Yohana 12 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Yohana 12:1-50

Maria Ampaka Yesu Mafuta Huko Bethania

(Mathayo 26:6-13; Marko 14:3-9)

112:1 Yn 11:55; Mt 21:17Siku sita kabla ya Pasaka, Yesu alikwenda Bethania mahali ambako Lazaro aliyekuwa amefufuliwa na Yesu alikuwa anaishi. 212:2 Lk 10:38-42Wakaandaa karamu kwa heshima ya Yesu. Martha akawahudumia wakati Lazaro alikuwa miongoni mwa waliokaa mezani pamoja na Yesu. 312:3 Yn 11:12Kisha Maria akachukua chupa ya painti moja12:3 Painti moja ni kama nusu lita. yenye manukato ya nardo12:3 Nardo ni aina ya mafuta yaliyokuwa yanatengenezwa kutokana na mimea yenye mizizi inayotoa harufu nzuri. safi ya thamani kubwa, akayamimina miguuni mwa Yesu na kuifuta kwa nywele zake. Nyumba nzima ikajaa harufu nzuri ya manukato.

412:4 Mt 10:4Ndipo Yuda Iskariote mwana wa Simoni, mmoja wa wale wanafunzi ambaye ndiye angemsaliti Yesu, akasema, 5“Kwa nini manukato haya hayakuuzwa kwa dinari 30012:5 Dinari 300 ni sawa na mshahara wa kibarua wa siku 300. na fedha hizo wakapewa maskini?” 612:6 Yn 13:29Yuda alisema hivi si kwa kuwa aliwajali maskini, bali kwa kuwa alikuwa mwizi, kwani ndiye alikuwa akitunza mfuko wa fedha akawa anaiba kile kilichowekwa humo.

712:7 Yn 19:40Yesu akasema, “Mwacheni. Aliyanunua manukato hayo ili ayaweke kwa ajili ya siku ya maziko yangu. 812:8 Kum 15:11Maskini mtakuwa nao siku zote, lakini mimi hamtakuwa nami siku zote.”

Shauri La Kumuua Lazaro

912:9 Yn 11:43, 44Umati mkubwa wa Wayahudi walipojua kwamba Yesu alikuwa huko Bethania, walikuja si tu kwa ajili ya Yesu, lakini pia kumwona Lazaro ambaye Yesu alikuwa amemfufua. 1012:10 Lk 16:31Kwa hiyo viongozi wa makuhani wakafanya mpango wa kumuua Lazaro pia, 1112:11 Yn 11:45; 12:18kwa kuwa kutokana na habari za kufufuliwa kwake Wayahudi wengi walikuwa wanamwendea Yesu na kumwamini.

Kuingia Kwa Yesu Yerusalemu Kwa Ushindi

(Mathayo 21:1-11; Marko 1:1-11; Luka 19:28-40)

1212:12 Mt 21:8; Mk 11:8; Lk 19:35, 36Siku iliyofuata umati mkubwa uliokuwa umekuja kwenye Sikukuu walisikia kwamba Yesu angekuja Yerusalemu. 1312:13 Za 118:25-26; Yn 1:49Basi wakachukua matawi ya mitende, wakatoka kwenda kumlaki, huku wakipaza sauti wakisema,

“Hosana!”12:13 Kiebrania kusema Okoa, basi likawa neno la shangwe.

“Amebarikiwa yeye ajaye kwa Jina la Bwana!”

“Amebarikiwa Mfalme wa Israeli!”

1412:14 Mt 21:7Yesu akamkuta mwana-punda akampanda, kama ilivyoandikwa,

1512:15 Zek 9:9“Usiogope, Ewe binti Sayuni;

tazama, Mfalme wako anakuja,

amepanda mwana-punda!”

1612:16 Lk 18:34; Yn 7:39Wanafunzi wake Yesu mwanzoni hawakuelewa mambo haya, lakini Yesu alipotukuzwa, ndipo walipokumbuka kuwa mambo haya yalikuwa yameandikwa kwa ajili yake na alitendewa yeye.

1712:17 Yn 11:42Wale waliokuwepo wakati Yesu alipomwita Lazaro kutoka kaburini na kumfufua kutoka kwa wafu, waliendelea kushuhudia. 1812:18 Yn 12:11; 19:37Ni kwa sababu pia walikuwa wamesikia kwamba alikuwa ametenda muujiza huu ndiyo maana umati wa watu ukaenda kumlaki. 1912:19 Yn 11:47, 48Hivyo Mafarisayo walipoona hayo wakaambiana, “Mnaona, hamwezi kufanya lolote. Angalieni, ulimwengu wote unamfuata yeye!”

Yesu Anatabiri Kifo Chake

2012:20 Yn 7:35; Mdo 11:20Basi palikuwa Wayunani fulani miongoni mwa wale waliokuwa wamekwenda kuabudu wakati wa Sikukuu. 2112:21 Mt 11:21; Yn 1:44Hawa wakamjia Filipo, ambaye alikuwa mwenyeji wa Bethsaida huko Galilaya, wakiwa na ombi. Wakamwambia, “Tungependa kumwona Yesu.” 22Filipo akaenda akamweleza Andrea, nao wote wawili wakamwambia Yesu.

2312:23 Yn 13:32; 17:1Yesu akawajibu, “Saa imewadia ya Mwana wa Adamu kutukuzwa. 2412:24 1Kor 15:36Amin, amin nawaambia, mbegu ya ngano isipoanguka ardhini na kufa, hubakia kama mbegu peke yake. Lakini ikifa huzaa mbegu nyingi. 2512:25 Mk 8:35; Lk 14:26Mtu yeyote anayependa maisha yake atayapoteza, naye ayachukiaye maisha yake katika ulimwengu huu atayaokoa hata kwa uzima wa milele. 2612:26 Flp 1:23Mtu yeyote akinitumikia lazima anifuate, nami mahali nilipo ndipo mtumishi wangu atakapokuwa. Mtu akinitumikia, Baba yangu atamheshimu.

2712:27 Mt 26:38, 39; Lk 12:50; Yn 13:21; Lk 22:53; Yn 18:37“Sasa roho yangu imefadhaika sana. Niseme nini? ‘Baba, niokoe katika saa hii.’ Lakini ni kwa kusudi hili nimeufikia wakati huu. 2812:28 Mt 3:17Baba, litukuze jina lako.”

Ndipo ikaja sauti kutoka mbinguni, “Nimelitukuza, nami nitalitukuza tena.” 2912:29 Lk 22:43Ule umati wa watu uliokuwa mahali pale uliisikia nao ukasema, “Hiyo ni sauti ya radi,” wengine wakasema, “Malaika ameongea naye.”

3012:30 Kut 19:9Yesu akawaambia, “Sauti hii imesikika kwa faida yenu, wala si kwa faida yangu. 3112:31 Yn 16; 11; Efe 2:2; 1Yn 5:19Sasa ni saa ya hukumu kwa ajili ya ulimwengu huu, sasa mkuu wa ulimwengu huu atatupwa nje. 3212:32 Isa 11:10; Yn 3:14; 6:44Lakini mimi, nikiinuliwa kutoka nchi, nitawavuta watu wote waje kwangu.” 3312:33 Yn 18:32; 21:19Yesu aliyasema haya akionyesha ni kifo gani atakachokufa.

3412:34 Za 110:4; Isa 9:7; Mt 8:20; Yn 3:14Ule umati wa watu ukapiga kelele ukasema, “Tumesikia kutoka Sheria kwamba ‘Kristo12:34 Kristo maana yake ni Masiya, yaani Aliyetiwa mafuta. adumu milele,’ wewe wawezaje kusema, ‘Mwana wa Adamu hana budi kuinuliwa juu’? Huyu ‘Mwana wa Adamu’ ni nani?”

3512:35 Yn 1:9; 8:12; 9:5; Yer 13:16; Efe 5:8; 1Yn 2:11Ndipo Yesu akawaambia, “Bado kitambo kidogo nuru ingalipo pamoja nanyi. Enendeni maadamu mna nuru, msije mkakumbwa na giza. Mtu anayetembea gizani hajui anakokwenda. 3612:36 Lk 16:8; Efe 5:8; 1The 5:5; 1Yn 2:9, 10, 11; Yn 8:59; 11:54Wekeni tumaini lenu katika nuru hiyo ili mpate kuwa wana wa nuru.” Baada ya kusema haya, Yesu aliondoka, akajificha wasimwone.

Wayahudi Waendelea Kutokuamini

3712:37 Yn 2:11Hata baada ya Yesu kufanya miujiza hii yote mbele yao, bado hawakumwamini. 3812:38 Isa 53:1; Rum 10:16Hili lilikuwa ili kutimiza lile neno la nabii Isaya lililosema:

“Bwana, ni nani aliyeamini ujumbe wetu,

na mkono wa Bwana umefunuliwa kwa nani?”

3912:39 Isa 6:9, 10; Mt 13:14, 15Kwa hivyo hawakuamini, kwa sababu Isaya anasema mahali pengine:

4012:40 Isa 6:10; Mt 13:13, 15“Amewafanya vipofu,

na kuifanya mioyo yao kuwa migumu,

ili wasiweze kuona kwa macho yao,

wala kuelewa kwa mioyo yao,

wasije wakageuka nami nikawaponya.”

4112:41 Isa 6:1-4; Lk 24:27Isaya alisema haya alipoona utukufu wa Yesu na kunena habari zake.

4212:42 Yn 7:48; 9:22Lakini wengi miongoni mwa viongozi wa Wayahudi walimwamini, lakini kwa sababu ya Mafarisayo hawakukiri waziwazi kwa maana waliogopa kufukuzwa katika masinagogi. 4312:43 Yn 5:44; Rum 2:29Wao walipenda sifa za wanadamu kuliko sifa zitokazo kwa Mungu.

Amwaminiye Yesu Hatabaki Gizani

4412:44 Mt 10:40; Yn 5:24Yesu akapaza sauti akasema, “Yeyote aniaminiye, haniamini mimi peke yangu, bali yeye aliyenituma. 4512:45 Yn 14:9Yeyote anionaye mimi, amemwona yeye aliyenituma. 4612:46 Yn 3:19; 8:12Mimi nimekuja kama nuru ulimwenguni, ili kwamba kila mtu aniaminiye asibaki gizani.

4712:47 Yn 3:17“Mimi simhukumu mtu yeyote anayesikia maneno yangu na asiyatii, kwa maana sikuja kuuhukumu ulimwengu, bali kuuokoa. 4812:48 Yn 5:45Yuko amhukumuye yeye anikataaye mimi na kutokuyapokea maneno yangu, yaani, yale maneno niliyosema yenyewe yatamhukumu siku ya mwisho. 4912:49 Yn 14:31Kwa maana sisemi kwa ajili yangu mwenyewe, bali Baba aliyenituma aliniamuru ni nini cha kusema na jinsi ya kukisema. 5012:50 Yn 8:26, 28Nami ninajua amri zake huongoza hadi kwenye uzima wa milele. Hivyo lolote nisemalo, ndilo lile Baba aliloniambia niseme.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 12:1-50

Mariya Adzoza Mapazi a Yesu

1Masiku asanu ndi limodzi Paska asanafike, Yesu anafika ku Betaniya, kumene kumakhala Lazaro, amene Yesu anamuukitsa kwa akufa. 2Kumeneko anamukonzera Yesu chakudya cha madzulo. Marita anatumikira pamene Lazaro anali mmodzi wa iwo amene anakhala nawo pa chakudyacho. 3Kenaka Mariya anatenga botolo la mafuta a nadi, onunkhira bwino kwambiri, amtengowapatali; Iye anadzoza mapazi a Yesu napukuta ndi tsitsi lake. Ndipo nyumba yonse inadzaza ndi fungo lonunkhira bwino la mafutawo.

4Koma mmodzi wa ophunzira ake, Yudasi Isikarioti, amene pambuyo pake adzamupereka anati, 5“Nʼchifukwa chiyani mafuta awa sanagulitsidwe ndipo ndalama zake nʼkuzipereka kwa osauka?” Mafutawo anali a mtengo wa malipiro a chaka chimodzi. 6Iye sananene izi chifukwa cha kuganizira osauka koma chifukwa anali mbava; ngati wosunga thumba la ndalama, amabamo zomwe ankayikamo.

7Yesu anayankha kuti, “Mulekeni. Mafutawa anayenera kusungidwa mpaka tsiku loyika maliro anga. 8Inu mudzakhala ndi osauka nthawi zonse, koma simudzakhala nane nthawi zonse.”

9Pa nthawi imeneyi gulu lalikulu la Ayuda linadziwa kuti Yesu anali kumeneko, ndipo linabwera, sichifukwa cha Iye yekha koma kudzaonanso Lazaro, amene anamuukitsa kwa akufa. 10Choncho akulu a ansembe anakonza njira yoti aphenso Lazaro, 11pakuti chifukwa cha iye Ayuda ambiri amapita kwa Yesu ndi kumukhulupirira.

Yesu Alowa mu Yerusalemu

12Tsiku lotsatira, gulu lalikulu la anthu lomwe linabwera kuphwando linamva kuti Yesu anali mʼnjira kupita ku Yerusalemu. 13Iwo anatenga nthambi za kanjedza ndi kupita kukakumana naye, akufuwula kuti,

“Hosana!

“Wodala Iye amene akubwera mʼdzina la Ambuye!

“Yodala Mfumu ya Israeli!”

14Yesu anapeza bulu wamngʼono ndi kukwerapo, monga kunalembedwa kuti:

15“Usachite mantha mwana wamkazi wa Ziyoni;

taona mfumu yako ikubwera,

itakhala pa mwana wabulu.”

16Poyamba ophunzira ake sanamvetsetse zonsezi. Koma pomwe Yesu analemekezedwa ndi pamene anazindikira kuti zinthu izi zinalembedwa ndipo kuti anamuchitira Iye.

17Tsopano gulu la anthu lomwe linali naye pa nthawi imene amaukitsidwa Lazaro ku manda linapitiriza kuchitira umboni. 18Anthu ambiri, anapita kukakumana naye, chifukwa iwo anamva kuti Iye anachita chizindikiro chodabwitsachi. 19Choncho Afarisi anati kwa wina ndi mnzake, “Taonani, palibe chimene mwachitapo. Anthu onse akumutsatira Iye!”

Agriki Afuna Kuona Yesu

20Tsopano panali Agriki ena pakati pa amene anapita kukapembedza ku phwando. 21Iwo anabwera kwa Filipo, wochokera ku Betisaida wa ku Galileya, ndi pempho, nati, “Akulu, ife tikufuna kuona Yesu.” 22Filipo anapita kukawuza Andreya; Andreya ndi Filipo pamodzi anakawuza Yesu.

23Yesu anayankha kuti, “Nthawi yafika yakuti Mwana wa Munthu alemekezedwe. 24Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti, ‘Mbewu ya tirigu imakhala imodzi yokha ngati sikugwa mʼnthaka ndi kufa. Koma ngati imfa, imabereka mbewu zambiri.’ 25Munthu amene amakonda moyo wake adzawutaya, pamene munthu amene amadana ndi moyo wake mʼdziko lino lapansi adzawusungira ku moyo wosatha. 26Aliyense amene atumikira Ine ayenera kunditsata; ndipo kumene Ine ndili, wotumikira wanga adzakhalanso komweko. Atate anga adzalemekeza amene atumikira Ine.

27“Moyo wanga ukuvutika tsopano, kodi ndidzanena chiyani? Ndinene kuti Atate pulumutseni ku nthawi ino? Ayi. Chifukwa chimene Ine ndinabwera pa nthawi iyi ndi chimenechi. 28Atate, lemekezani dzina lanu!”

Kenaka mawu anabwera kuchokera kumwamba, “Ine ndalilemekeza, ndipo ndidzalilemekezanso.” 29Gulu la anthu lomwe linali pamenepo litamva linati, “Kwagunda bingu,” ena anati, “Mngelo wayankhula kwa Iye.”

30Yesu anati, “Mawu awa abwera chifukwa cha inu osati chifukwa cha Ine. 31Ino tsopano ndi nthawi yachiweruzo pa dziko lapansi; tsopano olamulira wa dziko lapansi adzathamangitsidwa. 32Koma Ine, akadzandipachika pa dziko lapansi, ndidzakokera anthu onse kwa Ine.” 33Iye ananena izi kuti aonetse mmene adzafere.

34Gulu la anthu linayankha kuti, “Ife tinamva kuchokera mʼmalamulo kuti Khristu adzakhala kwamuyaya, nanga bwanji Inu mukunena kuti, ‘Mwana wa Munthu ayenera kukwezedwa?’ Kodi Mwana wa Munthuyu ndani?”

35Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Inu mukhala ndi kuwunika kwa nthawi pangʼono. Yendani pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mdima usakupitirireni. Munthu amene amayenda mu mdima sadziwa kumene akupita. 36Khulupirirani kuwunika, pamene mukanali ndi kuwunika, kuti mukhale ana a kuwunika.” Yesu atamaliza kuyankhula izi, Iye anachoka nabisala kuti asamuone.

Ayuda Apitirira Kusakhulupirira

37Ngakhale Yesu anachita zizindikiro zodabwitsa zonsezi pamaso pawo, sanamukhulupirirebe. 38Izi zinakwaniritsa mawu a mneneri Yesaya kuti:

“Ambuye, wakhulupirira uthenga wathu ndani,

ndipo ndi kwa yani komwe mkono wa Ambuye wavumbulutsidwa?”

39Pa chifukwa cha ichi iwo sanakhulupirire, chifukwa Yesaya ananenanso kuti:

40“Iye wachititsa khungu maso awo

ndi kuwumitsa mitima yawo,

kotero kuti iwo sangathe kuona ndi maso awo,

kapena kuzindikira ndi mitima yawo,

kapena kutembenuka kuti Ine ndikanawachiza.”

41Yesaya ananena izi chifukwa anaona ulemerero wa Yesu ndi kuyankhula za Iye.

42Komabe pa nthawi yomweyi ambiri ngakhale atsogoleri anakhulupirira Iye. Koma chifukwa cha Afarisi iwo sanavomereze chikhulupiriro chawo chifukwa amaopa kuti angawatulutse mʼsunagoge; 43pakuti iwo amakonda kuyamikiridwa ndi anthu kuposa kuyamikiridwa ndi Mulungu.

44Kenaka Yesu anafuwula nati, “Munthu aliyense amene akhulupirira Ine, sakhulupirira Ine ndekha, komanso Iye amene anandituma Ine. 45Iye amene waona Ine, waonanso Iye amene anandituma Ine. 46Ine ndabwera mʼdziko lapansi monga kuwunika, kotero palibe amene amakhulupirira Ine nʼkumakhalabe mu mdima.

47“Ndipo munthu amene amva mawu anga koma osawasunga, Ine sindimuweruza. Pakuti Ine sindinabwere kudzaweruza dziko lapansi, koma kudzapulumutsa. 48Iye amene akana Ine ndipo salandira mawu anga ali ndi womuweruza. Tsiku lomaliza mawu amene ndiyankhulawa adzamutsutsa. 49Pakuti Ine sindiyankhula mwa Ine ndekha, koma Atate amene anandituma amandilamulira choti ndinene ndi momwe ndinenere. 50Ine ndikudziwa kuti lamulo lake ndi moyo wosatha. Choncho chilichonse chimene Ine ndinena ndi chimene Atate andiwuza.”