Yeremia 49 – NEN & CCL

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Yeremia 49:1-39

Ujumbe Kuhusu Amoni

149:1 Amo 1:13; Mwa 19:38; 1Sam 11:1-11; 2Sam 10:1-9; Law 18:21; Mwa 30:11Kuhusu Waamoni:

Hili ndilo asemalo Bwana:

“Je, Israeli hana wana?

Je, hana warithi?

Kwa nini basi Moleki amechukua milki ya Gadi?

Kwa nini watu wake wanaishi katika miji yake?

249:2 Yer 4:19; Kum 3:11; Isa 1:2; Eze 25:2-11; Kum 13:16; Yer 30:16; Eze 21:28-32Lakini siku zinakuja,”

asema Bwana,

“nitakapopiga kelele ya vita

dhidi ya Raba mji wa Waamoni;

utakuwa kilima cha magofu,

navyo vijiji vinavyouzunguka

vitateketezwa kwa moto.

Kisha Israeli atawafukuza

wale waliomfukuza,”

asema Bwana.

349:3 Mwa 12:8; Yos 8:28; 13:26; Mwa 37:34“Lia kwa huzuni, ee Heshboni, kwa kuwa Ai umeangamizwa!

Pigeni kelele, enyi wakazi wa Raba!

Vaeni nguo za gunia na kuomboleza,

kimbieni hapa na pale ndani ya kuta,

kwa kuwa Moleki atakwenda uhamishoni,

yeye pamoja na makuhani na maafisa wake.

449:4 Yer 21:13; 9:23; 1Tim 6:17; Yer 3:6Kwa nini unajivunia mabonde yako,

kujivunia mabonde yako yaliyozaa sana?

Ee binti usiye mwaminifu, unayeutumainia utajiri wako na kusema,

‘Ni nani atakayenishambulia?’

549:5 Yer 44:14Nitaleta hofu kuu juu yako

kutoka kwa wale wote wanaokuzunguka,”

asema Bwana, Bwana Mwenye Nguvu Zote.

“Kila mmoja wenu ataondolewa,

wala hakuna hata mmoja atakayekusanya wakimbizi.

649:6 Yer 12:14-17; 48:47“Lakini hatimaye,

nitarudisha mateka wa Waamoni,”

asema Bwana.

Ujumbe Kuhusu Edomu

749:7 Ay 5:12-14; Za 83:6; Eze 25:12; Mwa 36:11-15, 34; 25:30Kuhusu Edomu:

Hili ndilo asemalo Bwana Mwenye Nguvu Zote:

“Je, hakuna tena hekima katika Temani?

Je, shauri limewapotea wenye busara?

Je, hekima yao imechakaa?

849:8 Mwa 10:7; Yer 25:23; Isa 2:19; Amu 6:2; Mwa 25:3Geuka na ukimbie, jifiche katika mapango marefu kabisa,

wewe uishiye Dedani,

kwa kuwa nitaleta maafa juu ya Esau

wakati nitakapomwadhibu.

9Je, kama wachuma zabibu wangekuja kwako,

wasingebakiza zabibu chache?

Kama wezi wangekujia usiku,

je, si wangeiba tu kiasi ambacho wangehitaji?

1049:10 Eze 35:4; Isa 17:14; Mao 1:18; Mwa 3:8; Isa 34:10-12; Yer 11:23Lakini nitamvua Esau nguo abaki uchi,

nitayafunua maficho yake,

ili asiweze kujificha.

Watoto wake, jamaa na majirani wataangamia,

naye hatakuwepo tena.

1149:11 Hos 14:3; Mit 23:10-11; Kum 10:18; Yak 1:27Waache yatima wako; nitayalinda maisha yao.

Wajane wako pia

wanaweza kunitumaini mimi.”

1249:12 Isa 51:23; Mt 20:22; Mit 11:31; Yer 25:28-29; 25:15Hili ndilo asemalo Bwana: “Kama wale wasiostahili kukinywea kikombe ni lazima wakinywe, kwa nini wewe usiadhibiwe? Hutakwepa kuadhibiwa, ni lazima ukinywe. 1349:13 Mwa 22:16; 36:33; Isa 34:6; Yer 42:18; Eze 35:9; Yer 42:18Ninaapa kwa nafsi yangu,” asema Bwana, “kwamba Bosra utakuwa magofu na kitu cha kutisha, cha aibu na cha kulaania; miji yake yote itakuwa magofu milele.”

14Nimesikia ujumbe kutoka kwa Bwana:

Mjumbe alitumwa kwa mataifa kusema,

“Jikusanyeni ili kuushambulia!

Inukeni kwa ajili ya vita!”

15“Sasa nitakufanya uwe mdogo miongoni mwa mataifa,

aliyedharauliwa miongoni mwa watu.

1649:16 Ay 39:27-28; Amo 9:2; Eze 35:13; Oba 1:12Vitisho vyako na kiburi cha moyo wako

vimekudanganya,

wewe unayeishi katika majabali ya miamba,

wewe unayedumu katika miinuko ya kilima.

Ujapojenga kiota chako juu sana kama cha tai,

nitakushusha chini kutoka huko,”

asema Bwana.

1749:17 Kum 29:22; Yer 50:13; Eze 35:7“Edomu atakuwa kitu cha kuogofya;

wote wapitao karibu

watashangaa na kuzomea

kwa sababu ya majeraha yake yote.

1849:18 Mwa 19:24; Kum 29:23; Amo 4:11; Isa 34:10; Yer 23:14Kama vile Sodoma na Gomora zilivyoangamizwa,

pamoja na miji iliyokuwa jirani nayo,”

asema Bwana,

“vivyo hivyo hakuna mtu yeyote atakayeishi humo.

Naam, hakuna mtu yeyote atakayekaa humo.

1949:19 Yer 12:5; Ay 9:19; Yer 50:44; Za 89:6-8; 1Sam 17:34; Kut 8:10; 2Nya 20:6“Kama simba anayepanda kutoka vichaka vya Yordani

kuja kwenye nchi ya malisho mengi,

ndivyo nitamfukuza Edomu kutoka nchi yake ghafula.

Ni nani aliye mteule nitakayemweka kwa ajili ya jambo hili?

Ni nani aliye kama mimi,

na ni nani awezaye kunipinga?

Tena ni mchungaji yupi awezaye

kusimama kinyume nami?”

2049:20 Isa 14:27; Yer 50:45; Mao 1:10; Mal 1:3-4; Isa 34:5; Mwa 36:11Kwa hiyo, sikia kile Bwana alichokipanga dhidi ya Edomu,

kile alichokusudia dhidi ya wale waishio Temani:

Aliye mchanga katika kundi ataburutwa mbali;

yeye ataharibu kabisa malisho yao kwa sababu yao.

2149:21 Za 114:7; Eze 31:16; Yer 51:29; Eze 26:18; Yer 50:46; Eze 26:15; 27:28Kwa sauti ya anguko lao, dunia itatetemeka.

Kilio chao kitasikika hadi Bahari ya Shamu.49:21 Kwa Kiebrania ni Bahari ya Mafunjo.

2249:22 Kum 28:49; Hab 1:8; Isa 13:8; Yer 48:40-41; 4:13; Hos 8:1; Nah 3:13; Mwa 36:33Tazama! Tai atapaa juu angani na kuruka chini kwa ghafula,

akitandaza mabawa yake juu ya Bosra.

Katika siku hiyo, mioyo ya mashujaa wa Edomu

itakuwa kama moyo wa mwanamke katika utungu wa kuzaa.

Ujumbe Kuhusu Dameski

2349:23 2Fal 14:28; Mdo 9:2; 1Fal 8:65; Eze 47:16; 2Fal 18:34; Mwa 49:4; Isa 57:20Kuhusu Dameski:

“Hamathi na Arpadi imetahayarika,

kwa kuwa wamesikia habari mbaya.

Wamevunjika moyo na wametaabika

kama bahari iliyochafuka.

2449:24 Yer 13:21Dameski amedhoofika,

amegeuka na kukimbia,

hofu ya ghafula imemkamata sana;

amepatwa na uchungu na maumivu,

maumivu kama ya mwanamke katika utungu wa kuzaa.

25Kwa nini mji ambao unajulikana haujaachwa,

mji ambao ninaupenda?

2649:26 Isa 17:12-14; Yer 50:30; Isa 9:17; 13:18Hakika, vijana wake wanaume wataanguka barabarani;

askari wake wote watanyamazishwa siku hiyo,”

asema Bwana Mwenye Nguvu Zote.

2749:27 Eze 39:6; Amo 1:4; 1Fal 15:18; Yer 21:14; 43:12; Eze 39:6; Mwa 14:15“Nitatia moto kuta za Dameski;

utaangamiza ngome za Ben-Hadadi.”

Ujumbe Kuhusu Kedari Na Hazori

2849:28 Mwa 25:13; Amu 6:3; Isa 21:13; Yer 10:22; Yos 11:1Kuhusu Kedari na falme za Hazori, ambazo Nebukadneza mfalme wa Babeli alizishambulia:

Hili ndilo asemalo Bwana:

“Inuka, ushambulie Kedari

na kuwaangamiza watu wa mashariki.

2949:29 Yer 6:25; 46:5; Za 120:5Hema zao na makundi yao ya kondoo yatachukuliwa;

vibanda vyao vitatwaliwa

pamoja na mali zao zote na ngamia zao.

Watu watawapigia kelele,

‘Hofu kuu iko kila upande!’

3049:30 Amu 6:2; Yos 11:1; Yer 10:22“Kimbieni haraka!

Kaeni kwenye mapango marefu sana, ninyi mkaao Hazori,”

asema Bwana.

“Nebukadneza, mfalme wa Babeli amepanga shauri baya dhidi yenu;

amebuni hila dhidi yenu.

3149:31 Eze 38:11; Hes 23:9; Mik 7:14“Inuka na ulishambulie taifa lililo starehe,

linaloishi kwa kujiamini,”

asema Bwana,

“taifa lisilo na malango wala makomeo;

watu wake huishi peke yao.

3249:32 Yer 9:26; 25:22; Amu 6:5; Yer 13:24Ngamia wao watakuwa nyara,

nayo makundi yao makubwa ya ngʼombe yatatekwa.

Wale walio maeneo ya mbali

nitawatawanya pande zote,

nami nitaleta maafa juu yao

kutoka kila upande,”

asema Bwana.

3349:33 Yer 10:22; 48:9; Isa 13:22; Hos 11:1“Hazori itakuwa makao ya mbweha,

mahali pa ukiwa milele.

Hakuna yeyote atakayeishi humo;

hakuna mtu atakayekaa ndani yake.”

Ujumbe Kuhusu Elamu

3449:34 Mwa 10:22; 2Fal 24:18Hili ndilo neno la Bwana lililomjia nabii Yeremia kuhusu Elamu, mapema katika utawala wa Sedekia mfalme wa Yuda:

3549:35 Za 37:15; Ezr 4:9; Dan 8:2; Isa 22:6Hili ndilo Bwana Mwenye Nguvu Zote asemalo:

“Tazama, nitavunja upinde wa Elamu,

ulio tegemeo la nguvu zao.

3649:36 Dan 11:4Nitaleta pepo nne dhidi ya Elamu

toka pande nne za mbingu,

nitawatawanya katika hizo pande nne,

wala hapatakuwa na taifa

ambalo watu wa Elamu waliofukuzwa

hawatakwenda.

3749:37 Yer 44:2; 30:24; 9:16; Eze 32:24Nitamfadhaisha Elamu mbele ya adui zao,

mbele yao wale wanaotafuta uhai wao;

nitaleta maafa juu yao,

naam, hasira yangu kali,”

asema Bwana.

“Nitawafuatia kwa upanga

mpaka nitakapowamaliza.

38Nitaweka kiti changu cha enzi huko Elamu

na kumwangamiza mfalme wake na maafisa wake,”

asema Bwana.

3949:39 Yer 48:47“Lakini nitarudisha mateka wa Elamu

katika siku zijazo,”

asema Bwana.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 49:1-39

Uthenga Wonena za Aamoni

1Yehova ananena izi:

Amoni,

“Kodi Israeli alibe ana aamuna?

Kapena alibe mlowamʼmalo?

Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi?

Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?

2Koma nthawi ikubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo

ku Raba, likulu la Amoni;

ndipo malo awo opembedzera milungu yawo

adzatenthedwa ndi moto.

Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo

kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,”

akutero Yehova.

3“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika!

Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba!

Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu;

thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga,

chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.

4Chifukwa chiyani mukunyadira

chigwa chanu,

inu anthu osakhulupirika

amene munadalira chuma chanu nʼkumati:

‘Ndani angandithire nkhondo?’

5Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe

zochokera kwa onse amene akuzungulira,”

akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse.

“Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake.

Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.

6“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,”

akutero Yehova.

Uthenga Wonena za Edomu

7Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu:

“Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani?

Kodi anzeru analeka kupereka uphungu?

Kodi nzeru zawo zinatheratu?

8Inu anthu a ku Dedani, thawani,

bwererani ndi kukabisala ku makwalala

chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau

popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.

9Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu

akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

Anthu akuba akanafika usiku

akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

10Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau.

Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo,

kotero kuti sadzathanso kubisala.

Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka.

Palibe wonena kuti,

11‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza.

Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’ ”

12Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho. 13Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”

14Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti,

“Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu!

Konzekerani nkhondo!”

15“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina.

Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.

16Kuopseza kwako kwakunyenga;

kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga

a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri.

Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

17“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha.

Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo

chifukwa cha kuwonongeka kwake.

18Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora,

pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,”

akutero Yehova,

“motero palibe munthu

amene adzakhala mu Edomu.

19“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani

kupita ku malo a msipu wobiriwira,

Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo.

Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine.

Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani?

Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”

20Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova

ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani.

Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo

ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.

21Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera;

kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.

22Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka

nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu

idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

Uthenga Wonena za Damasiko

23Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa:

“Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha

chifukwa amva nkhani yoyipa.

Mitima yawo yagwidwa ndi mantha

ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.

24Anthu a ku Damasiko alefuka.

Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa

chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu.

Ali ndi nkhawa komanso mantha

ngati za mayi pa nthawi yake yochira.

25Mzinda wotchuka

ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!

26Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa;

ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

27“Ndidzatentha malinga a Damasiko;

moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”

Uthenga Wonena za Kedara ndi Hazori

28Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa:

“Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara.

Kawonongeni anthu a kummawako.

29Landani matenti awo ndi nkhosa zawo,

ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo.

Mutengenso ngamira zawo.

Anthu adzafuwula kwa iwo kuti,

‘Kuli zoopsa mbali zonse!’

30“Thawani mofulumira!

Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,”

akutero Yehova.

“Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu;

wakonzekera zoti alimbane nanu.

31“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere,

umene ukukhala mosatekeseka,”

akutero Yehova,

“mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo;

anthu ake amakhala pa okha.

32Ngamira zawo zidzafunkhidwa,

ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa.

Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali.

Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,”

akutero Yehova.

33“Hazori adzasanduka bwinja,

malo okhalamo nkhandwe

mpaka muyaya.

Palibe munthu amene adzayendemo.”

Uthenga Wonena za Elamu

34Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:

35Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu,

umene uli chida chawo champhamvu.

36Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu

kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga;

ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi,

ndipo sipadzakhala dziko

limene anthu a ku Elamu sadzafikako.

37A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo

komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo.

Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga

ndipo adzakhala pa mavuto,”

akutero Yehova.

“Ndidzawapirikitsa ndi lupanga

mpaka nditawatheratu.

38Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu

ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

39“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera

anthu a ku Elamu dziko lawo,”

akutero Yehova.