Ujumbe Kuhusu Wafilisti
147:1 Zek 9:5-7; Sef 2:4-5; Amo 1:6; Mwa 10:14-19Hili ndilo neno la Bwana lililomjia nabii Yeremia kuhusu Wafilisti, kabla Farao hajaishambulia Gaza:
247:2 Isa 8:7; 14:31; 15:3Hili ndilo asemalo Bwana:
“Tazama jinsi maji yanavyoinuka huko kaskazini,
yatakuwa mafuriko yenye nguvu sana.
Yataifurikia nchi na vitu vyote vilivyomo ndani yake,
miji na wale waishio ndani yake.
Watu watapiga kelele;
wote waishio katika nchi wataomboleza
347:3 Yer 46:9; Eze 23:24; Yer 50:43; Eze 7:17; 21:7kwa sauti ya kwato za farasi waendao mbio,
kwa sauti ya magari ya adui
na mngurumo wa magurudumu yake.
Baba hawatageuka kuwasaidia watoto wao,
mikono yao italegea.
447:4 Isa 23:1; Amo 1:9-10; Mwa 10:14-15; Yer 25:22; Yoe 3:4; Kum 2:23; Za 9:2-4Kwa maana siku imewadia
kuwaangamiza Wafilisti wote
na kuwakatilia mbali walionusurika wote
ambao wangeweza kusaidia Tiro na Sidoni.
Bwana anakaribia kuwaangamiza Wafilisti,
mabaki toka pwani za Kaftori.47:4 Kaftori ndio Krete.
547:5 Yer 41:5; Mik 1:16; Yer 25:20; Law 19:28Gaza atanyoa kichwa chake katika kuomboleza,
Ashkeloni atanyamazishwa.
Enyi mabaki kwenye tambarare,
mtajikatakata wenyewe mpaka lini?
647:6 Isa 34:5; Yer 12:12; Eze 21:3; Yer 48:10; 50:35“Mnalia, ‘Aa, upanga wa Bwana,
utaendelea mpaka lini ndipo upumzike?
Rudi ndani ya ala yako;
acha na utulie.’
747:7 Eze 25:15-17Lakini upanga utatuliaje
wakati Bwana ameuamuru,
wakati ameuagiza kuishambulia Ashkeloni
pamoja na pwani yake?”
Uthenga Wonena za Afilisti
1Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
2Yehova akuti,
“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;
adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.
Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,
mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.
Anthu adzafuwula;
anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
3akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,
phokoso la magaleta ake
ndi kulira kwa mikombero yake.
Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;
manja awo adzangoti khoba.
4Pakuti tsiku lafika
lowononga Afilisti onse
ndi kupha onse otsala,
onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.
Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,
otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
5Anthu a ku Gaza ameta mipala;
anthu a ku Asikeloni akhala chete.
Inu otsala a ku chigwa,
mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
6“Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,
kodi udzapumula liti?
Bwerera mʼmalo ako;
ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
7Koma lupangalo lidzapumula bwanji
pamene Yehova walilamulira
kuti lithire nkhondo
Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”