvu wa Yakobo:

3132:3 2Sam 7:2, 27“Sitaingia nyumbani mwangu

au kwenda kitandani mwangu:

4132:4 Rut 3:18sitaruhusu usingizi katika macho yangu,

wala kope zangu kusinzia,

5132:5 1Fal 8:17; Mdo 7:46mpaka nitakapompatia Bwana mahali,

makao kwa ajili ya Yule Mwenye Nguvu wa Yakobo.”

6132:6 1Sam 7:2; 17:12; Yos 9:17; 18:1; 1Nya 13:5Tulisikia habari hii huko Efrathi,

tulikutana nayo katika mashamba ya Yaara:132:6 Yaani Kiriath-Yearimu.

7132:7 2Sam 15:25; Za 5:7; 122:1; 1Nya 28:2“Twendeni kwenye makao yake,

na tuabudu kwenye kiti cha kuwekea miguu yake;

8132:8 Hes 10:35inuka, Ee Bwana, uje mahali pako pa kupumzikia,

wewe na Sanduku la nguvu zako.

9132:9 Ay 27:6; Zek 3:4; Isa 61:3, 10; Mal 3:3; Ay 29:14Makuhani wako na wavikwe haki,

watakatifu wako na waimbe kwa furaha.”

10Kwa ajili ya Daudi mtumishi wako,

usimkatae mpakwa mafuta wako.

11132:11 Za 89:3-4, 35; 1Nya 17:11-14; Mt 1:1; Lk 3:31Bwana alimwapia Daudi kiapo,

kiapo cha uhakika ambacho hatakitangua:

“Nitamweka mmoja wa wazao wako mwenyewe

katika kiti chako cha enzi,

12132:12 2Nya 6:16; Za 25:10; Lk 1:32; Mdo 2:30kama wanao watashika Agano langu

na sheria ninazowafundisha,

ndipo wana wao watarithi

kiti chako cha enzi milele na milele.”

13132:13 Kut 15:17; Za 48:1, 2; 68:16; 1Fal 18:13Kwa maana Bwana ameichagua Sayuni,

amepaonea shauku pawe maskani yake:

14132:14 Za 80:1; 68:16; 2Sam 6:2“Hapa ni mahali pangu pa kupumzika milele na milele;

hapa ndipo nitakapoketi nikitawala, kwa sababu nimepaonea shauku:

15132:15 Za 107:9; 147:14Nitambariki kwa kumpa mahitaji tele:

nitashibisha maskini wake kwa chakula.

16132:16 2Nya 6:41; Ay 8:21; Za 149:5Nitawavika makuhani wake wokovu,

nao watakatifu wake watadumu wakiimba kwa furaha.

17132:17 1Sam 2:10; Za 18:28; 84:9; 92:10; Eze 29:21; Lk 1:69; 1Fal 11:36; 2Fal 8:19; 2Nya 21:7“Hapa nitamchipushia Daudi pembe,132:17 Pembe inawakilisha nguvu.

na kuweka taa kwa ajili ya masiya132:17 Masiya yaani mpakwa mafuta. wangu.

18132:18 Ay 8:22; 2Sam 12:30Adui zake nitawavika aibu,

bali taji kichwani pake itangʼaa sana.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

2Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

3“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

4sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

5mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

6Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

7“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

8‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

9Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

11Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

12ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

14“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

15Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

16Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

18Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”